< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
बऊत जणेया सेयो गल्ला, जो आसा बीचे ओईया, इतियास लिखणे रे आसा री मताद कित्ती,
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
जेड़ा कि पईले ई तिने जो इना गल्ला खे देखणे वाल़े और वचनो खे मानणे वाल़े सेवक थे, आसा गे पऊँछाईया।
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
तेबेई तो, ओ श्रीमान् थियुफिलुस! माखे बी ये ठीक लगेया कि तिना सबी गल्ला रा सारा आल शुरूओ तेई ठीक-ठीक पता लगाई की तिना ताखे एक-एक करी की लिखूँ।
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
ताकि तूँ ये जाणी लो कि यो गल्ला, जिना री तैं शिक्षा पाई राखी, केड़िया अटल ए।
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
यहूदिया प्रदेशो रे राजा हेरोदेसो रे बखते अबिय्याहो रे दलो रे जकरयाह नाओं रा एक पुरोईत था और तेसरी लाड़िया रा नाओं इलीशिबा था। ये दोनो लाड़ा-लाड़ी हारूणो रे कुलो रे थे।
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
सेयो दोनो परमेशरो सामणे तर्मी थे और परमेशरो री सारी आज्ञा और बिधिया पाँदे निर्दोष चलो थे।
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
तिना रे कोई ल्वाद नि थी, कऊँकि इलीशिबा बांझ थी और सेयो दोनो स्याणे ऊईगे थे।
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
एक दिन जेबे जकरयाह आपणे दलो री बारिया पाँदे परमेशरो सामणे पुरोईतो रा काम करो था।
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
तेबे पुरोईता री रवाजा रे मुताबिक, तेसरे नाओं री चिट्ठी निकल़ी, कि परमेशरो रे मन्दरो रे जाई की तूप बाल़।
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
और तूप बाल़ने रे बखते, लोका री सारी मण्डल़ी बारे मन्दरो रे आँगणो रे प्रार्थना करने लगी री थी।
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
तेबे जकरयाहो खे प्रभुए रा स्वर्गदूत तूपो री वेदिया रे दाँणे कनारे खड़ेया रा दिशेया।
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
जकरयाह तेसखे देखी की कबराईगा और बऊत डरीगा।
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
पर स्वर्गदूते तेसखे बोलेया, “ओ जकरयाह! डर नि, कऊँकि परमेशरे तेरी प्रार्थना सुणी ली री और जो तेरी लाड़ी इलीशिबा ए, तेसा रे ताखे एक पाऊ जमणा और तैं तेसरा नाओं यूहन्ना राखणा।
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
ताखे आनन्द और खुशी ऊणी और बऊत सारे लोक तेसरे जमणे ते खुश ऊणे।
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
कऊँकि से परमेशरो सामणे महान् ऊणा, तेस अँगूरा रा रस और शराब कदी नि पीणा और से आपणी माया रे गर्भो तेई पवित्र आत्मा ते परेया रा ऊणा।
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
तेस इस्राएलो बीचा ते कई जणे, तिना रे प्रभु परमेशरो री तरफा खे फेरने।
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
से एलिय्याह री आत्मा और सामर्था रे ऊई की तेसरे आगे-आगे चलणा ताकि पितरा रा मन बाल-बच्चेया री तरफा खे फेरो। आज्ञा नि मानणे वाल़ेया खे तर्मिया री समजा रे ल्याओ और प्रभुए खे एक लायक प्रजा त्यार करो।”
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
जकरयाहे स्वर्गदूतो ते पूछेया, “ये आऊँ किंयाँ जाणूं कि एड़ा ई मां साथे ऊणा? कऊँकि आऊँ और मेरी लाड़ी तो स्याणे ऊईगे रे।”
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
स्वर्गदूते तेसखे बोलेया, “आऊँ जिब्राईल ए, जो परमेशरो सामणे खड़ा रओआ। आऊँ तां साथे गल्ला करने और ये सुसमाचार सुनाणे रिया तंईं पेजी राखेया
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
और देख जदुओ तक यो गल्ला पूरिया नि ऊई जाओगिया, तदुओ तक तूँ चुप रणा और बोली नि सकदा। कऊँकि तैं मेरिया गल्ला पाँदे कि सेयो आपणे बखते पूरिया ऊणिया, विश्वास नि कित्तेया।”
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
लोक जकरयाहो खे न्याल़दे रए और हैरान ऊईगे कि तेसखे मन्दरो रे इतणी देर किंयाँ ऊईगी?
