< Luka 15 >

1 Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
Men alle Toldere og Syndere holdt sig nær til ham for at høre ham.
2 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
Og baade Farisæerne og de skriftkloge knurrede og sagde: „Denne tager imod Syndere og spiser med dem.‟
3 Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
Men han talte denne Lignelse til dem og sagde:
4 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
„Hvilket Menneske af eder, som har hundrede Faar og har mistet eet af dem, forlader ikke de ni og halvfemsindstyve i Ørkenen og gaar ud efter det, han har mistet, indtil han finder det?
5 Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
Og naar han har fundet det, lægger han det paa sine Skuldre med Glæde.
6 ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
Og naar han kommer hjem, sammenkalder han sine Venner og Naboer og siger til dem: Glæder eder med mig; thi jeg har fundet mit Faar, som jeg havde mistet.
7 Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
Jeg siger eder: Saaledes skal der være Glæde i Himmelen over een Synder, som omvender sig, mere end over ni og halvfemsindstyve retfærdige, som ikke trænge til Omvendelse.
8 “Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
Eller hvilken Kvinde, som har ti Drakmer og taber een Drakme, tænder ikke Lys og fejer Huset og søger med Flid, indtil hun finder den?
9 Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
Og naar hun har fundet den, sammenkalder hun sine Veninder og Naboersker og siger: Glæder eder med mig; thi jeg har fundet den Drakme, som jeg havde tabt.
10 Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
Saaledes, siger jeg eder, bliver der Glæde hos Guds Engle over een Synder, som omvender sig.‟
11 Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
Men han sagde: „En Mand havde to Sønner.
12 Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
Og den yngste af dem sagde til Faderen: Fader! giv mig den Del af Formuen, som tilfalder mig. Og han skiftede Godset imellem dem.
13 “Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
Og ikke mange Dage derefter samlede den yngste Søn alt sit og drog udenlands til et fjernt Land og ødte der sin Formue i et ryggesløst Levned.
14 Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
Men da han havde sat alt til, blev der en svær Hungersnød i det samme Land; og han begyndte at lide Mangel.
15 Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
Og han gik hen og holdt sig til en af Borgerne der i Landet, og denne sendte ham ud paa sine Marker for at vogte Svin.
16 Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
Og han attraaede at fylde sin Bug med de Bønner, som Svinene aade; og ingen gav ham noget.
17 “Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
Men han gik i sig selv og sagde: Hvor mange Daglejere hos min Fader have ikke Brød i Overflødighed? men jeg omkommer her af Hunger.
18 Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
Jeg vil staa op og gaa til min Fader og sige til ham: Fader! jeg har syndet imod Himmelen og over for dig,
19 Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
jeg er ikke længer værd at kaldes din Søn, gør mig som en af dine Daglejere!
20 Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
Og han stod op og kom til sin Fader. Men da han endnu var langt borte, saa hans Fader ham og ynkedes inderligt, og han løb til og faldt ham om Halsen og kyssede ham.
21 “Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
Men Sønnen sagde til ham: Fader! jeg har syndet imod Himmelen og over for dig, jeg er ikke længer værd at kaldes din Søn.
22 “Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
Men Faderen sagde til sine Tjenere: Henter det bedste Klædebon frem, og ifører ham det, og giver ham en Ring paa hans Haand og Sko paa Fødderne;
23 Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
og henter Fedekalven og slagter den, og lader os spise og være lystige!
24 Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
Thi denne min Søn var død og er bleven levende igen, han var fortabt og er funden. Og de begyndte at være lystige!
25 “Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
Men hans ældste Søn var paa Marken, og da han kom og nærmede sig Huset, hørte han Musik og Dans.
26 Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
Og han kaldte en af Karlene til sig og spurgte, hvad dette var?
27 Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
Men han sagde til ham: Din Broder er kommen, og din Fader har slagtet Fedekalven, fordi han har faaet ham sund igen.
28 “Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
Men han blev vred og vilde ikke gaa ind. Men hans Fader gik ud og bad ham.
29 Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
Men han svarede og sagde til Faderen: Se, saa mange Aar har jeg tjent dig, og aldrig har jeg overtraadt noget af dine Bud, og du har aldrig givet mig et Kid, for at jeg kunde være lystig med mine Venner.
30 Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
Men da denne din Søn kom, som har fortæret dit Gods med Skøger, slagtede du Fedekalven til ham.
31 Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
Men han sagde til ham: Barn! du er altid hos mig, og alt mit er dit.
32 Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”
Men man burde være lystig og glæde sig, fordi denne din Broder var død og er bleven levende og var fortabt og er funden.‟

< Luka 15 >