< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
Forasmuch as many have taken in hand to set forth in order a declaration of those things which are most surely believed among us,
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
Even as they delivered them unto us, which from the beginning were eyewitnesses, and ministers of the word;
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
It seemed good to me also, having had perfect understanding of all things from the very first, to write unto thee in order, most excellent Theophilus,
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
That thou mightest know the certainty of those things, wherein thou hast been instructed.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
There was in the days of Herod, the king of Judæa, a certain priest named Zacharias, of the course of Abia: and his wife was of the daughters of Aaron, and her name was Elisabeth.
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
And they were both righteous before God, walking in all the commandments and ordinances of the Lord blameless.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
And they had no child, because that Elisabeth was barren, and they both were now well stricken in years.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
And it came to pass, that while he executed the priest’s office before God in the order of his course,
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
According to the custom of the priest’s office, his lot was to burn incense when he went into the temple of the Lord.
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
And the whole multitude of the people were praying without at the time of incense.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
And there appeared unto him an angel of the Lord standing on the right side of the altar of incense.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
And when Zacharias saw him, he was troubled, and fear fell upon him.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
But the angel said unto him, Fear not, Zacharias: for thy prayer is heard; and thy wife Elisabeth shall bear thee a son, and thou shalt call his name John.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
And thou shalt have joy and gladness; and many shall rejoice at his birth.
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
For he shall be great in the sight of the Lord, and shall drink neither wine nor strong drink; and he shall be filled with the Holy Ghost, even from his mother’s womb.
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
And many of the children of Israel shall he turn to the Lord their God.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
And he shall go before him in the spirit and power of Elijah, to turn the hearts of the fathers to the children, and the disobedient to the wisdom of the just; to make ready a people prepared for the Lord.
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
And Zacharias said unto the angel, Whereby shall I know this? for I am an old man, and my wife well stricken in years.
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
And the angel answering said unto him, I am Gabriel, that stand in the presence of God; and am sent to speak unto thee, and to shew thee these glad tidings.
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
And, behold, thou shalt be dumb, and not able to speak, until the day that these things shall be performed, because thou believest not my words, which shall be fulfilled in their season.
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
And the people waited for Zacharias, and marvelled that he tarried so long in the temple.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
And when he came out, he could not speak unto them: and they perceived that he had seen a vision in the temple: for he beckoned unto them, and remained speechless.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
And it came to pass, that, as soon as the days of his ministration were accomplished, he departed to his own house.
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
And after those days his wife Elisabeth conceived, and hid herself five months, saying,
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
Thus hath the Lord dealt with me in the days wherein he looked on me, to take away my reproach among men.
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
And in the sixth month the angel Gabriel was sent from God unto a city of Galilee, named Nazareth,
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
To a virgin espoused to a man whose name was Joseph, of the house of David; and the virgin’s name was Mary.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
And the angel came in unto her, and said, Hail, thou that art highly favoured, the Lord is with thee: blessed art thou among women.
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
And when she saw him, she was troubled at his saying, and cast in her mind what manner of salutation this should be.
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
And the angel said unto her, Fear not, Mary: for thou hast found favour with God.
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
And, behold, thou shalt conceive in thy womb, and bring forth a son, and shalt call his name JESUS.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
He shall be great, and shall be called the Son of the Highest: and the Lord God shall give unto him the throne of his father David:
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
And he shall reign over the house of Jacob for ever; and of his kingdom there shall be no end. (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
Then said Mary unto the angel, How shall this be, seeing I know not a man?
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
And the angel answered and said unto her, The Holy Ghost shall come upon thee, and the power of the Highest shall overshadow thee: therefore also that holy thing which shall be born of thee shall be called the Son of God.
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
And, behold, thy cousin Elisabeth, she hath also conceived a son in her old age: and this is the sixth month with her, who was called barren.
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
For no word spoken by God shall be void of power.
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
And Mary said, Behold the handmaid of the Lord; be it unto me according to thy word. And the angel departed from her.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
And Mary arose in those days, and went into the hill country with haste, into a city of Judah;
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
And entered into the house of Zacharias, and saluted Elisabeth.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
And it came to pass, that, when Elisabeth heard the salutation of Mary, the babe leaped in her womb; and Elisabeth was filled with the Holy Ghost:
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
And she spake out with a loud voice, and said, Blessed art thou among women, and blessed is the fruit of thy womb.
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
And whence is this to me, that the mother of my Lord should come to me?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
For, lo, as soon as the voice of thy salutation sounded in mine ears, the babe leaped in my womb for joy.
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
And blessed is she that believed: for there shall be a performance of those things which were told her from the Lord.
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
And Mary said, My soul doth magnify the Lord,
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
And my spirit hath rejoiced in God my Saviour.
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
For he hath regarded the low estate of his handmaiden: for, behold, from henceforth all generations shall call me blessed.
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
For he that is mighty hath done to me great things; and holy is his name.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
And his mercy is on them that fear him from generation to generation.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
He hath shewed strength with his arm; he hath scattered the proud in the imagination of their hearts.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
He hath put down the mighty from their seats, and exalted them of low degree.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
He hath filled the hungry with good things; and the rich he hath sent empty away.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
He hath holpen his servant Israel, in remembrance of his mercy;
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
As he spake to our fathers, to Abraham, and to his seed for ever. (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
And Mary abode with her about three months, and returned to her own house.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
Now Elisabeth’s full time came that she should be delivered; and she brought forth a son.
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
And her neighbours and her cousins heard how the Lord had shewed great mercy upon her; and they rejoiced with her.
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
And it came to pass, that on the eighth day they came to circumcise the child; and they called him Zacharias, after the name of his father.
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
And his mother answered and said, Not so; but he shall be called John.
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
And they said unto her, There is none of thy kindred that is called by this name.
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
And they made signs to his father, how he would have him called.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
And he asked for a writing tablet, and wrote, saying, His name is John. And they marvelled all.
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
And his mouth was opened immediately, and his tongue loosed, and he spake, and praised God.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
And fear came on all that dwelt round about them: and all these sayings were noised abroad throughout all the hill country of Judæa.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
And all they that heard them laid them up in their hearts, saying, What manner of child shall this be! And the hand of the Lord was with him.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
And his father Zacharias was filled with the Holy Ghost, and prophesied, saying,
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
Blessed be the Lord God of Israel; for he hath visited and redeemed his people,
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
And hath raised up an horn of salvation for us in the house of his servant David;
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
As he spake by the mouth of his holy prophets, which have been since the world began: (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
That we should be saved from our enemies, and from the hand of all that hate us;
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
To perform the mercy promised to our fathers, and to remember his holy covenant;
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
The oath which he sware to our father Abraham,
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
That he would grant unto us, that we being delivered out of the hand of our enemies might serve him without fear,
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
In holiness and righteousness before him, all the days of our life.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
And thou, child, shalt be called the prophet of the Highest: for thou shalt go before the face of the Lord to prepare his ways;
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
To give knowledge of salvation unto his people by the remission of their sins,
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
Through the tender mercy of our God; whereby the dayspring from on high hath visited us,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
To give light to them that sit in darkness and in the shadow of death, to guide our feet into the way of peace.
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
And the child grew, and waxed strong in spirit, and was in the deserts till the day of his shewing unto Israel.

< Luka 1 >