< Luka 16 >

1 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
And he spoke a parable to his disciples. There was a certain rich man, who had a steward; and accusations were brought to him of him, that he squandered his property.
2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
And his lord called him, and said to him: What is this that I hear of thee? Render to me an account of thy stewardship; for thou canst no longer be my steward.
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
And the steward said with himself: What shall I do, since my lord is about to take from me the stewardship? To dig, I am unable; and to become a beggar, I am ashamed.
4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
I know what to do, that, when I am put out of the stewardship, they may receive me to their houses.
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
And he called each one of his lord's debtors; and he said to the first, How much owest thou to my lord?
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
And he said to him, One hundred measures of oil. And he said to him: Take thy bill, and sit down quickly, and write Fifty measures.
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
And he said to another: And how much owest thou to my lord? And he said to him, One hundred cors of wheat. And he said to him: Take thy bill, and sit down, and write Eighty cors.
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
And our Lord praised the unrighteous steward, for having acted sagaciously: for the children of this world are more sagacious than the children of light, in this their generation. (aiōn g165)
9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
And I also say to you: Make to yourselves friends, with this unrighteous mammon; so that when it is finished, they may receive you to their everlasting tabernacles. (aiōnios g166)
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
He that is faithful in the little, is also faithful in the much; and he that is unjust in the little, is also unjust in the much.
11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
If therefore ye have not been faithful in the unrighteous mammon, who will intrust to you the reality?
12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
And if ye have not been found faithful in that which is not yours, who will give to you that which is yours?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
There is no servant, who can serve two lords. For, either he will hate the one and love the other, or he will honor the one and despise the other. Ye cannot serve God and mammon.
14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
And the Pharisees, when they heard all these things, because they loved money, derided him.
15 Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
And Jesus said to them: Ye are such as justify yourselves before men; but God knoweth your heart: for that which is exalted among men, is abominable before God.
16 “Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
The law and the prophets were until John: since then, the kingdom of God is proclaimed, and every one presseth it to enter in.
17 Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
And it is easier for heaven and earth to pass away, than for one letter to pass from the law.
18 “Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
Whoever putteth away his wife, and taketh another, committeth adultery; and whoever taketh her that is put away, committeth adultery.
19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
And there was a certain rich man, who was clothed in fine linen and scarlet, and passed every day in splendid luxury.
20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
And there was a certain poor man, whose name was Lazarus; and he was laid at the gate of the rich man, smitten with ulcers.
21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
And he desired to fill his belly with the fragments that fell from the rich man's table: and the dogs also came and licked his ulcers.
22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
And so it was, that the poor man died; and angels transported him to Abraham's bosom. The rich man also died, and was buried.
23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
And being tormented in hell, he raised his eyes from afar off, and saw Abraham, and Lazarus in his bosom. (Hadēs g86)
24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
And he called with a loud voice, and said: Abraham, my father, have pity on me; and send Lazarus, that he may dip the tip of his finger in water, and moisten my tongue; for, lo, I am tormented in this flame.
25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
And Abraham said to him: My son, remember, that thou receivedst thy good things in thy lifetime, and Lazarus his evil things: and now, behold he is here at rest, and thou art tormented.
26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
And with all these, there is a great barrier between us and you; so that they who would pass from here to you, cannot; neither can they pass from there to us
27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
He said to him: I pray thee, therefore, my father, that thou wouldst send him to my father's house;
28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
for I have five brothers; that he may go and protest to them; lest they also come to this place of torment.
29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
Abraham said to him: They have Moses and the prophets, let them hear them.
30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
But he said to him: No, my father Abraham: but if one shall go to them from the dead, they will repent.
31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”
Abraham said to him: If they hear not Moses and the prophets, they will not believe, though one should rise from the dead.

< Luka 16 >