< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
Seeing that many have taken it in hand to draw up an account of those matters which have been fully established among us,
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
just as they reported them to us, who were from beginning eye- witnesses and ministers of the word,
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
it seemed good to me also accurately, from the very beginning, to write them to you in order, most excellent Theophilus,
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
so that you may know the certainty of the story which you have been taught by the word of mouth.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
In the reign of Herod, King of Judea, there was a certain priest, named Zachariah, belonging to the class of Abijah. He had a wife named Elizabeth,
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
who was a descendant of Aaron. They were both righteous in the sight of the Lord, walking in all the commandments and ordinances of the law, blameless.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
Now they had no child, for Elizabeth was barren, and both were far advanced in years.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
Now while Zachariah was acting as priest before God in the due course of his class, it fell to his lot, according to the custom of priesthood,
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
to enter into the sanctuary of the Lord and to burn incense.
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
And the whole multitude of the people were without, praying at the hour of incense.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
Then there appeared to him an angel of the Lord, standing on the right side of the altar of incense.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
And as he saw him Zachariah was troubled, and fear fell upon him.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
But the Angel said to him. "Do not be afraid, Zachariah, because your petition has been heard, and your wife Elizabeth will bear you a son, and you are to call him John.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
"And he shall be to you a joy and an exultation, and many shall rejoice over his birth.
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
"For he shall be great in the sight of the Lord, "He shall drink neither wine nor strong drink, "He shall be filled with the Holy Spirit from the hour of his birth,
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
"And shall win many of the sons of Israel to the Lord, their God.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
"He shall go before Him in the wisdom and power of Elijah to turn the hearts of the fathers to their children and the disobedient to the wisdom of the righteous, and so to make ready for the Lord a people prepared for him."
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
"How shall I be sure of this?" said Zachariah to the Angel. "For I am an old man and my wife is advanced in years."
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
"I am Gabriel," answered the angel, "who stand in the presence of God; and I have been sent to speak to you and to bring and to bring you this good news.
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
"And now you shall be silent and unable to speak until the day the day when this has taken place; because you did not believe my words - Words which will be fulfilled at their appointed time."
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
Meanwhile the people were waiting for Zachariah and wondering why he stayed so long in the sanctuary.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
And when he came out he could not speak to them, and then they knew that he had seen a vision in the sanctuary. He kept making signs to them and remained dumb.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
As soon as his term of priestly service was ended he went home;
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
and after those days Elizabeth, his wife, Conceived, and she hid herself five months, saying.
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
"This has the Lord done for me. He has now deigned to take the away my reproach among men."
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
Six months later the angel Gabriel was sent by God to a town in Galilee, called Nazareth,
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
to a maiden betrothed to a man named Joseph, a descendant of David. Her name was Mary.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
The angel went in and said to her. "Joy to you, highly favored one! "The Lord is with you."
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
Mary was greatly agitated at his word, and was revolving in her mind what this salutation could mean.
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
when the angel said to her. "Fear not Mary, for you have found grace with God.
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
"And behold, you shall conceive in your womb and bear a son; and you shall call his name Jesus.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
"He shall be great, and shall be called the Son of the Most High. "And the Lord God will give him the throne of his forefather David,
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
"and he shall reign over the House of Jacob forever; and of his kingdom there shall be no end." (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
And Mary said to the angel. "How can this be? For I have no husband?"
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
"The Holy Spirit shall come upon you," said the angel, "and the power of the most High shall overshadow you, and therefore the holy offspring which is born, shall be called the son of God.
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
"And behold your kinswoman, Elizabeth, she also has conceived a son in her old age, and this was the sixth month with her that was called barren.
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
"For no word of God shall be void of power."
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
Then Mary said. "Behold I am Lord’s slave. Let it be to me as you have said." Then the angel departed from her.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
Soon after this Mary set out and hastened unto the hill-country to a town in Judah;
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
and there she came into the house of Zachariah, and greeted Elizabeth.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
And when Elizabeth heard her salutation, the babe leaped in her womb, and Elizabeth herself was filled with the Holy Spirit,
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
and called out with a loud cry. "Blessed are you among women, and blessed is your unborn child!
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
"But why is this honor done me, that the mother of my Lord should come me?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
"For behold when the sound of your salutation reached my ears, the babe leaped with joy within my womb.
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
"And blessed is she who believed that the Lord’s words spoken to her would be fulfilled."
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
And Mary said. "My soul doth magnify the Lord,
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
"My spirit exults in the God, who is my Saviour,
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
"For he has regarded the humiliation of his slave, And from this hour all ages will count me blessed.
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
"For he who is mighty has done great things for me; And holy is his name.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
"His mercy is unto generations and generations on those who reverence him.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
"He has showed strength with his arm. "He has scattered proud in the imagination of their hearts;
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
"he has put down princes from their thrones, and has exalted those of low degree.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
"The hungry he has filled with good things, But the rich he has sent empty away.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
"He has helped Israel, his servant, that he might remember mercy,
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
"As he spoke to our forefathers, to Abraham and his offspring forever." (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
So Mary stayed with Elizabeth about three months and returned home.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
Now when the time of Elizabeth’s delivery was come, she gave birth to a son;
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
and her neighbors and kinsfolk heard that the Lord had magnified his mercy toward her; and they rejoiced with her,
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
and came on the eighth day to circumcise the child. They were about to call him "Zachariah," after his father,
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
when his mother said, "No, he is to be called John."
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
Said they, "You have no relatives of that name!"
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
Then they asked his father by signs what he wished to call the child.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
So he asked for a writing tablet and wrote down, "His name is John."
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
Every one was surprised, and at once his mouth was opened and his tongue loosed, and he spoke, blessing God.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
And there came a great fear upon all in the neighborhood; and throughout the hill country of Judea all these sayings were much talked about.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
All the story laid it up in their hearts, saying "What, then, will this child be?" For the Lord’s hands was with him.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
And his father, Zachariah, was filled with the Holy Spirit and prophesied, saying.
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
"Blessed be the Lord, the God of Israel, For he has visited and redeemed his people,
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
"And has raised up a mighty Deliverer for us In the house of his servant David,
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
"As he spake by the mouth of his holy Prophets Which have been since the world began (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
To deliver us from our enemies, and from the power Of all who hate us.
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
"He showed mercy to our forefathers, He remembered his holy covenant,
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
"The oath which he swore to Abraham, our forefather,
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
"That he we should be delivered out of the Hand of our enemies, And should serve him without fear,
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
"In holiness and righteousness before him All our days.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
"And thou, child, shalt be called the Prophet of the Most High, For thou shalt go before the Lord to prepare the way
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
"To give to his people a knowledge of salvation Through the remission of their sins,
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
"Through the heart of mercy of our God, Whereby the Dayspring from on high shall visit us,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
"To give light to those who sit in darkness and in the shadow of death, And to guide our feet into the paths of peace."
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
And the child grew, and became strong in the Spirit, and remained in the desert till the day of his showing to Israel.

< Luka 1 >