< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
Efter månge hafva tagit sig före att beskrifva de ting, som ibland oss aldravissast äro;
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
Såsom de oss sagt hafva, som af begynnelsen det med sin ögon sågo, och sjelfve en del voro af det de sade;
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
Syntes ock mig, sedan jag af begynnelsen all ting granneliga utfrågat hafver, ordenteligen skrifva dig till, min gode Theophile;
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
Att du må förfara vissa sanningen om de stycker, der du om undervister äst.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
Uti Herodis, Judee Konungs, tid, var en Prest, utaf Abie skifte, benämnd Zacharias; och hans hustru, af Aarons döttrar, benämnd Elisabet.
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
De voro både rättfärdige för Gud, vandrande i all Herrans bud och stadgar ostraffeliga.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
Och de hade inga barn; ty Elisabet var ofruktsam, och både voro de framlidne i sin ålder.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
Så begaf det sig, då han i sitt skifte skulle hålla sitt Prestaämbete för Gudi,
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
Efter Presterskapets sed, och det föll på honom, att han skulle upptända rökelse, gick han in i Herrans tempel;
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
Och allt folket var utantill, och bad, så länge rökelsen skedde.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
Så syntes honom Herrans Ängel, ståndandes på högra sidon vid rökaltaret.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
Och Zacharias vardt förskräckt, då han såg honom, och en räddhåge föll öfver honom.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
Så sade Ängelen till honom: Var icke förfärad, Zacharia; ty din bön är hörd, och din hustru Elisabet skall föda dig en son, hvilkens namn du skall kalla Johannes.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
Och dig skall varda glädje och fröjd; och månge skola fröjdas af hans födelse;
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
Ty han skall varda stor för Herranom; vin och starka drycker skall han icke dricka; och skall straxt i moderlifvet uppfylld varda med den Helga Anda;
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
Och han skall omvända många af Israels barn till Herran, deras Gud.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
Och han skall gå för honom, med Elie anda och kraft, till att omvända fädernas hjerta till barnen, och de ohöriga till de rättfärdigas snällhet; och göra Herranom ett beredt folk.
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
Då sade Zacharias till Ängelen: Hvaraf skall jag detta veta? Ty jag är gammal, och min hustru är framliden i åldren.
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
Ängelen svarade, och sade till honom: Jag är Gabriel, som står i Guds åsyn, och är utsänd till att tala dig till, och båda dig denna goda tidenden.
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
Och si, du skall varda mållös, och skall intet kunna tala, intill den dagen, då detta sker; derföre, att du icke trodde minom ordom, hvilke skola fullkomnad varda i sin tid.
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
Och folket förbidde Zachariam, och förundrade sig, att han så länge dvaldes i templet.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
Men då han utgick, kunde han intet tala med dem; och så förmärkte de, att han hade sett någon syn i templet; och han tecknade dem, och blef mållös.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
Och det begaf sig, då hans ämbetsdagar ute voro, gick han hem i sitt hus.
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
Och efter de dagar vardt hans hustru Elisabet hafvandes; och fördolde sig i fem månader, och sade:
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
Så hafver nu Herren gjort med mig, i de dagar, då han såg till mig, på det han skulle borttaga min försmädelse ibland menniskorna.
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
Uti sjette månaden vardt Gabriel Ängel utsänd af Gudi, uti en stad i Galileen, benämnd Nazareth;
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
Till en jungfru, som förlofvad var enom man, hvilkens namn var Joseph, af Davids hus; och jungfrunes namn Maria.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
Och Ängelen kom in till henne, och sade: Hel, full med nåd! Herren är med dig; välsignad du ibland qvinnor.
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
Då hon såg honom, vardt hon förfärad af hans tal, och tänkte uppå, hurudana helsning detta var.
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
Då sade Ängelen till henne: Frukta dig icke, Maria; ty du hafver funnit nåd för Gudi.
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
Si, du skall afla i ditt lif, och föda en son, hvilkens Namn du skall kalla JESUS.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
Han skall varda stor, och kallas dens Högstas Son; och Herren Gud skall gifva honom hans faders Davids säte;
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
Och han skall vara en Konung öfver Jacobs hus i evig tid; och på hans rike skall ingen ände vara. (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
Då sade Maria till Ängelen: Huru skall detta tillgå? Ty jag vet af ingen man.
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
Ängelen svarade, och sade till henne: Den Helge Ande skall komma öfver dig, och dens Högstas kraft skall öfverskygga dig; derföre ock det Helga, som af dig födt varder, skall kallas Guds Son.
