< Levitiko 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
2 “Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda,
and seide, A soule that synneth, and dispisith the Lord, and denyeth to his neiybore a thing bitakun to kepyng, that was bitakun to his feith, ethir takith maisterfuli a thing bi violence, ether makith fals chaleng,
3 kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho,
ether fyndith a thing lost, and denyeth ferthermore and forswerith, and doth ony other thing of manye in whiche thingis men ben wont to do synne,
4 ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo
`if it is conuict of the gilt,
5 kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse.
it schal yelde hool alle thingis whiche it wolde gete bi fraude, and ferthermore the fyuethe part to the lord, to whom it dide harm.
6 Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo.
Sotheli for his synne it schal offre a ram vnwemmed of the floc, and it schal yyue that ram to the preest, bi the valu and mesure of the trespas;
7 Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”
and the preest schal preie for hym bifor the Lord, and it schal be foryouun to hym, for alle thingis whiche he synnede in doyng.
8 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide,
9 “Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse.
Comaunde thou to Aaron, and to hise sones, This is the lawe of brent sacrifice; it schal be brent in the auter al nyyt til the morewe; fier that is youun fro heuene schal be of the same auter.
10 Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo.
The preest schal be clothid with a coote, and `pryuy lynnun clothis; and he schal take awei the aischis, which the fier deuourynge brente, and he schal putte bisidis the auter;
11 Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando.
and he schal be spuylid of the formere clothis, and he schal be clothid with other, and schal bere aischis out of the castels, and in a moost clene place he schal make tho to be wastid til to a deed sparcle.
12 Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo.
Forsothe fier schal brenne euere in the auter, which fier the preest schal nurische, puttynge trees vndur, in the morewtid bi ech dai; and whanne brent sacrifice is put aboue, the preest schal brenne the ynnere fatnessis of pesible thingis.
13 Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.
This is euerlastynge fier, that schal neuer faile in the auter.
14 “‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa.
This is the lawe of sacrifice, and of fletynge offryngis, whiche `the sones of Aaron schulen offre bifore the Lord, and bifor the auter.
15 Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova.
The preest schal take an handful of wheete flour, which is spreynd with oile, and al the encense which is put on the wheete flour, and he schal brenne it in the auter, in to mynde of swettist odour to the Lord.
16 Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano.
Forsothe Aaron with hise sones schal ete the tother part of wheete flour, without sour dow; and he schal ete in the hooli place of the greet street of the tabernacle.
17 Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo.
Sotheli herfor it schal not be `diyt with sour dow, for a part therof is offrid in to encense of the Lord; it schal be hooli `of the noumbre of holi thingis, as for synne and for trespas.
18 Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’”
Malis oonli of the kynrede of Aaron schulen ete it; it is a lawful thing and euerlastynge in youre generaciouns, of the sacrifice of the Lord; ech man that touchith tho schal be halewyd.
19 Yehova anawuzanso Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
20 “Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo.
and seide, This is the offryng of Aaron, and of hise sones, which thei owen offre to the Lord in the day of her anoyntyng; thei schulen offre the tenthe part of ephi of wheete flour, in euerlastynge sacrifice, the myddis therof in the morewtid, and the myddis therof in the euentid;
21 Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova.
which schal be spreynt with oile in the friyng panne, and schal be fried.
22 Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera.
Sotheli the preest which is successour to the fadir `bi riyt, schal offre it hoot, in to sweteste odour to the Lord; and al it schal be brent in the auter.
23 Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”
For al the sacrifice of preestis schal be wastid with fier, nether ony man schal ete therof.
24 Yehova anawuza Mose kuti
And the Lord spak to Moises, and seide,
25 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika.
Spek thou to Aaron and to hise sones, This is the lawe of sacrifice for synne; it schal be offrid bifor the Lord, in the place where brent sacrifice is offrid; it is hooli `of the noumbre of hooli thingis.
26 Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano.
The preest that offrith it, schal ete it in the hooli place, in the greet street of the tabernacle.
27 Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika.
What euer thing schal touche the fleischis therof, it schal be halewid; if a cloth is bispreynt of the blood therof, it schal be waischun in the hooli place.
28 Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi.
Sotheli the erthun vessel, in which it is sodun, schal be brokun; that if the vessel is of bras, it schal be scourid, and `schal be waischun with watir.
29 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri.
Ech male of preestis kyn schal ete of the fleischis therof; for it is hooli `of the noumbre of hooli thingis.
30 Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’”
Sotheli the sacrifice which is slayn for synne, whos blood is borun in to the tabernacle of witnessyng to clense in the seyntuarie, schal not be etun, but it schal be brent in fier.

< Levitiko 6 >