< Levitiko 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Opet reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda,
Kad ko zgriješi i uèini zlo djelo Gospodu udarivši u bah bližnjemu svojemu za ostavu ili za stvar predanu u ruke ili otevši što ili zanesavši bližnjega svojega,
3 kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho,
Ili naðe izgubljeno što, pa udari u bah, ili se krivo zakune za koju god stvar koju može èovjek uèiniti i ogriješiti se njom,
4 ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo
Kad tako zgriješi i skrivi, neka vrati što je oteo ili prisvojio prijevarom ili što mu je bilo dano na ostavu ili što je izgubljeno našao,
5 kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse.
Ili za što se zakleo krivo, neka plati cijelo i još dometne peti dio onome èije je; neka mu da onaj dan kad prinese žrtvu za svoj grijeh.
6 Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo.
A na žrtvu za grijeh svoj neka prinese Gospodu ovna zdrava, sa cijenom kojom precijeniš krivicu neka ga dovede svešteniku.
7 Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”
I oèistiæe ga sveštenik pred Gospodom, i oprostiæe mu se svaka stvar koju je uèinio, te skrivio.
8 Yehova anawuza Mose kuti,
I reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
9 “Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse.
Zapovjedi Aronu i sinovima njegovijem, i reci im: ovo je zakon za žrtvu paljenicu: žrtva paljenica neka stoji na ognju na oltaru cijelu noæ do jutra, i oganj na oltaru neka gori jednako.
10 Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo.
Sveštenik neka obuèe svoju haljinu lanenu, i gaæe lanene neka obuèe na tijelo svoje, i neka zgrne pepeo kad oganj spali na oltaru žrtvu paljenicu, i neka ga izruèi kod oltara.
11 Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando.
Potom neka svuèe haljine svoje i obuèe druge haljine, i neka iznese pepeo napolje iz okola na èisto mjesto.
12 Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo.
A oganj što je na oltaru neka gori na njemu, neka se ne gasi, nego neka sveštenik loži na oganj drva svako jutro, i neka namješta na nj žrtvu paljenicu, i neka pali na njemu salo od žrtava zahvalnih.
13 Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.
Oganj neka jednako gori na oltaru, neka se ne gasi.
14 “‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa.
A ovo je zakon za dar: sinovi Aronovi neka ga prinose Gospodu pred oltarom.
15 Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova.
Uzevši šaku bijeloga brašna i ulja od dara i sav kad koji bude na daru, neka zapali na oltaru spomen njegov na ugodni miris Gospodu.
16 Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano.
A što preteèe, neka jede Aron i sinovi njegovi; neka se jede bez kvasca na svetom mjestu; u trijemu šatora od sastanka neka jedu.
17 Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo.
Neka se ne mijesi s kvascem; to im dadoh da im bude dio od žrtava mojih ognjenih; to je svetinja nad svetinjama kao žrtva za grijeh i kao žrtva za prijestup.
18 Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’”
Svako muško izmeðu sinova Aronovijeh neka to jede zakonom vjeènim od koljena do koljena od žrtava koje se pale Gospodu; što se god dotakne toga, biæe sveto.
19 Yehova anawuzanso Mose kuti,
I reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
20 “Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo.
Ovo je žrtva Aronova i sinova njegovijeh, koju æe prinositi Gospodu onaj dan kad se koji pomaže: desetinu efe bijeloga brašna za dar svagdašnji, polovinu ujutru a polovinu uveèe.
21 Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova.
U tavi s uljem neka se gotovi; prženo neka donese; i pržene komade dara neka prinese na ugodni miris Gospodu.
22 Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera.
I sveštenik izmeðu sinova njegovijeh, koji bude pomazan nakon njega, neka èini tako isto zakonom vjeènim; neka se pali Gospodu sve to;
23 Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”
I svaki dar sveštenikov neka se sav spali, a neka se ne jede.
24 Yehova anawuza Mose kuti
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
25 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika.
Kaži Aronu i sinovima njegovijem, i reci: ovo je zakon za žrtvu radi grijeha: na mjestu gdje se kolje žrtva paljenica, neka se kolje i žrtva za grijeh pred Gospodom; svetinja je nad svetinjama.
26 Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano.
Sveštenik koji prinese žrtvu za grijeh neka je jede; na svetom mjestu neka se jede, u trijemu od šatora od sastanka.
27 Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika.
Što se god dotakne mesa njezina, biæe sveto; i ako ko pokapa krvlju njezinom haljinu, ono što pokapa neka opere na svetom mjestu.
28 Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi.
I sud zemljani u kojem bude kuhano neka se razbije; ako li je kuhano u sudu mjedenom, neka se istre i vodom opere.
29 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri.
Svako muško izmeðu sveštenika neka to jede; svetinja je nad svetinjama.
30 Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’”
Ali nijedna žrtva za grijeh, od koje se krv unese u šator od sastanka da se uèini oèišæenje od grijeha u svetinji, neka se ne jede, nego neka se ognjem sažeže.

< Levitiko 6 >