< Luka 16 >

1 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
Jesu naye cha wamba valutwana vakwe, “Kuvena mukwame wa muhumi avena muyendisi wa misevezi yakwe, mi kuva vihiwa kuti muyendisi wa misevezi ya kwe u kwete ku mu sinyeza iluwo lya kwe.
2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
Cwale muhumi cha musupa mi chati kwali, 'Zintu nzi zi nizule kuamana niwe? U nihe chakwizula za musevezi wako, ili kuti kese uzwile havusu ni vuyendisi.'
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
Muyendisi cha liwambila, 'chiniswanela kupanga chinzi, hakuva mukulwana choni zwisa musevezi? Ka nina ziho za kusha, mi niswava ku mukumbila.
4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
Nizi chini swanela ku tenda, ili kuti china zwiswa ha musevezi wangu wa vu yendisi, bantu va ni tambule mu mazuvo avo.
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
Cwale muyendisi chasupa zumwi ni zumwi ya vaali kukolota si mwin'a kwe, mi cha vuza we ntazi, 'U kolota vukayi simwin'a ngu? 6.
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
Cha wamba, 'Ni kolota makumi ekumi ya byima bya mafuta e oli.' Mi chati kwali, muhinde zikoloti zenu, mwikale kapili, mi muñole makumi akwana yanza.'
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
Cwale muyendisi cha wamba ku zumwi, 'mi vukayi yo kolota?' Chati, 'makumi ekumi a vuyima bwa vuroto.' Chati kwali, 'hinde chikoloti mi u ñole makumi akwana yenza ni to tatwe.
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
Simwin'a kwe cha lumba chikombwa chi sa sepahali kakuti ava sevezi mu kusasepahala. Vaana ve fasi ilyi vena ahulu mukusa sepahala chiva kwete kuseveza ni vantu vavo hita vaana vena mu liseli. (aiōn g165)
9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
Ni wamba kwenu, mutende valikani che nzila za mashenyi a sa sepahali, kutendela kuti chi bwamana, va woole ku mitambula mu mazuvo asamani. (aiōnios g166)
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
Iye yo sepahala ku zinini mwa sepahale ni ku zikando, mi niya sasepahali mu zinini kasepahali mu zikando.
11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
Haiva kena u va sepahali ku ku sevelisa mashelenyi a fosahele, nje ni yeta kusepe mu chifumu che niti?
12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
Mi haiva kawini ku sepahala mu kusevelisa mashelinyi a vamwi, njeni ya sa kuhe mashelenyi ako u mwine?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
Ka kwina muhikana yo wola ku seveleza malena vo vele, kusicwalo mwa toye umwi ni kusaka zumwi, mwa kumalele umwi kapa kunyefula zumwi. Ko woli kuseveleza Ereeza ni chifumu.
14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
Hanu Vafalisi, va vali kusaka hahulu mashelenyi, va va zuwi zoose inzi, mi chi va museka.
15 Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
Mi chati kuvali, “Mu li shiyamisa mu menso a vantu, kono Ireeza wizi ikulo zenu. Zina zivoneka vulotu mumeeso a vantu kwe Reeza zi fosahele.
16 “Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
Mulao ni vupolofita ziva kuseveza kuleta Johani hasika. Ku zwa iyo nako, inzwii lya muvuso we Reeza li va kutazwa, mi zumwi ni zumwi ava sa kuhambiliza inzila za vo mwateni.
17 Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
Kono kuhuva kwiwulu ni hansi zi mane isi kuti intaku imwi ya mulao sanzi ivi ni mutendo.
18 “Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
Yense yo kauhana ni mwanakazi wakwe ni kusesa zumwi u chita vushahi, mi yo sesa mwanakazi ya va kanwa kwa mwihyabwe naye utenda vushahi.
19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
Linu ku vena mukwame ya va humite, ya va kuzwete zi zwato ze pulipera ni line mi mazuva onse ava kulikola chifumu cha kwe.
20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
Mukumbizi ava kusumpwa Lazaro ava lele hamulyango, avali kwizwile zilavi muvili wonse.
21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
Mi avali kuhala kulya vungululwa vu vali kuwa hentafule ya muhumi, mi kuzwaho, vambwa va vali kukomba zilavi zakwe.
22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
Ku vezi kuva kuti mukumbizi chafwa, mi avezi ku hindwa mangeloi ku mutwala kwimbali ya Abrahama. Muhumi naye chafwa mi cha zikwa,
23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
mi mu lyangalilo, na sukulukite, cha kotola menso mi cha vona Abrahama nena vutavule ni Lazaro nena ha chizuva chakwe. (Hadēs g86)
24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
Cha lila mi chati, Tayo Abrahama, uni zuwile kusasama, mi tumine Lazaro, kuti a tompe munwe wakwe mu menzi mi nja tontoze lulimi lwangu, kakuti ni hile maswe mowu mulilo.
25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
Kono Abrahama chati, 'mwan'a ngu, u hupule kuti muvuhalo bwako uva tambuli zako zilotu, mi Lazaro mwinzila iswana ava ku tavela zintu zivilala, kono hanu cho kwete kusengwa sengwa kunu, mi iwe wina mumanyando.
26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
Mi kuzwaho zintu zoose, chigodi chikando chivavi mukati, ili kuti avo vasaka kuluta kuzwa kunu kwiza kwako kese vawole, mi kakwina yese awole kuzwa uko kwiza kwetu.'
27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
Muhumi chati, ni ku kumbila, Tayo Abrahama, kuti umuni tumine kuzuvo ya tayo
28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
kakuti nina vanche vava swisu va tenda yanza - kutendela kuti akava kalimele, kutiya kuti navo chiveza mwe chi chivaka cha masukuluka.'
29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
Kono Abrahama chati, veena Mushe ni vapolofita; mu vasiye va tekeleze ku vali.'
30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
Muhumi che tava chati, 'Nanta, Tayo Abrahama, kono haiva zumwi na yenda kuvali kuvafwile, mu va lichiule.'
31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”
Kono Abrahama chati kwali, 'Haiba ni vasa tekelezi kwa Mushe ni vapolofita, kese vaole kuzumina ni haiva vafwile kuti va vuke.'”

< Luka 16 >