< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
بسیاری دست به تألیف حکایت اموری زده‌اند که نزد ما به انجام رسیده است.
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
برای انجام این کار، آنها از مطالبی استفاده کرده‌اند که از طریق شاهدان عینی وقایع و شاگردان اولیه، در دسترس ما قرار گرفته است.
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
از آنجا که من خود، این مطالب را از آغاز تا پایان، با دقت بررسی و مطالعه کرده‌ام، چنین صلاح دیدم که ماجرا را به طور کامل و به ترتیب برای شما، عالیجناب تِئوفیلوس، بنویسم،
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
تا از درستی تعلیمی که یافته‌اید، اطمینان حاصل کنید.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
ماجرا را از کاهنی یهودی آغاز می‌کنم، با نام زکریا، که در زمان هیرودیس، پادشاه یهودیه، زندگی می‌کرد. او عضو دسته‌ای از کاهنان معبد بود که اَبیّا نام داشت. همسرش الیزابت نیز مانند خود او از قبیلهٔ کاهنان یهود و از نسل هارون برادر موسی بود.
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
زکریا و الیزابت هر دو در نظر خدا بسیار درستکار بودند و با جان و دل تمام احکام و فرایض خداوند را رعایت می‌کردند.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
اما آنها فرزندی نداشتند، زیرا الیزابت نازا بود؛ از این گذشته، هر دو بسیار سالخورده بودند.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
یکبار که گروه زکریا در معبد خدمت می‌کرد، و او به انجام وظایف کاهنیِ خود مشغول بود،
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
به حکم قرعه نوبت به او رسید که به جایگاه مقدّس معبد داخل شود و در آنجا بخور بسوزاند.
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
به هنگام سوزاندن بخور، جمعیت انبوهی در صحن معبد مشغول عبادت بودند.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
ناگهان فرشته‌ای بر زکریا ظاهر شد و در طرف راست مذبح بخور ایستاد.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
زکریا از دیدن فرشته مبهوت و هراسان شد.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
فرشته به او گفت: «ای زکریا، نترس! چون آمده‌ام به تو خبر دهم که خدا دعایت را شنیده است، و همسرت الیزابت برایت پسری به دنیا خواهد آورد که نامش را یحیی خواهی گذاشت.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
این پسر باعث شادی و سُرور شما خواهد شد، و بسیاری نیز از تولدش شادی خواهند نمود.
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
زیرا او در نظر خداوند بزرگ خواهد بود. او هرگز نباید شراب و مشروبات سُکرآور بنوشد، چون حتی پیش از تولد، از روح‌القدس پر خواهد بود!
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
بسیاری از بنی‌اسرائیل توسط او به سوی خداوند، خدای خود بازگشت خواهند نمود.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
او خدمت خود را با همان روح و قدرت ایلیای نبی انجام خواهد داد. او پیشاپیش مسیح خواهد آمد تا مردم را برای ظهور او آماده کند و دل پدران را به سوی فرزندان بازگرداند. او سبب خواهد شد افراد سرکش، حکمت خداترسان را بپذیرند.»
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
زکریا به فرشته گفت: «ولی این غیرممکن است، چون من پیر شده‌ام و همسرم نیز سالخورده است!»
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
فرشته در جواب گفت: «من جبرائیل هستم که در حضور خدا می‌ایستم و اوست که مرا فرستاده تا این خبر خوش را به تو بدهم.
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
اما حال که سخنان مرا باور نکردی، لال خواهی شد و تا زمانی که کودک به دنیا بیاید یارای سخن گفتن نخواهی داشت؛ زیرا آنچه گفتم، در زمان مقرر واقع خواهد شد.»
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
در این میان، مردم در صحن معبد منتظر زکریا بودند و از اینکه او در بیرون آمدن از جایگاه مقدّس این همه تأخیر می‌کرد، در حیرت بودند.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
سرانجام وقتی بیرون آمد و نتوانست با ایشان سخن گوید، از اشارات او پی بردند که در جایگاه مقدّس معبد رؤیایی دیده است.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
زکریا پس از پایان دوره خدمتش، به خانهٔ خود بازگشت.
