< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
He also spoke a parable to them that they must always pray, and not give up,
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
saying, "There was a judge in a certain city who did not fear God, and did not respect people.
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
A widow was in that city, and she often came to him, saying, 'Give me justice against my adversary.'
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
He would not for a while, but afterward he said to himself, 'Though I neither fear God, nor respect people,
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
yet because this widow bothers me, I will give her justice, or else she will wear me out by her continual coming.'"
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
The Lord said, "Listen to what the unrighteous judge says.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
Won't God avenge his chosen ones, who are crying out to him day and night, and yet he exercises patience with them?
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
I tell you that he will avenge them quickly. Nevertheless, when the Son of Man comes, will he find faith on the earth?"
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
He spoke also this parable to certain people who were convinced of their own righteousness, and who despised all others.
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
"Two men went up into the temple to pray; one was a Pharisee, and the other was a tax collector.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
The Pharisee stood and prayed to himself like this: 'God, I thank you, that I am not like other people, extortioners, unrighteous, adulterers, or even like this tax collector.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
I fast twice a week. I give tithes of all that I get.'
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
But the tax collector, standing far away, would not even lift up his eyes to heaven, but beat his breast, saying, 'God, be merciful to me, a sinner.'
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
I tell you, this man went down to his house justified rather than the other; for everyone who exalts himself will be humbled, but he who humbles himself will be exalted."
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
Now they were also bringing their babies to him, that he might touch them. But when the disciples saw it, they rebuked them.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
Jesus summoned them, saying, "Allow the little children to come to me, and do not hinder them, for the Kingdom of God belongs to such as these.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
Truly, I tell you, whoever does not receive the Kingdom of God like a little child, he will in no way enter into it."
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
A certain ruler asked him, saying, "Good Teacher, what must I do to inherit everlasting life?" (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
Jesus asked him, "Why do you call me good? No one is good, except one—God.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
You know the commandments: 'Do not commit adultery,' 'Do not murder,' 'Do not steal,' 'Do not give false testimony,' 'Honor your father and your mother.'"
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
And he said, "I have kept all these things from my youth up."
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
When Jesus heard it, he said to him, "You still lack one thing. Sell all that you have, and distribute it to the poor. You will have treasure in heaven. Come, follow me."
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
But when he heard these things, he became very sad, for he was very rich.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
And Jesus looked at him and said, "How hard it is for those who have riches to enter into the Kingdom of God.
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
For it is easier for a camel to enter in through a needle's eye, than for a rich person to enter into the Kingdom of God."
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
Those who heard it said, "Then who can be saved?"
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
But he said, "The things which are impossible with man are possible with God."
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
And Peter said, "Look, we have left our own things and followed you."
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
He said to them, "Truly I tell you, there is no one who has left house, or wife, or brothers, or parents, or children, for the Kingdom of God's sake,
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
who will not receive many times more in this time, and in the world to come, everlasting life." (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
He took the twelve aside, and said to them, "Look, we are going up to Jerusalem, and all the things that are written through the prophets concerning the Son of Man will be completed.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
For he will be delivered up to the non-Jews, will be mocked, treated shamefully, and spit on.
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
They will scourge and kill him. On the third day, he will rise again."
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
They understood none of these things. This saying was hidden from them, and they did not understand the things that were said.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
It happened, as he came near Jericho, a certain blind man sat by the road, begging.
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
Hearing a crowd going by, he asked what this meant.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
They told him that Jesus of Nazareth was passing by.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
He called out, "Jesus, Son of David, have mercy on me."
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
Those who led the way rebuked him, that he should be quiet; but he shouted all the more, "Son of David, have mercy on me."
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
Standing still, Jesus commanded him to be brought to him. When he had come near, he asked him,
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
"What do you want me to do?" He said, "Lord, that I may see again."
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
Jesus said to him, "Receive your sight. Your faith has healed you."
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
And immediately he received his sight, and followed him, glorifying God. All the people, when they saw it, praised God.

< Luka 18 >