< Levitiko 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
I reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
Uzmi Arona i sinove njegove s njim i odijelo i ulje pomazanja i tele za žrtvu radi grijeha i dva ovna i kotaricu prijesnijeh hljebova.
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
I saberi sav zbor pred vrata šatoru od sastanka.
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
I uèini Mojsije kako mu zapovjedi Gospod, i sabra se zbor pred vrata šatoru od sastanka.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
I reèe Mojsije zboru: ovo je zapovjedio Gospod da se uèini.
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
I dovede Mojsije Arona i sinove njegove, i opra ih vodom.
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
I obuèe mu košulju, i opasa ga pojasom, i ogrnu ga plaštem, i metnu mu svrh njega opleæak, i steže oko njega pojas od opleæka, i opasa ga njim.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
I metnu na nj naprsnik, a na naprsnik metnu Urim i Tumim.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
Još mu metnu kapu na glavu, i na kapu metnu sprijed ploèu zlatnu, krunu svetu, kao što zapovjedi Gospod Mojsiju.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
I uze Mojsije ulje pomazanja, i pomaza šator i sve stvari u njemu, i osveti ih.
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
I pokropi njim oltar sedam puta, i pomaza oltar i sve sprave njegove, i umivaonicu i podnožje njezino, da se osveti.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
I izli ulja pomazanja na glavu Aronu, i pomaza ga da se osveti.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
I dovede Mojsije sinove Aronove, i obuèe im košulje, i opasa ih pojasom, i veza im kapice na glave, kao što mu bješe zapovjedio Gospod.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
I dovede tele za grijeh, i Aron i sinovi njegovi metnuše ruke svoje na glavu teletu za grijeh.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
I zakla ga Mojsije, i uzevši krvi njegove pomaza rogove oltaru unaokolo prstom svojim, i oèisti oltar, a ostalu krv izli na podnožje oltaru, i osveti ga da se na njemu èini oèišæenje od grijeha.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
I uze sve salo što je na crijevima, i mrežicu s jetre, i oba bubrega, i salo oko njih, i zapali Mojsije na oltaru.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
A tele s kožom i s mesom i balegom spali ognjem iza okola, kao što bješe Gospod zapovjedio Mojsiju.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
I dovede ovna za žrtvu paljenicu, i Aron i sinovi njegovi metnuše ruke svoje na glavu ovnu;
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
I zakla ga Mojsije, i pokropi krvlju njegovom oltar ozgo unaokolo.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
I isjekavši ovna na dijelove zapali Mojsije glavu i dijelove i salo.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
A crijeva i noge opra vodom, i tako spali Mojsije svega ovna na oltaru; i bi žrtva paljenica za ugodni miris, žrtva ognjena Gospodu, kao što bješe Gospod zapovjedio Mojsiju.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
I dovede drugoga ovna, ovna za posveæenje; i Aron i sinovi njegovi metnuše ruke svoje na glavu ovnu.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
I zaklavši ga Mojsije uze krvi njegove, i pomaza njom kraj desnoga uha Aronu i palac desne ruke njegove i palac desne noge njegove.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
I dovede Mojsije sinove Aronove, pa i njima pomaza istom krvlju kraj desnoga uha i palac desne ruke i palac desne noge; a ostalu krv izli Mojsije po oltaru unaokolo.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
Potom uze salo i rep i sve salo što je na crijevima, i mrežicu s jetre, i oba bubrega, i salo oko njih, i pleæe desno,
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
A iz kotarice u kojoj stajahu prijesni hljebovi pred Gospodom uze jedan kolaè prijesan, i jedan kolaè hljeba s uljem i jednu pogaèu, i metnu na salo i na pleæe desno.
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
I metnu to sve Aronu u ruke, i sinovima njegovijem u ruke, i obrnu tamo i amo za žrtvu obrtanu pred Gospodom.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
Poslije uzevši to iz ruku njihovijeh Mojsije zapali na oltaru svrh žrtve paljenice; to je posveæenje na ugodni miris, žrtva ognjena Gospodu.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
I uze Mojsije grudi, i obrnu ih tamo i amo za žrtvu obrtanu pred Gospodom; i od ovna posvetnoga dopade Mojsiju dio, kao što bješe Gospod zapovjedio Mojsiju.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
I uze Mojsije ulja za pomazanje i krvi koja bješe na oltaru, i pokropi Arona i haljine njegove, i sinove njegove i haljine njihove s njim; i tako posveti Arona i haljine njegove, i sinove njegove i haljine njihove s njim.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
Potom reèe Mojsije Aronu i sinovima njegovijem: kuhajte to meso na vratima šatora od sastanka, i ondje ga jedite i hljeb posvetni što je u kotarici, kao što sam zapovjedio rekavši: Aron i sinovi njegovi neka jedu to.
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
A što ostane mesa ili hljeba, ognjem sažezite.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
I ne izlazite s vrata šatora od sastanka sedam dana, dokle se ne navrše dani posveæenja vašega, jer æete se sedam dana posveæivati.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
Kako je bilo danas, tako je Gospod zapovjedio da se èini, da biste se oèistili od grijeha.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
Zato na vratima šatora od sastanka ostanite danju i noæu za sedam dana, i izvršite što je Gospod zapovjedio da izvršite, da ne pomrete, jer mi je tako zapovjeðeno.
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
I Aron i sinovi njegovi uèiniše sve što bješe Gospod zapovjedio preko Mojsija.

< Levitiko 8 >