< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
Neya nabhabhwila echijejekanyo kutyo jibheile okusabhwa bhasiga kufwa mwoyo.
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
Naikati, Aliga alio mulamusi umwi, unu atamubhayaga Nyamuanga na atabhalaga bhanu.
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
Aliga alimo omutumba gasi mumusi omwo, namujakoga kwiya ngendo nyamfu, naikati, 'Nsakila na undamule no kunana echibhalo chani no musokwa wani.'
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
Mwanya mwamfu atendaga kumusakila, nawe eishe naika mumwoyo gwae, 'Nolo kutyo anye nitamubhaya Nyamuanga amwi nitakubhala munu,
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
Nawe kwokubha omutumba gasi kanyansha nimulamule nimuyane echibhalo chae asige okugendelela okunyegelela bhuli mwanya.”
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
Latabhugenyi naika ati, 'Mungwe omulamusi oyo atali mulengelesi kutyo kaika.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
Angu Nyamuanga atalilamula abhasolwa bhae bhanu abhamulilila mungeta na mumwisi? angu omwene atalibha mwikomelesha kubhene?
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
Enibhabhwila ati, alibhalamula bhwangu. Nawe Omwana wa Adamu anu alibhaja mbe alisanga elikilisha kuchalo?
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
Niwo nabhabhwila echijejekanyo chinu abhanu abhandi bhanu abhelola kutyo bhali bhalengelesi nibhagaya abhandi,
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
'Bhanubhabhili bhalinyile mwiyekalu okusabhwa. oumwi Mufalisayo oundi omutobhesha wa likodi.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
Omufalisayo nemelegulu nasabhwa emisango jinu omwene,'Nyamuanga enikusima kulwokubha anye nitali lwa bhanu abhandi abhasakusi, abhajimya, abhalomesi, na nitali lwo mutobhesha wo bhushulu unu.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
Anye enisalalila kwiya kabhili ku bhwoyo. Enigwata omugabho gwa likumi kubhinu bhyona bhinu enibhona.'
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
Nawe uliya omutobhesha, emeleguyu alela, nalema okwimusha ameso gae kulwile, nebhuma bhuma muchifubha chae naikati,'Nyamuanga, mfwilwa chigongo anye nili webhibhibhi.'
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
Enibhabwila, omunu unu asubhile ika abhalilwe obhulengelesi kukila uliya kulwokubha bhuli unu kekusha alikeibhwa, nawe bhuli munu unu kekeya alikusibwa.'
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
Abhanu nibhamuletela abhana bhebhwe abhalela, abhone okubhakunyako, abheigisibhwa bhae bhejile bhalola nibhabhaganya.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
Nawe Yesu nabhabhilikila kumwene naikati,'Mubhasige abhana abhalela bhaje kwanye, mutabhaganya. Kulwokubha obhukama bhwa Nyamuanga ni bhwa bhanu lwa bho.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
Mwikilishe, enibhabhwilati, omunu wona wonaunu atabhulamila obhukama bhwa Nyamuanga lwo mwana omulela atalingilamo kata.'
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
Mukulu umwi namubhusha naikati,'awe Omwiigisha wo bhwana nikole kutiki koleleki nilye omwandu gwo bhuanga bhwa kajanende?' (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
Yesu namubhwila ati, 'Kulwaki oumbilikila wo bhwana? Atalio munu unu ali wo bhwana, tali Nyamuanga wenyelela.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
Umenyele ebhilagilo, utalomelega, utetaga, utebhaga, utabheeleshaga, ubhalega esomwana na nyokomwana.
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
Omukulu naikati, 'ago gona nigagwatile okusoka bhulela bhwani.'
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
Yesu ejile ongwa ago namubhwila ati, “Gulio musango gumwi. Nibhusi bhusi ugushe bhinu ulinabhyo ugabhile abhataka niwo ulibha no bhunibhi mulwile niwo uje undubhe.
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
'Nawe omunibhi ejile akongwa ejo nasulumbala muno okubha aliga alimunibhi muno.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
Neya Yesu, namulola kutyo asulumbala muno naikati, 'kukomee abhanibhi okwingila mubhukama bhwa Nyamuanga!
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
Okubha nichangu ingamila okufulumita mwiundu lya insinga kukila omunibhi okwingila mubhukama bhwa Nyamuanga.'
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
Bhanu bhonguhye ago, nibhaikati, 'Kambe jili kutyo niga katula okukila?'
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
Yesu nasubhya naikati, 'Bhinu ebhitamya abhanu Nyamuanga kabhitula.”
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
Petelo naikati, Eswe, chisigile bhuli chinu nchikulubha awe.
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
'Yesu nabhabhwila ati, Nichimali, enibhabhwila ati, atalio omunu unu kasiga inyumba, amwi mugasi, amwi bhamula bhabho, amwi bhebhusi amwi bhana kulwo bhukama bhwa Nyamuanga,
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
Nawe kabhona kwiya kamfu muchalo munu, na jinsiku jinu ejija kabhona obhuanga bhunu bhutakuwao.' (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
Ejile akabhakumanya abho ekumi na bhabhili, nabhabhwila ati, 'Lola echigenda Yelusalemu, na jinu jona jandikilwe na bhalagi ku Mwana wa Adamu ejikumila.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
Kulwokubha kagwatwa nabha mumabhoko ga bhanu bhabhanyamaanga kajimibhwa, nibhamwimatulila, nibhamufubhulila amachwanta.
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
Bhalimusanya jinsanju nibhamwita na kulusiku lwa kasatu alisuluka.'
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
Bhatasombokewe omusango ogwo, gwaliga gwibhisile kubhene, bhatamenyele jinu aikaga.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
Anu Yesu afogelee Yeliko, omunu umwi muofu aliga enyanjile mulubhaju lwa injila nasabhilishaga.
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
Ejile ogwa bhanu bhamfu nibhatulao nasubhyati echo niki.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
Nibhamubhwila ati ni Yesu wa Najaleti nuwe kalabhao.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Mbe omuofu nalila kwo bhulaka bhwa ingulu naikati, 'Yesu omwana wa Daudi, umfwile chigongo. '
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
Bhanu bhaliga nibhalibhata nibhamuganya omuofu oyo, nibhamubhwila ajibhile. Nawe omwene nagendelela okulila kwo bhulaka, Omwana wa Daudi, umfwile chigongo.
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
Yesu nemelegulu nabhalagila nabhabhwila bhamulete. Omuofu ejile amulebhelela, Yesu namubhusha ati,
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
'Owenda nikukole kutiki? Naikati, Latabhugenyi, enenda okulola.'
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
Yesu namubhwila ati, 'mbe lola. Okwikilisha kwao kwakwiulisha.'
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
Ao nao nalola, namulubha Yesu namukusha Nyamuanga. Bhejile bhalola elyo, abhanu bhona nibhamukusha Nyamuanga.

< Luka 18 >