< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
And he spoke a parable to them [to this end], that men ought always [to] pray, and not to faint;
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
Saying, There was in a city a judge, who feared not God, neither regarded man.
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
And there was a widow in that city; and she came to him, saying, Avenge me of my adversary.
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
And he would not for a while: but afterward he said within himself, Though I fear not God, nor regard man;
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
Yet because this widow troubleth me, I will avenge her, lest by her continual coming she weary me.
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
And the Lord said, Hear what the unjust judge saith.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
And will not God avenge his own elect, who cry day and night to him, though he beareth long with them?
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
I tell you that he will avenge them speedily. Nevertheless, when the Son of man cometh, will he find faith on the earth?
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
And he spoke this parable to certain who trusted in themselves that they were righteous, and despised others:
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
Two men went up into the temple to pray; the one a Pharisee, and the other a publican.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
The Pharisee stood and prayed thus with himself, God, I thank thee, that I am not as other men [are], extortioners, unjust, adulterers, or even as this publican.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
I fast twice in the week, I give tithes of all that I possess.
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
And the publican, standing afar off, would not lift up so much as [his] eyes to heaven, but smote upon his breast, saying, God be merciful to me a sinner.
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
I tell you, this man went down to his house justified [rather] than the other: for every one that exalteth himself shall be abased; and he that humbleth himself shall be exalted.
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
And they brought to him also infants, that he would touch them: but when [his] disciples saw [it], they rebuked them.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
But Jesus called them [to him], and said, Suffer little children to come to me, and forbid them not: for of such is the kingdom of God.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
Verily I say to you, Whoever shall not receive the kingdom of God as a little child, shall in no wise enter into it.
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
And a certain ruler asked him, saying, Good Master, what shall I do to inherit eternal life? (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
And Jesus said to him, Why callest thou me good? none [is] good, save one, [that is] God.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
Thou knowest the commandments, Do not commit adultery, Do not kill, Do not steal, Do not bear false witness, Honor thy father and thy mother.
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
And he said, All these have I kept from my youth.
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
Now when Jesus heard these things, he said to him, Yet lackest thou one thing: sell all that thou hast, and distribute to the poor, and thou shalt have treasure in heaven: and come, follow me.
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
And when he heard this, he was very sorrowful: for he was very rich.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
And when Jesus saw that he was very sorrowful, he said, How hardly will they that have riches enter into the kingdom of God!
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
For it is easier for a camel to go through a needle's eye, than for a rich man to enter into the kingdom of God.
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
And they that heard [it], said, Who then can be saved?
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
Then he said, The things which are impossible with men, are possible with God.
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
Then Peter said, Lo, we have left all, and followed thee.
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
And he said to them, Verily I say to you, there is no man that hath left house, or parents, or brethren, or wife, or children for the sake of the kingdom of God,
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
Who shall not receive manifold more in this present time, and in the world to come life everlasting. (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
Then he took the twelve, and said to them, Behold, we go up to Jerusalem, and all things that are written by the prophets concerning the Son of man shall be accomplished.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
For he will be delivered to the Gentiles, and will be mocked, and spitefully treated, and spitted on;
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
And they will scourge [him], and put him to death: and the third day he will rise again.
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
And they understood none of these things: and this saying was hid from them, neither knew they the things which were spoken.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
And it came to pass, that as he had come nigh to Jericho, a certain blind man sat by the way side begging;
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
And hearing the multitude passing by, he asked what it meant.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
And they told him, that Jesus of Nazareth was passing by.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
And he cried, saying, Jesus, [thou] son of David, have mercy on me.
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
And they who went before rebuked him, that he should hold his peace: but he cried so much the more, [Thou] son of David, have mercy on me.
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
And Jesus stood and commanded him to be brought to him: and when he had come near, he asked him,
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
Saying, What wilt thou that I shall do to thee? And he said, Lord, that I may receive my sight.
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
And Jesus said to him, Receive thy sight: thy faith hath saved thee.
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
And immediately he received his sight, and followed him, glorifying God: and all the people, when they saw [it], gave praise to God.

< Luka 18 >