< Luka 17 >

1 Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
And he said to his disciples, It is impossible for the stumbling-blocks not to come, but woe to him through whom they come!
2 Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
It is better for him if a donkey-powered millstone were hanged about his neck, and he were thrown into the sea, than that he should cause one of these little ones to stumble.
3 Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
Take heed to yourselves. And if thy brother should sin against thee, rebuke him, and if he repents, forgive him.
4 Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
And if he should sin against thee seven times in the day, and seven times in the day turn back, saying, I repent, thou will forgive him.
5 Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
And the apostles said to the Lord, Increase faith for us.
6 Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
And the Lord said, If ye have faith as a grain of mustard plant, ye would say to this sycamine tree, Be thou uprooted and be planted in the sea, and it would have obeyed you.
7 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
But which of you having a bondman plowing or feeding livestock, who, when he comes in from the field, will straightaway say, After coming near, sit down?
8 Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
Will he not rather say to him, Prepare what I may dine, and having gird thyself, serve me until I eat and drink, and after these things thou will eat and drink?
9 Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
Does he have a favor for that bondman because he did the things that were commanded? I think not.
10 Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
Thus ye also, when ye did all the things that were commanded you, say, We are unprofitable bondmen, because we have done what we are obligated to do.
11 Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
And it came to pass as he went to Jerusalem, that he was passing through the middle of Samaria and Galilee.
12 Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
And as he entered into a certain village, ten leprous men who stood from afar met him.
13 ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
And they raised a voice, saying, Jesus, Master, be merciful to us.
14 Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
And when he saw them, he said to them, After departing, display yourselves to the priests. And it came to pass, during their going they were cleansed.
15 Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
And one of them, when he saw that he was healed, turned back with a great voice glorifying God.
16 Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
And he fell upon his face beside his feet giving him thanks. And he was a Samaritan.
17 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
And having answered, Jesus said, Were not the ten cleansed? But where are the nine?
18 Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
Were there none found who returned to give glory to God, except this foreigner?
19 Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
And he said to him, After rising, go. Thy faith has healed thee.
20 Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
And questioned by the Pharisees when the kingdom of God comes, he answered them and said, The kingdom of God does not come with observation,
21 kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
nor will they say, Lo, here! or, Lo, there! For behold, the kingdom of God is inside of you.
22 Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
And he said to the disciples, The days will come when ye will long to see one of the days of the Son of man, and ye will not see it.
23 Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
And they will say to you, Lo, here! Lo, there! Do not depart, nor pursue.
24 Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
For just as the lightning, its flashing from under the sky to under the sky, illuminates, so will the Son of man be in his day.
25 Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
But first it is necessary for him to suffer many things and be rejected from this generation.
26 “Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
And just as it happened in the days of Noah, so also it will be in the days of the Son of man.
27 Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
They ate, they drank, they married, they were given in marriage, until the day that Noah entered into the ark, and the flood came and destroyed them all.
28 “Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
And likewise as it happened in the days of Lot. They ate, they drank, they bought, they sold, they planted, they built.
29 Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
But in that day Lot went out from Sodom he rained fire and brimstone from the sky, and destroyed them all.
30 “Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
It will be according to these things in that day the Son of man is revealed.
31 Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
In that day, he who will be on the housetop, and his vessels in the house, let him not go down to take them up. And let him who is in the field likewise not return for the things behind.
32 Kumbukirani mkazi wa Loti!
Remember Lot's wife.
33 Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
Whoever will seek to save his life will lose it, and whoever will lose it will keep it alive.
34 Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
I say to you, in that night there will be two in one bed. The one man will be taken, and the other man will be left.
35 Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
Two will be grinding together. The one woman will be taken, and the other woman will be left.
36 Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
This verse is not in the majority of the Greek manuscripts.
37 Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”
And having answered, they say to him, Where, Lord? And he said to them, Where the body is, there the vultures will be gathered together.

< Luka 17 >