< Luka 15 >

1 Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
Issi gallas qaraxa qanxeyssatinne nagaranchchoti Yesuusa timirttiya si7anaw iya yuushuwan shiiqidosona.
2 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
Shin Farisaawetinne higge asttamaareti, “Hayssi uray nagaranchchota shiishidi ekkees, enttara issife mees” yaagidi zuuzummidosona.
3 Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
Yesuusi yaagidi hayssa leemiso enttaw odis;
4 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
“Hintte giddofe issuwas xeetu dorssati de7iyabaa gidikko enttafe issoy dhayikko uddufun tammanne uddufunata bazzon aggidi dhayoyssa demmana gakkanaw koyonnay oonee?
5 Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
Demmida wode ufayttidi ba gannan tookkidi,
6 ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
ba soo simmees. Ba laggettanne shoorota issife xeegidi, ‘Dhayida ta dorssaa demmas, taara issife ufayttite’ yaagees.
7 Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
Hessadakka, maaroti koshshonna uddufun tammanne uddufun xillotappe aathidi maarotan geliya issi nagaranchchuwa gaason salon gita ufayssi gidees.
8 “Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
“Woykko tammu biri de7iya issi maccasiya tammaafe issiya dhayikko demmana gakkanaw xomppe oythada keethaa pittada mintha koyonnara oonee?
9 Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
Demmida wode ba laggettanne ba shoorota xeegada ‘Dhayida ta issi bira demmida gisho taara wolla ufayttite’ yaagawusu.
10 Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
Si7ite, hessa mela issi maarotethan geliya nagaranchchuwan Xoossaa kiitanchchota sinthan ufayssi gidees” yaagis.
11 Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
Zaaridi Yesuusi, “Issi uraas nam77u nayti de7oosona.
12 Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
Enttafe kaalo na7ay ba aawakko, ‘Ta aawaw, ne shaluwappe ta gishuwa taw imma’ yaagis. Aaway ba shaluwa ba naytas shaakkis.
13 “Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
Guutha gallasappe guye kaalo na7ay ba gishuwa ubbaa qachchi ekkidi haaho biitta bis. Yan alttacan shaluwa toochchidi onggis.
14 Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
I baw de7iyaba ubbaa wurssidaappe guye he biitta ubban mino koshi keyin metootis.
15 Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
Hessa gisho, he biittaa asaappe issuwa soo gaata gelis. Uray iya guduntho heemmana mela ba moothaa yeddis.
16 Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
Gudunthoti miya harquwafe maanaw amottis, shin iyokka iyaw immiya asi benttibeenna.
17 “Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
Wozani simmin, ‘Aappun ta aawa aylletas kathi wora wodhdhin ta hayssan koshara hayqqanaw gakkadina?’
18 Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
Denddada ta aawakko bada, ‘Ta aawaw, salon Xoossaa, sa7an nena qohas.
19 Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
Hizappe ne na7a geetettada xeegettanaw taw bessonna gisho, ne son de7iya aylletappe issuwada tana payda’ yaagana” yaagis.
20 Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
Hessa gisho, denddidi ba aawakko bis. “Hanoshin, I buroo haahon de7ishin aaway qadhettidi, iyaakko woxxi bidi idimmidi yeeris.
21 “Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
Na7aykka, ‘Ta aawaw salon Xoossaa, sa7an nena ta qohas. Hizappe ne na7a geetettada xeegettanaw bessike’ yaagis.
22 “Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
“Iya aaway aylleta xeegidi, ‘Ellesidi ubbaafe lo77o gidida ma7o ehidi iya mayzite; iya biradhdhen sagaayo, iya tohuwan caamma aathite.
23 Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
Modhdho gatarmentho ehidi shukkite, moos, ufayttoos.
24 Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
Ta na7ay hayssi hayqqis, shin ha77i paxis; dhays, shin benttis’ yaagis. Hessafe guye, ufayetethi oykkidosona.
25 “Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
“He wode bayra na7ay goshsha gaden de7ees. Yaappe yishe soo matishin yethinne gufa girssi si7is.
26 Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
I, aylletappe issuwa xeegidi haniyabay aybeekko eranaw oychchis.
27 Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
Aylley, ‘Ne ishay saro yida gisho ne aaway modhdho gatarmentho iyaw shukkis’ yaagis.
28 “Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
“Bayra ishay yilotidi soo gelanawukka koyibeenna. Aaway kare keyidi soo gelana mela iya woossis.
29 Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
Shin I ba aawakko, ‘Hekko, hayssa mela laythi ta new aylletada ne kiitaappe issuwaka pacisonna new kiitettin ta ta laggetara ufayttana mela hari attoshin issi laaqa deeshe immabaakka.
30 Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
Hanoshin, hayssi ne na7ay ne shaluwa laymatara doomisidi yin modhdho gatarmentho shukkadasa’” yaagis.
31 Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
“Aawaykka, ‘Ta na7aw, neeni ubba wode taara de7aasa, tabay ubbay neessa.
32 Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”
Hayssi ne ishay hayqqis, shin paxis; dhays, shin benttis. Hessa gisho, daro ufayttanaw bessees’ yaagana” yaagis.

< Luka 15 >