< Luka 17 >

1 Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
Or il dit à ses disciples: « Il est inévitable qu'il arrive des scandales, néanmoins malheur à celui par lequel ils arrivent;
2 Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
il lui est plus avantageux qu'on lui mette au col une pierre meulière, et qu'on le précipite dans la mer, que de scandaliser un seul de ces petits.
3 Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
Prenez garde à vous-mêmes: Si ton frère a péché, reprends-le, et s'il se repent, pardonne-lui;
4 Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
et si, sept fois le jour, il a péché contre toi, et que sept fois il revienne vers toi, en disant: « Je me repens, » tu lui pardonneras. »
5 Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
Et les apôtres dirent au seigneur: « Mets en nous plus de foi. »
6 Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
Mais le seigneur dit: « Si vous aviez de la foi, gros comme un grain de moutarde, vous diriez à ce mûrier-ci: « Déracine-toi, et plante-toi dans la mer; » et il vous obéirait.
7 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
Mais lequel de vous, ayant un esclave qui conduit la charrue ou paît les troupeaux, lui dira, à son retour des champs: « Viens vite te mettre à table? »
8 Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
Est-ce qu'au contraire il ne lui dira pas: « Prépare-moi à manger, et ceins-toi pour me servir jusques à ce que j'aie mangé et bu, et après cela, toi, tu mangeras et tu boiras? »
9 Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
Est-ce qu'il sait gré à l'esclave de ce qu'il a fait ce qui lui était prescrit?
10 Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
De même vous aussi, quand vous aurez fait tout ce qui vous a été prescrit, dites: Nous sommes des esclaves inutiles, c'est ce que nous devions faire que nous avons fait. »
11 Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
Et il advint, pendant le voyage vers Jérusalem, qu'il passait entre la Samarie et la Galilée.
12 Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
Et comme il entrait dans un village, vinrent à sa rencontre dix hommes lépreux, qui se levèrent de loin,
13 ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
et ils haussèrent la voix en disant: « Jésus, maître, aie pitié de nous! »
14 Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
Ce que voyant, il leur dit: « Allez vous montrer aux prêtres. » Et il advint, pendant qu'ils s'y rendaient, qu'ils furent guéris.
15 Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
Or l'un d'entre eux voyant qu'il avait été guéri revint glorifiant Dieu à haute voix,
16 Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
et il tomba la face contre terre à ses pieds en lui rendant grâces; et c'était un Samaritain.
17 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
Mais Jésus prenant la parole dit: « Les dix n'ont-ils pas été guéris? Mais les neuf où sont-ils?
18 Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
On ne les a pas vus revenir pour donner gloire à Dieu, sauf cet étranger. »
19 Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
Et il lui dit: « Lève-toi, va-t-en. »
20 Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
Or ayant été interrogé par les pharisiens sur l'époque de la venue du royaume de Dieu, il leur répliqua: « Le royaume de Dieu ne vient pas de manière à être épié,
21 kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
et l'on ne dira point: « Le voici ici, ou là. » Car voici, le royaume de Dieu est au milieu de vous. »
22 Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
Mais il dit aux disciples: « Des jours viendront, où vous désirerez voir un des jours du fils de l'homme, et vous ne le verrez pas;
23 Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
et on vous dira: « Le voici ici, ou le voilà là; » n'y courez pas,
24 Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
car, comme l'éclair flamboyant brille de l'une des extrémités du ciel jusques à l'autre extrémité du ciel, il en sera de même du fils de l'homme;
25 Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
mais il faut d'abord qu'il souffre beaucoup, et qu'il soit rejeté par cette génération.
26 “Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
Et comme il est advenu du temps de Noé, de même adviendra-t-il aussi du temps du fils de l'homme;
27 Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
on mangeait, on buvait, les hommes prenaient des femmes et on donnait aux femmes des maris, jusques au jour où Noé entra dans l'arche; et le déluge survint et les fit tous périr.
28 “Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
De même, comme il advint du temps de Lot, on mangeait, on buvait, on achetait, on vendait, on plantait, on bâtissait,
29 Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
mais le jour où Lot sortit de Sodome, il tomba du ciel une pluie de feu et de soufre et elle les fit tous périr,
30 “Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
de même en sera-t-il le jour où le fils de l'homme sera révélé.
31 Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
En ce jour-là, que celui qui sera sur le toit, et dont les ustensiles sont dans la maison, ne descende point pour les prendre, et que celui qui est aux champs ne revienne pas non plus en arrière:
32 Kumbukirani mkazi wa Loti!
souvenez-vous de la femme de Lot.
33 Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
Mais celui qui aura cherché à rester en possession de sa vie la perdra, tandis que celui qui l'aura perdue la conservera.
34 Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
Je vous le déclare, cette nuit-là deux personnes seront sur un lit, l'une sera prise et l'autre sera laissée.
35 Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
Deux femmes moudront ensemble, l'une sera prise, mais l'autre sera laissée. »
36 Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
[Deux hommes seront dans la campagne, l'un sera pris et l'autre sera laissé.]
37 Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”
Et prenant la parole ils lui dirent: « Où, Seigneur? » Mais il leur dit: « Là où est le corps, c'est là aussi que se rassembleront les aigles. »

< Luka 17 >