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
जेबे से बारे आया, तेबे से तिना साथे गलाई नि सकेया, तेबे तिना खे पता लगी गा कि तिने मन्दरो रे कोई दर्शन पाई राखेया, से तिना साथे साअरे रे गल्ला करदा रया और गूँगा ऊईगा।
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
जेबे मन्दरो रे तेसरे पुरोईतो रे कामो री सेवा करने रे दिन पूरे ऊईगे, तेबे से यरूशलेमो नगरो खे छाडी की आपणे कअरो खे चली गा।
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
तेबे तेसरी लाड़ी इलीशिबा गर्भवती ऊईगी और पाँज मीन्ने तक आपू खे कअरे ये बोली की लकोए रे राखेया,
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
“मांणूए जो मेरी बेज्जती करी राखी, तिजी खे दूर करने खे, परमेशरे मां पाँदे कृपा करने खे एड़ा करी राखेया।”
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
इलीशिबा रे गर्भावस्था रे छटुए मीन्ने परमेशरो री तरफा ते जिब्राईल स्वर्गदूत गलील प्रदेशो रे नासरत नाओं नगरो रे,
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
एक कुआँरिया गे पेजेया। तेसारी मंगणी यूसुफ नाओं रे दाऊदो रे कराने रे एक माठे साथे ऊई थी। तेसा कुआँरिया रा नाओं मरियम था।
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
स्वर्गदूते तेसा गे पीतरे आयी की बोलेया, “खुशी और जय तेरी ओ, जेस पाँदे परमेशरो री कृपा ऊई री, प्रभु तां साथे ए।”
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
से तेस वचनो ते बऊत कबराई गी और सोचणे लगी कि ये केड़ी गल्ल ए?
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
स्वर्गदूते तेसा खे बोलेया, “ओ मरियम! डर नि कऊँकि परमेशरो री कृपा तां पाँदे ऊई री।
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
देख, तूँ गर्भवती ऊणी, तेरे एक पाऊ जमणा और तैं तेसरा नाओं यीशु राखणा।
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
से महान् ऊणा, और परमप्रदानो रा पुत्र ऊणा और प्रभु परमेशरे तेसरे पुरखा दाऊदो रा सिंहासन तेसखे देणा।
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
और तेस याकूबो रे कराने रे सदा राज्य करना और तेसरे राज्य रा अंत कदी नि ऊणा।” (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
मरियमे स्वर्गदूतो खे बोलेया, “ये किंयाँ ऊणा? आऊँ तो मर्दो खे जाणदी ई नि, कऊँकि आऊँ तो एबु कुँवारी ए”
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
स्वर्गदूते तेसा खे जवाब दित्तेया, “पवित्र आत्मा तां पाँदे उतरना और परमप्रदानो री सामर्थ तां पाँदे छांयाँ करनी, तेबेई तो से, जो जमणे वाल़ा ए, तेसखे पवित्र और परमेशरो रा पुत्र बोलेया जाणा।
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
देख, तेरे टब्बरो री इलीशिबा रे बी स्याणदे बखते पाऊ ऊणे वाल़ा ए। ये तेसा रा, जेसा खे बांझ बोलोए, छटा मीन्ना चली रा।
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
कऊँकि परमेशर सब कुछ करी सकोआ।”
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
मरियमे बोलेया, “देख, आऊँ परमेशरो री दासी ए, मां साथे तेरे वचनो रे मुताबिक ओ।” तेबे स्वर्गदूत तेसा गे ते चली गा।
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
तिना दिना रे मरियम उठी की फटाफट पाह्ड़ी इलाके रे यहूदा प्रदेशो रे एक नगरो खे गई
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
और तेसे जकरयाहो रे कअरे जाई की इलीशिबा खे नमस्ते कित्ती।
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
जिंयाँ ई इलीशिबे मरियमा री नमस्ते सुणी, तिंयाँ ई बच्चा तेसा रे पेटो रे उटकेया और ईलीशिबा पवित्र आत्मा ते फरी गी।
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
तेबे तेसे मरियमा खे जोरे की बोलेया, “तूँ सबी जवाणसा बीचे धन्य ए और जेस बच्चे खे तां जन्म देणा से बी धन्य ए।
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
ये कृपा मां पाँदे केथा ऊई कि मेरे प्रभुए री आम्मा मांगे आयी?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
जिंयाँ ई मैं तेरी नमस्ते सुणी, तिंयाँ ई बच्चा मेरे पेटो रे खुश ऊई की उटकणे लगेया।
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
धन्य ए से, जिने विश्वास कित्तेया कि जो गल्ला प्रभुए री तरफा ते तेसा गे बोलिया, सेयो पुरिया ऊणिया।”
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
तेबे मरियमे बोलेया, “मेरा प्राण प्रभुए री बढ़ाई करोआ।
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
और मेरी आत्मा मेरा उद्धार करने वाल़े परमेशरो ते खुश ए।
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
कऊँकि तिने आपणी दासिया कनारो खे देखेया, तेबेई तो, देखो, आजो ते सारे जुगा-जुगा रे लोका माखे धन्य बोलणा।
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
कऊँकि तिने शक्तिमाने मेरे बड़े-बड़े काम करी राखे और तेसरा नाओं पवित्र ए।
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