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
طولی نکشید که همسرش الیزابت باردار شد. او برای مدت پنج ماه گوشه‌نشینی اختیار کرد و می‌گفت:
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
«سرانجام خداوند بر من نظر لطف انداخت و کاری کرد که دیگر در میان مردم شرمگین نباشم!»
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
در ششمین ماه بارداری الیزابت، خدا فرشته خود جبرائیل را به ناصره، یکی از شهرهای ایالت جلیل فرستاد،
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
تا نزد دختری به نام مریم برود. مریم نامزدی داشت به نام یوسف، از نسل داوود پادشاه.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
جبرائیل بر مریم ظاهر شد و گفت: «درود بر تو، که بسیار مورد لطف هستی! خداوند با توست!»
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
مریم از این سخنان پریشان و متحیّر شد، و نمی‌دانست این چه نوع تحیّتی می‌تواند باشد.
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
فرشته به او گفت: «ای مریم، نترس! زیرا خدا بر تو نظر لطف انداخته است!
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
تو به‌زودی باردار شده، پسری به دنیا خواهی آورد و نامش را عیسی خواهی نهاد.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
او بسیار بزرگ خواهد بود و پسر خدای متعال نامیده خواهد شد، و خداوند تخت سلطنت جدّش، داوود را به او خواهد سپرد،
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
تا برای همیشه بر نسل یعقوب سلطنت کند، سلطنتی که هرگز پایانی نخواهد داشت!» (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
مریم از فرشته پرسید: «اما چگونه چنین چیزی امکان دارد؟ دست هیچ مردی هرگز به من نرسیده است!»
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
فرشته پاسخ داد: «روح‌القدس بر تو خواهد آمد، و قدرت خدای متعال بر تو سایه خواهد افکند. از این رو، آن نوزاد مقدّس بوده، پسر خدا خوانده خواهد شد.
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
بدان که خویشاوند تو، الیزابت نیز شش ماه پیش در سن پیری باردار شده و به‌زودی پسری به دنیا خواهد آورد؛ بله، همان کس که همه او را نازا می‌خواندند.
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
زیرا برای خدا هیچ کاری محال نیست!»
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
مریم گفت: «من خدمتگزار خداوند هستم. هر چه دربارۀ من گفتی، همان بشود.» آنگاه فرشته او را ترک گفت.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
پس از چند روز، مریم تدارک سفر دید و شتابان به کوهستان یهودیه رفت،
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
جایی که زکریا زندگی می‌کرد. مریم وارد خانه شده، به الیزابت سلام کرد.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
به محض اینکه صدای سلام مریم به گوش الیزابت رسید، آن طفل در رحم او به حرکت درآمد. آنگاه الیزابت از روح‌القدس پر شد،
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
و با صدای بلند به مریم گفت: «تو در میان زنان خجسته‌ای، و فرزندت نیز خجسته است.
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
چه افتخار بزرگی است برای من، که مادر خداوندم به دیدنم بیاید!
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
وقتی وارد شدی و به من سلام کردی، به محض اینکه صدایت را شنیدم، بچه از شادی در رَحِمِ من به حرکت درآمد!
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
خوشا به حال تو، زیرا ایمان آوردی که هر چه خدا به تو گفته است، به انجام خواهد رسید!»
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
مریم گفت: «خداوند را با تمام وجود ستایش می‌کنم،
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
و روح من، به سبب نجات‌دهنده‌ام خدا، شاد و مسرور است!
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
چون او منِ ناچیز را مورد عنایت قرار داده است. از این پس، همهٔ نسلها مرا خوشبخت خواهند خواند،
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
زیرا خدای قادر و قدوس در حق من کارهای بزرگ کرده است.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
«لطف و رحمت او، نسل اندر نسل شامل حال آنانی می‌شود که از او می‌ترسند.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
او دست خود را با قدرت دراز کرده و متکبران را همراه نقشه‌هایشان پراکنده ساخته است.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
سلاطین را از تخت به زیر کشیده و فروتنان را سربلند کرده است.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
گرسنگان را با نعمتهای خود سیر کرده، اما ثروتمندان را تهی دست روانه نموده است.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
او رحمت خود را به یاد آورده، و خادم خویش اسرائیل را یاری داده است.