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
Och si, Elisabet, din fränka, hafver ock aflat en son i sin ålderdom; och detta är sjette månaden åt henne, som hetes vara ofruktsam;
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
Ty för Gud är ingen ting omöjelig.
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
Då sade Maria: Si, Herrans tjenarinna; varde mig efter ditt tal. Och Ängelen skiljdes ifrå henne.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
Uti de dagar stod Maria upp, och gick i bergsbygdena med hast, uti Jude stad;
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
Och kom uti Zacharie hus, och helsade Elisabet.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
Och det begaf sig, då Elisabet hörde Marie helsning, sprang barnet uti hennes lif. Och Elisabet vardt uppfylld med den Helga Anda;
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
Och hon ropade med höga röst, och sade: Välsignad du ibland qvinnor, och välsignad dins lifs frukt.
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
Och hvadan kommer mig detta, att mins Herras moder kommer till mig?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
Si, då rösten af dine helsning kom i min öron, sprang barnet af glädje i mitt lif.
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
Och salig äst du, som trodde; ty all ting varda fullbordad, som dig sagd äro af Herranom.
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
Och Maria sade: Min själ prisar storliga Herran;
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
Och min ande fröjdar sig i Gudi, minom Frälsare;
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
Ty han hafver sett till sine tjenarinnos ringhet: Si, härefter varda all slägte mig saliga kallande.
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
Ty den Mägtige hafver gjort mägtig ting med mig, och hans Namn är heligt;
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
Och hans barmhertighet varar ifrå slägte till slägte, öfver dem som frukta honom.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
Han hafver bedrifvit magt med sinom arm, och förskingrat dem, som högfärdige äro uti deras hjertas sinne.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
De mägtige hafver han satt af sätet, och uppsatt de ringa.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
De hungriga hafver han med god ting uppfyllt, och de rika hafver han låtit tomma blifva.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
Han hafver upptagit sin tjenare Israel, tänkande på sina barmhertighet;
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
Såsom han sagt hafver till våra fäder, Abraham och hans säd, till evig tid. (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
Och Maria blef när henne vid tre månader; och gick så hem i sitt hus igen.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
Så vardt då Elisabet tiden fullbordad att hon skulle föda, och hon födde en son.
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
Och hennes grannar och fränder fingo höra, att Herren hade gjort stor barmhertighet med henne, och fröjdade sig med henne.
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
Och det begaf sig, på åttonde dagen kommo de till att omskära barnet; och kallade honom, efter hans fader, Zacharias.
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
Då svarade hans moder, och sade: Ingalunda; men han skall heta Johannes.
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
Då sade de till henne: Uti dine slägt är ingen, som hafver det namnet.
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
Så tecknade de hans fader, hvad han ville kalla honom.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
Och han äskade ena taflo, der han uti skref, sägandes: Johannes är hans namn; och alle förundrade sig derpå.
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
Och straxt öppnades hans mun, och hans tunga; och han talade, lofvandes Gud.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
Och stor fruktan kom öfver alla deras grannar; och ryktet om allt detta gick ut öfver alla Judiska bergsbygdena.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
Och alle de, som det hörde, sattet i sitt hjerta, sägande: Hvad månn varda utaf detta barnet? Ty Herrans hand var med honom.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
Och hans fader Zacharias vardt uppfylld med den Helga Anda, propheterade, och sade:
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
Lofvad vare Herren, Israels Gud; ty han hafver besökt och förlossat sitt folk;
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
Och hafver upprättat oss salighetenes horn, uti sins tjenares Davids hus;
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
Såsom han i förtiden talat hafver, genom sina helga Propheters mun; (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
Att han skulle frälsa oss ifrå våra ovänner, och utur allas deras hand, som hata oss;
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
Och bevisa barmhertighet med våra fäder, och minnas på sitt helga Testamente;
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
Och på den ed, som han svorit hafver vårom fader Abraham, att gifva oss;
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
Att vi, frälste utur våra ovänners hand, måtte honom tjena utan fruktan;
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
I helighet och rättfärdighet, för honom, i alla våra lifsdagar.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
Och du barn skall kallas dens Högstas Prophet; du skall gå för Herranom, till att bereda hans vägar;
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
Och gifva hans folke salighetenes kunskap, till deras synders förlåtelse;
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
Genom vår Guds innerliga barmhertighet, genom hvilken uppgången af höjdene hafver oss besökt;
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
Till att uppenbaras dem, som sitta i mörkret och dödsens skugga, och styra våra fötter på fridsens väg.
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
Och barnet växte upp, och stärktes i Andanom; och vistades i öknene, till den dagen han skulle framkomma för Israels folk.

< Luka 1 >