तेस परमेशरो री दया, जो तेसते डरोए, पीढ़िया री पीढ़िया तक बणी री रओई।
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
तिने आपणे आथो रे जरिए सामर्था रे काम दिखाए और जो आपू खे बड़ा समजोए, सेयो रूल़ाई ते।
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
तिने राजेया रा राज खत्म करी ता और शरीफ ऊच्चे कित्ते।
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
तिने पूखे अच्छी चीजा ते रजाए और अमीर खाली आथे निकयाल़ी ते।
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
तिने आपणा सेवक इस्राएल सम्बाल़ी ता। ताकि आपणी तेसा दया रे वादे खे याद करुँ,
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
जो अब्राहम और तेसरे कुल़ो पाँदे सदा रणी, जेड़ा तिने म्हारे बाओ-दादेया खे बोलेया था।” (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
मरियम तकरीबन तीन मीन्ने तक तेती रई और तेबे कअरो खे चली गी।
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
तेबे इलीशिबा रे बच्चा पैदा करने रा बखत पूरा ऊईगा और तेसा रे एक पाऊ जम्मेया।
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
तेसा रे पड़ोसी और टब्बरो वाल़ेया जेबे ये सुणेया कि प्रभुए तेसा पाँदे बड़ी पारी दया करी राखी, सेयो तेसा साथे बऊत खुश ऊए।
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
तेबे एड़ा ऊआ कि सेयो आठुए दिने बाल़को रा खतना करने आए और तेसरा नाओं, तेसरे बाओ रे नाओं पाँदे जकरयाह राखणे लगे।
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
तेबे बच्चे री आम्मे बोलेया, “ना; एसरा नाओं यूहन्ना राखणा।”
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
तेबे तिने बोलेया, “तेरे टब्बरो रे एड़ा नाओं केसी रा निए।”
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
तेबे तिने तेसरे बाओ ते साअरे रे पूछेया, “तूँ एसरा क्या नाओं राखणा चाएया?”
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
तेबे तिने लिखणे री पट्टी मुंगाई की लिखी ता, “एसरा नाओं यूहन्ना ए” और सब हैरान ऊईगे।
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
तेबे तेसरा मूँ और जीब तेबुई खुली गी। तेबे से बोलणे जोगा ऊईगा और परमेशरो रा धन्यवाद करने लगेया।
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
तेसरे ओरे-पोरे रणे वाल़े लोक डरी गे और तिना सबी गल्ला री चर्चा यहूदिया प्रदेशो रे सारे पाह्ड़ी इलाके रे फैली गी।
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
सब सुणने वाल़े आपणे-आपणे मनो रे बिचार करने लगे, “ये बाल़क केड़ा ऊणा?” कऊँकि परमेशरो रा आथ तेस साथे ए।
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
तेबे तेसरा पिता जकरयाह पवित्र आत्मा ते परी गा और भविष्यबाणी करने लगेया,
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
“प्रभु इस्राएलो रा परमेशर धन्य ए, जो तिने आपणे लोका कनारो खे देखेया और तिना खे छुटकारा दित्तेया
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
और आपणे सेवक दाऊदो रे कराने रे आसा खे उद्धारकर्ता पेजी राखेया।
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
जेड़ा तिने आपणे पवित्र भविष्यबक्तेया ते बुलवाया था, जो दुनिया रे शुरूओ ते ऊँदे ऊए आयी रे (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
मतलब-आसा रे दुश्मणा ते और बैरिया रे आथो ते म्हारा उद्धार करी राखेया।
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
ताकि आसा रे बाप-दादेया पाँदे कृपा करी की आपणी पवित्र वाचा याद राखो
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
और से कसम जो तिने आसा रे पिते अब्राहमो साथे खाई थी
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
कि तेस आसा खे ये देणा, ताकि आसे आपणे दुश्मणा रे आथो ते बची की
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
परमेशरो सामणे पवित्रता, और धार्मिकता साथे सारी जिन्दगी नच्चके रई की तेसरी सेवा करदे रईए।
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
ओ बाल़क! ताखे परमप्रदान परमेशरो रा भविष्यबक्ता बोलेया जाणा, कऊँकि तूँ प्रभुए री बाट त्यार करने खे तिना रे आगे-आगे चलणा।
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
ताकि तिना रे लोका खे उद्धारो रा ज्ञान देई सके, जो तिना रे पापो री माफिया ते मिलोआ।
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
ये आसा रे परमेशरो री तेसा बड़िया दया ते ऊणा; जेसरी बजअ ते, स्वर्गो ते आसा पाँदे प्यागा रा प्रयासा ऊणा।
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
ताकि न्हेरे रे और मरने वाल़ेया खे जिन्दगी देई सको, और आसा रे पैरा खे शान्तिया री बाटा रे सिदे चलाई सको।”
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
तेबे से बाल़क यूहन्ना बड़दा और आत्मा रे तागतबर ऊँदा गया और इस्राएलो रे सामणे आऊणे रे दिना तक, जंगल़ो रे रया।

< Luka 1 >