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
بله، او که وعدهٔ ابدی خود را که به ابراهیم و فرزندانش داده بود، به یاد آورده است.» (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
مریم حدود سه ماه نزد الیزابت ماند. سپس به خانه خود بازگشت.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
سرانجام، انتظار الیزابت پایان یافت و زمان وضع حملش فرا رسید و پسری به دنیا آورد.
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
وقتی که همسایگان و بستگان او از این خبر آگاهی یافتند و دیدند که خداوند چه لطف بزرگی در حق او نموده است، نزد او آمده، در شادی‌اش شریک شدند.
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
چون نوزاد هشت روزه شد، تمام بستگان و دوستانشان برای مراسم ختنه گرد آمدند و قصد داشتند نام پدرش، زکریا را بر او بگذارند.
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
اما الیزابت نپذیرفت و گفت: «نام او یحیی خواهد بود.»
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
گفتند: «اما در خانواده تو، کسی چنین نامی نداشته است.»
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
پس با اشاره، از پدر نوزاد پرسیدند که می‌خواهد نام او را چه بگذارد.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
زکریا با اشاره، تخته‌ای خواست و در برابر چشمان حیرت‌زدهٔ همه نوشت: «نامش یحیی است!»
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
در همان لحظه زبانش باز شد و قدرت سخن گفتن را بازیافت و به شکرگزاری خدا پرداخت.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
همسایگان با دیدن تمام این وقایع بسیار متعجب شدند، و خبر این ماجرا در سراسر کوهستان یهودیه پخش شد.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
هر که این خبر را می‌شنید، به فکر فرو می‌رفت و از خود می‌پرسید: «این طفل، در آینده چه خواهد شد؟»، زیرا همه می‌دیدند که او مورد توجه خاص خداوند قرار دارد.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
آنگاه پدرش زکریا، از روح‌القدس پر شد و نبوّت کرده، چنین گفت:
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
«خداوند، خدای اسرائیل را سپاس باد، زیرا به یاری قوم خود شتافته و ایشان را رهایی بخشیده است.
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
او به‌زودی برای ما نجات‌دهنده‌ای قدرتمند از نسل داوود خواهد فرستاد؛
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
چنانکه از دیرباز، از زبان انبیای مقدّس خود وعده می‌داد (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
که شخصی را خواهد فرستاد تا ما را از چنگ دشمنانمان و از دست همه آنانی که از ما نفرت دارند، رهایی بخشد.
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
«او نسبت به نیاکان ما، رحیم و مهربان بوده است. بله، او عهد و پیمان مقدّس خود را به یاد آورده است،
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
همان عهدی را که با سوگند با جدّ ما، ابراهیم بست،
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
که ما را از دست دشمنانمان رهایی بخشد تا بتوانیم بدون ترس و واهمه او را عبادت کنیم
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
و تمام روزهای عمر خود را در حضور او با پاکی و عدالت بگذرانیم.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
«و تو ای فرزند من، نبی خدای متعال نامیده خواهی شد، زیرا پیشاپیش خداوند حرکت خواهی کرد تا راه او را آماده نمایی،
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
و قوم او را آگاه سازی که با آمرزش گناهانشان نجات خواهند یافت.
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
اینها، همه به سبب رحمت و شفقت بی‌پایان خدای ماست. به‌زودی سپیده صبح از افق آسمان بر ما طلوع خواهد کرد
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
تا بر کسانی که در تاریکی و سایۀ مرگ ساکن هستند، بتابد و همهٔ ما را به سوی آرامش و صلح و صفا هدایت نماید.»
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
آن کودک رشد می‌کرد و در روح، نیرومند می‌شد. او در بیابانها به سر می‌بُرد، تا روزی فرا رسید که می‌بایست خدمت خود را به‌طور علنی در میان قوم اسرائیل آغاز کند.

< Luka 1 >