< Luka 16 >

1 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
Yesu nabhabhwila lindi abheigisibhwa bhaye ati, “Aliga alio omunu umwi mutagiri ali nomunu emelegululiye emilimu jaye, nibhamubhwila ati omukosi wao unu kalasa-lasa imali yao.
2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
Kulwejo tagiri namubhilikila, namubhwila ati, “Nimisangoki jinu enungwa ingulu yao? Nuumbalile obhukumi bhwe emilimu jao, kulwokubha utachasubha kwimelegululila emilimu lindi.”
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
Omukosi we emilimu neyaikila mumwoyo gwaye, 'lata bhugenyi wani kansoshako kumilimu jokwimelegulila emilimu, nikole kutiki? Nitali namanaga gokulima, nokusabhilisha eniswala.
4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
Mbe enimenya gunu nilakola koleleki labha nikasosibhwako kumilimu abhanu bhankumililega mumisi jebhwe.'
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
Kulwejo omukosi wemilimu nabhilikila bhanu bhaliga nibhatongwa na lata bhugenyi waye. Nabhwila owokwamba ati, 'omukulu wani kakutonga bhilinga?
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
Nasubhya ati, 'ndengo egana eja amafuta' namubhwila ati, 'nugege olwandiko lwao wiyanje bhwangu wandike makumi gatanu.'
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
Neya nabhwila oundi, 'kawe outongwa elinga?' naika ati, 'bhilengo egana ebhya jishano ja ingano.' Namubhwila ati, 'gega olwandiko lwao wandike makumi munana.'
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
Omumula uliya omunibhi namukuya omukosi wobhuyaga lwakutyo akolele kwo obhwenge. Kulwokubha abhana bhe echalo bhana obhwenge bhwafu na abhakola emilimu kwo bhwenge na abhanu bhanu bhali kulubhala lwebhwe kukila kutyo bhali abhana bho obhwelu. (aiōn g165)
9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
Mbe enibhabhwila mwikolele abhasani okusoka mubhinu bhyo obhunyamuke koleleki ebhinu bhikawao bhabhakumilile mubhwikalo bhunu bhutakuwao. (aiōnios g166)
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
Owakisi mwibhika kuchinu chitoto muno kabhaga wekisi okubhika nolwo chinu chinene. Na unu kasakula echitoto nolwo echinene ona kasakula.
11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
Labha emwe mutabheye bhakisi kubhinu bhyo obhunyamuke niga unu alibhayana okubhika ebhinu bhye echimali?
12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
Ka labha mutabheye bhakisi kubhinu bhyo undi niga unu alibhayana imali yemwe abhene?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
Atalio omunu unu katula okukolela bhese Bhugenyi bhabhili, kulwokubha kafururukwa no oumwi na nenda oundi, lugendo kagwatana na unu nokugaya oundi. Mutakutula okukolela Nyamuanga ne ebhinu.
14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
Mbe Abhafarisayo bhanu bhaliga nibhenda jimpilya, nibhongwa ejo jona na nibhamujimya.
15 Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
Yesu nabhabhwila ati, “Emwe nemwe omwigegela obhulengelesi imbele ya abhanu, nawe Nyamuanga kamenya emyoyo jemwe. Kulwokubha linu limenyekene kubhanu elibhaga efururusho ku Nyamuanga.
16 “Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
Mbe ebhilagilo na abhalagi bhyaliga bhilio okukingila Yoana naja. Okwambila akatungu ako, Omusango ogwo bhwana ogwo obhukama bhwa Nyamuanga ogulasibhwa, na bhuli munu kalegeja okwiingisha kwa amanaga.
17 Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
Jolobhele olwire na insi okuwao nawe inyuguta imwi eye echilagilo okubhulao.
18 “Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
Bhuli munu unu kasigana no mugasi waye natwala oundi kalomela, naunu katwala omugasi unu asigilwe no mulume waye kalomela.
19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
Mbe aliga alio omunu umwi alimunibhi nafwalaga jingubho ja irangi ya amajambarau ejobhugusi bhunene, bhuli siku nakondelesibhwa no obhwafu bhwo ubhutagiri bhwaye.
20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
Alio no omunu umwi lisinanlyaye Lazaro, alimutaka ne ebhilondo, neyanjaga kumulyango gwo omunibhi oyo.
21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
Lazaro esigomberaga okwiguta ganu galagalaga okusoka kumeja yo omunibhi jimbwa nijija okumulamba ebhilonda bhaye.
22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
Mbe ejile omutaka afwa nagegwa na bhamalaika nibhamukingya muchifubha cha Ibraimu. Omunibhi uliya ona nafwa nasikwa.
23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
Munyombe ao aliga alimunyako, nalalamila nalola Ibraimu alikula na Lazaro alimuchifubha chaye. (Hadēs g86)
24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
Nalola naika ati, 'Lata Ibraimu, nuumfwile chigongo utume Lazaro enike insonde yechala chaye mumanji anyilishe olulimi lwwni; kulwokubha eninyasibhwa mumulilo gunu.
25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
Nawe Ibraimu naika ati, 'Mwana wani ichuka lwa kutyo mubhulame bhwao walamiye agekisi, ka Lazaro nabhona amabhibhi. Nawe olyanu alyanu kafung'amibhwa kawe ounyasibhwa.
26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
Ingulu ya jona, liteweo elyobho enene na elela agati yeswe, koleleki bhanu abhenda okusoka enu okuja kwimwe bhasige okutula, nolwo abhanu bhe ewemwe bhatajokwambuka okuja kwiswe.'
27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
Omunibhi oyo naika ati, 'Enikusabhwa lata Ibraimu, utume Lazaro ika owasu kulata.
28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
Kulwokubha nina bhamula bhasu bhatanu koleleki abhakishe, enubhaya abhene ona bhasiga kukinga munyako anu nili.'
29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
Nawe Ibraimu naika ati, 'bhali na Musa na abhalagi. Bhasigela bhabhategeleshe abho.
30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
Omunibhi naika ati, 'Pai, Lata Ibraimu, omunu akasoka mubhafuye nabhakingako abhata ebhibhi.'
31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”
Nawe Ibraimu namubhwila ati, 'bhakabhula okungwa Musa na abhalagi bhatakutula okungwa nolwo omunu akasoka mubhafuye.'”

< Luka 16 >