< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
And then He told them a parable, the point being that one needs to always pray and not lose heart,
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
saying: “There was a judge in a certain town who did not fear God nor regard man.
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
But there was a widow in that town, and she kept coming to him, saying, ‘Get justice for me from my adversary.’
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
And for a while he refused; but afterward he said to himself, ‘Even though I don't fear God nor regard man,
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
yet because this widow keeps bothering me, I will defend her, so that her endless coming doesn't wear me out!’”
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
Then the Lord said: “Hear what the unjust judge said.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
And will not God get justice for His elect who are crying out to Him day and night, indeed being patient with them?
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
I tell you that He will get justice for them quickly. However, when the Son of the Man comes, will He actually find the faith on the earth?”
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
Then He told this parable to some who trusted in themselves that they were righteous, and despised the rest:
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
“Two men went up to the temple to pray, one a Pharisee and the other a tax collector.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
The Pharisee stood and started praying to himself like this: ‘God, I thank you that I am not like all the rest—robbers, unjust, adulterers—or even like this tax collector.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
I fast twice a week; I tithe all that I get.’
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
The tax collector, staying a good ways off, did not even venture to look up to heaven, but started beating on his chest, saying, ‘God, be merciful to me a sinner!’
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
I say to you that this one went back home justified rather than that one; because everyone who exalts himself will be humbled, but he who humbles himself will be exalted.”
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
Then they even started bringing their babies to Him, that He might touch them; but when the disciples saw it, they rebuked them.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
But Jesus summoned them and said: “Allow the little children to come to me, and do not hinder them; because the Kingdom of God is of such.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
I tell you assuredly, whoever does not receive the Kingdom of God the way a little child does will by no means enter it.”
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
A certain ruler asked Him, saying, “Good teacher, what must I do to inherit eternal life?” (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
So Jesus said to him: “Why do you call me good? No one is good except one—God.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
You know the commandments: ‘Do not commit adultery, do not murder, do not steal, do not give false testimony, honor your father and your mother.’”
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
And he said, “All these I have kept from my youth.”
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
Well upon hearing these things Jesus said to him, “You still lack one thing: sell all you have and distribute to the poor, and you will have treasure in heaven; and come, follow me.”
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
But when he heard this he became very sad, because he was extremely rich.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
When Jesus saw that he became sad, He said: “How difficult it is for those who have riches to enter the Kingdom of God!
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
It is actually easier for a camel to go through the eye of a needle than for a rich man to enter the Kingdom of God!”
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
So the hearers said, “Who then can be saved?”
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
And He said, “The things that are impossible with men are possible with God.”
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
Then Peter said, “Notice that we have left all and followed you!”
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
So He said to them, “Assuredly I say to you, there is no one who has left house or parents or brothers or wife or children, for the sake of the Kingdom of God,
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
who will not receive many times more in this present time, and in the age to come eternal life.” (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
Then He took the Twelve aside and said to them: “Take note, we are going up to Jerusalem, and all the things that are written by the prophets concerning the Son of the Man will be fulfilled:
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
He will be betrayed to the Gentiles, and will be mocked and insulted and spit upon,
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
and they will scourge and kill Him. And on the third day He will rise again.”
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
But they understood none of these things; this saying was hidden from them, and they did not know what was being said.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
Then it happened, as He approached Jericho, that a certain blind man was sitting alongside the road begging.
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
Hearing a crowd going by, he asked what it was.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
So they told him that Jesus the Natsorean was passing by.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Well he shouted, saying, “Jesus, Son of David, have mercy on me!”
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
Those who led the way started reproving him, to shut him up; but he kept calling out all the more, “Son of David, have mercy on me!”
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
So Jesus stopped and ordered that he be brought to Him. When he got close He asked him, saying,
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
“What do you want me to do for you?” So he said, “Lord, that I may see again!”
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
Then Jesus said to him: “See again! Your faith has made you well.”
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
And immediately he did! and he followed Him, glorifying God. And all who witnessed it gave praise to God.

< Luka 18 >