< Luka 15 >

1 Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
Then resorted vnto him all the Publicanes and sinners, to heare him.
2 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
Therefore the Pharises and Scribes murmured, saying, Hee receiueth sinners, and eateth with them.
3 Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
Then spake hee this parable to them, saying,
4 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
What man of you hauing an hundreth sheepe, if hee lose one of them, doeth not leaue ninetie and nine in the wildernesse, and goe after that which is lost, vntill he finde it?
5 Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
And when he hath found it, he laieth it on his shoulders with ioye.
6 ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
And when he commeth home, he calleth together his friendes and neighbours, saying vnto them, Reioyce with mee: for I haue founde my sheepe which was lost.
7 Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
I say vnto you, that likewise ioy shall be in heauen for one sinner that conuerteth, more then for ninetie and nine iust men, which neede none amendment of life.
8 “Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
Either what woman hauing ten groates, if she lose one groate, doth not light a candle, and sweepe the house, and seeke diligently till shee finde it?
9 Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
And when shee hath found it, shee calleth her friendes, and neighbours, saying, Reioyce with me: for I haue found the groate which I had lost.
10 Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
Likewise I say vnto you, there is ioy in the presence of the Angels of God, for one sinner that conuerteth.
11 Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
He sayde moreouer, A certaine man had two sonnes.
12 Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
And the yonger of them sayde to his father, Father, giue mee the portion of the goods that falleth to mee. So he deuided vnto them his substance.
13 “Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
So not many daies after, when the yonger sonne had gathered all together, hee tooke his iourney into a farre countrey, and there hee wasted his goods with riotous liuing.
14 Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
Nowe when hee had spent all, there arose a great dearth throughout that land, and he began to be in necessitie.
15 Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
Then hee went and claue to a citizen of that conntrey, and hee sent him to his farme, to feede swine.
16 Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
And hee would faine haue filled his bellie with the huskes, that the swine ate: but no man gaue them him.
17 “Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
Then he came to him selfe, and said, Howe many hired seruaunts at my fathers haue bread ynough, and I die for hunger?
18 Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
I wil rise and goe to my father, and say vnto him, Father, I haue sinned against heaue, and before thee,
19 Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
And am no more worthy to be called thy sonne: make me as one of thy hired seruants.
20 Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
So hee arose and came to his father, and when hee was yet a great way off, his father sawe him, and had compassion, and ranne and fell on his necke, and kissed him.
21 “Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
And the sonne sayde vnto him, Father, I haue sinned against heauen, and before thee, and am no more worthie to be called thy sonne.
22 “Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
Then the father said to his seruaunts, Bring foorth the best robe, and put it on him, and put a ring on his hand, and shoes on his feete,
23 Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
And bring the fat calfe, and kill him, and let vs eate, and be merie:
24 Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
For this my sonne was dead, and is aliue againe: and he was lost, but he is found. And they began to be merie.
25 “Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
Nowe the elder brother was in the fielde, and when he came and drewe neere to the house, he heard melodie, and dauncing,
26 Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
And called one of his seruaunts, and asked what those things meant.
27 Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
And hee sayde vnto him, Thy brother is come, and thy father hath killed the fatte calfe, because he hath receiued him safe and sound.
28 “Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
Then he was angry, and would not goe in: therefore came his father out and entreated him.
29 Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
But he answered and said to his father, Loe, these many yeeres haue I done thee seruice, neither brake I at any time thy commadement, and yet thou neuer gauest mee a kidde that I might make merie with my friends.
30 Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
But when this thy sonne was come, which hath deuoured thy good with harlots, thou hast for his sake killed the fat calfe.
31 Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
And he said vnto him, Sonne, thou art euer with me, and al that I haue, is thine.
32 Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”
It was meete that we shoulde make merie, and be glad: for this thy brother was dead, and is aliue againe: and hee was lost, but he is found.

< Luka 15 >