< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
To his Excellency, Theophilus. Many attempts have been already made to draw up an account of those events which have reached their conclusion among us,
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
just as they were reported to us by those who from the beginning were eye-witnesses, and afterward became bearers of the message.
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
And, therefore, I also, since I have investigated all these events with great care from their very beginning, have resolved to write a connected history of them for you,
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
in order that you may be able to satisfy yourself of the accuracy of the story which you have heard from the lips of others.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
In the reign of Herod, king of Judea, there was a priest named Zechariah, who belonged to the division called after Abijah. His wife, whose name was Elizabeth, was also a descendant of Aaron.
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
They were both righteous people, who lived blameless lives, guiding their steps by all the commandments and ordinances of the Lord.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
But they had no child, Elizabeth being barren; and both of them were advanced in years.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
One day, when Zechariah was officiating as priest before God, during the turn of his division,
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
it fell to him by lot, in accordance with the practice among the priests, to go into the Temple of the Lord and burn incense;
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
and, as it was the Hour of Incense, the people were all praying outside.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
And an angel of the Lord appeared to him, standing on the right of the Altar of Incense.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
Zechariah was startled at the sight and was awe-struck.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
But the angel said to him, “Do not be afraid, Zechariah; your prayer has been heard, and your wife Elizabeth will bear you a son, whom you will call by the name John.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
He will be to you a joy and a delight; and many will rejoice over his birth.
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
For he will be great in the sight of the Lord; he will not drink any wine or strong drink, and he will be filled with the Holy Spirit from the very hour of his birth,
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
and will reconcile many of the Israelites to the Lord their God.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
He will go before him in the spirit and with the power of Elijah, to reconcile fathers to their children and the disobedient to the wisdom of the righteous, and so make ready for the Lord a people prepared for him.”
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
“How can I be sure of this?” Zechariah asked the angel. “For I am an old man and my wife is advanced in years.”
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
“I am Gabriel,” the angel answered, “who stand in the presence of God, and I have been sent to speak to you and to bring you this good news.
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
And now you will be silent and unable to speak until the day when this takes place, because you did not believe what I said, though my words will be fulfilled in due course.”
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
Meanwhile the people were watching for Zechariah, wondering at his remaining so long in the Temple.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
When he came out, he was unable to speak to them, and they perceived that he had seen a vision there. But Zechariah kept making signs to them, and remained dumb.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
And, as soon as his term of service was finished, he returned home.
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
After this his wife, Elizabeth, became pregnant and lived in seclusion for five months.
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
“The Lord has done this for me,” she said, “he has shown me kindness and taken away the public disgrace of childlessness under which I have been living.”
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
Six months later the angel Gabriel was sent from God to a town in Galilee called Nazareth,
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
to a maiden there who was engaged to a man named Joseph, a descendant of David. Her name was Mary.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
Gabriel came into her presence and greeted her, saying, “You have been shown great favor – the Lord is with you.”
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
Mary was much disturbed at his words, and was wondering to herself what such a greeting could mean,
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
when the angel spoke again, “Do not be afraid, Mary, for you have found favor with God.
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
And now, you will conceive and give birth to a son, and you will give him the name Jesus.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
The child will be great and will be called ‘Son of the Most High,’ and the Lord God will give him the throne of his ancestor David,
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
and he will reign over the descendants of Jacob for ever; And to his kingdom there will be no end.” (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
“How can this be?” Mary asked the angel. “For I have no husband.”
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
“The Holy Spirit will descend on you,” answered the angel, “and the Power of the Most High will overshadow you; and therefore the child will be called ‘holy,’ and ‘Son of God.’
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
And Elizabeth, your cousin, is herself also expecting a son in her old age; and it is now the sixth month with her, though she is called barren;
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
for no promise from God will fail to be fulfilled.”
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
“I am the servant of the Lord,” exclaimed Mary. “Let it be with me as you have said.” Then the angel left her.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
Soon after this Mary set out, and made her way quickly into the hill-country, to a town in Judah;
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
and there she went into Zechariah’s house and greeted Elizabeth.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
When Elizabeth heard Mary’s greeting, the child moved within her, and Elizabeth herself was filled with the Holy Spirit,
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
and cried aloud, “Blessed are you among women, and blessed is your unborn child!
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
But how have I this honor, that the mother of my Lord should come to me?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
For, as soon as your greeting reached my ears, the child moved within me with delight!
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
Happy indeed is she who believed that the promise which she received from the Lord would be fulfilled.”
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
And Mary said: “My soul exalts the Lord,
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
and my spirit delights in God my Savior,
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
for he has looked with favor on his humble servant girl. From now on all generations will call me blessed!
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
“For the Almighty has done great things for me, and holy is his name.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
He has mercy on those who revere him in every generation.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
“Mighty are the deeds of his arm! He has scattered the self-satisfied proud,
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
he has cast down the mighty from their thrones, and he uplifts the humble,
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
he has filled the hungry with good things, and the rich he has sent away empty.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
“He has stretched out his hand to his servant Israel, ever mindful of his mercy,
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
as he promised to our ancestors, to Abraham and his descendants for ever.” (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
Mary stayed with Elizabeth about three months, and then returned to her home.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
When Elizabeth’s time came, she gave birth to a son;
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
and her neighbors and relatives, hearing of the great goodness of the Lord to her, came to share her joy.
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
A week later they met to circumcise the child, and were about to call him Zechariah after his father,
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
when his mother spoke up, “No, he is to be called John.”
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
“You have no relation of that name!” they exclaimed;
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
and they made signs to the child’s father, to find out what he wished the child to be called.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
Asking for a writing tablet, he wrote the words – ‘His name is John.’ Everyone was surprised
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
and immediately Zechariah recovered his voice and the use of his tongue, and began to bless God.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
All their neighbors were awe-struck at this, and throughout the hill-country of Judea the whole story was much talked about.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
All who heard it kept it in mind, asking one another – “What can this child be destined to become?” For the Power of the Lord was with him.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
Then his father Zechariah was filled with the Holy Spirit, and, speaking under inspiration, said:
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
“Blessed is the Lord, the God of Israel, who has visited his people and wrought their deliverance,
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
and has raised up for us the strength of our salvation in the house of his servant David –
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
as he promised by the lips of his holy prophets of old – (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
salvation from our enemies and from the hands of all who hate us,
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
showing mercy to our ancestors, and mindful of his sacred covenant.
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
This was the oath which he swore to our ancestor Abraham –
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
that we should be rescued from the hands of our enemies,
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
and should serve him without fear in holiness and righteousness, in his presence all our days.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
And you, child, will be called prophet of the Most High, for you will go before the Lord to make ready his way,
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
to give his people the knowledge of salvation through the forgiveness of their sins,
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
through the tender mercy of our God, whereby the dawn will break on us from heaven,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
to give light to those who live in darkness and the shadow of death, and guide our feet into the way of peace.”
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
The child grew and became strong in spirit, and he lived in the wilds until the time came for his appearance before Israel.

< Luka 1 >