< Luka 17 >

1 Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
And he said to his disciples, It is necessary for causes of trouble to come about, but unhappy is he by whom they come.
2 Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
It would be well for him if a great stone was put round his neck and he was dropped into the sea, before he made trouble for any of these little ones.
3 Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
Give attention to yourselves: if your brother does wrong, say a sharp word to him; and if he has sorrow for his sin, let him have forgiveness.
4 Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
And if he does you wrong seven times in a day, and seven times comes to you and says, I have regret for what I have done; let him have forgiveness.
5 Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
And the twelve said to the Lord, Make our faith greater.
6 Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
And the Lord said, If your faith was only as great as a grain of mustard seed, you might say to this tree, Be rooted up and planted in the sea; and it would be done.
7 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
But which of you, having a servant who is ploughing or keeping sheep, will say to him, when he comes in from the field, Come now and be seated and have a meal,
8 Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
Will he not say, Get a meal for me, and make yourself ready and see to my needs till I have had my food and drink; and after that you may have yours?
9 Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
Does he give praise to the servant because he did what was ordered?
10 Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
In the same way, when you have done all the things which are given you to do, say, There is no profit in us, for we have only done what we were ordered to do.
11 Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
And it came about that when they were on the way to Jerusalem he went through Samaria and Galilee.
12 Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
And when he went into a certain small town he came across ten men who were lepers, and they, keeping themselves at a distance,
13 ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
Said, in loud voices, Jesus, Master, have mercy on us.
14 Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
And when he saw them he said, Go, and let the priests see you. And, while they were going, they were made clean.
15 Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
And one of them, when he saw that he was clean, turning back, gave praise to God in a loud voice;
16 Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
And, falling down on his face at the feet of Jesus, he gave the credit to him; and he was a man of Samaria.
17 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
And Jesus said, Were there not ten men who were made clean? where are the nine?
18 Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
Have not any of them come back to give glory to God, but only this one from a strange land?
19 Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
And he said to him, Get up, and go on your way; your faith has made you well.
20 Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
And when the Pharisees put questions to him about when the kingdom of God would come, he gave them an answer and said, The kingdom of God will not come through observation:
21 kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
And men will not say, See, it is here! or, There! for the kingdom of God is among you.
22 Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
And he said to his disciples, The time will come when you will have a great desire to see one of the days of the Son of man, but you will not see it.
23 Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
And if they say to you, See, it is there! or, It is here! do not go away, or go after them.
24 Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
For as in a thunderstorm the bright light is seen from one end of the sky to the other, so will the Son of man be when his time comes.
25 Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
But first, he will have to undergo much and be put on one side by this generation.
26 “Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
And as it was in the days of Noah, so will it be in the day of the Son of man.
27 Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
They were feasting and taking wives and getting married, till the day of the overflowing of the waters, when Noah went into the ark, and they all came to destruction.
28 “Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
In the same way, in the days of Lot; they were feasting and trading, they were planting and building;
29 Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
But on the day when Lot went out of Sodom, fire came down from heaven and destruction came on them all.
30 “Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
So will it be in the day of the revelation of the Son of man.
31 Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
On that day, if anyone is on the roof of the house, and his goods are in the house, let him not go down to take them away; and let him who is in the field not go back to his house.
32 Kumbukirani mkazi wa Loti!
Keep in mind Lot's wife.
33 Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
If anyone makes an attempt to keep his life, it will be taken from him, but if anyone gives up his life, he will keep it.
34 Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
I say to you, In that night there will be two men sleeping in one bed, and one will be taken away and the other let go.
35 Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
Two women will be crushing grain together; one will be taken away and the other let go.
36 Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”
And they, answering him, said, Where, Lord? And he said to them, Where the body is, there will the eagles come together.

< Luka 17 >