< Levitiko 4 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:
Kaži sinovima Izrailjevim, i reci: ako ko zgriješi nehotice i uèini štogod što je Gospod zabranio da se ne èini,
3 “‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake.
Ako sveštenik pomazani zgriješi, te bude na grijeh narodu, neka za grijeh svoj koji je uèinio prinese tele zdravo Gospodu na žrtvu za grijeh.
4 Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova.
I dovedavši tele na vrata šatoru od svjedoèanstva pred Gospoda, neka metne ruku svoju teletu na glavu, i zakolje tele pred Gospodom.
5 Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
I neka uzme sveštenik pomazani krvi od teleta, i unese je u šator od sastanka.
6 Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika.
I neka zamoèi sveštenik prst svoj u krv, i krvlju sedam puta pokropi pred Gospodom pred zavjesom od svetinje.
7 Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
I neka pomaže sveštenik tom krvlju rogove oltaru, na kom se kadi mirisima pred Gospodom u šatoru od sastanka, a ostalu krv od teleta svu neka izlije na podnožje oltaru, na kom se pale žrtve na vratima šatora od sastanka.
8 Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo.
I neka izvadi sve salo iz teleta za grijeh, salo što pokriva crijeva i sve salo što je na crijevima;
9 Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo
I oba bubrega, i salo što je na njima i na slabinama, i mrežicu na jetri s bubrezima neka izvadi,
10 monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza.
Onako kako se vadi iz goveèeta za žrtvu zahvalnu; i neka zapali sveštenik na oltaru, na kom se žrtva pali.
11 Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo,
A kožu od teleta i sve meso s glavom i s nogama i crijeva i balegu,
12 kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.
I cijelo tele neka iznese napolje iz okola na èisto mjesto, gdje se prosipa pepeo, i neka ga spali ognjem na drvima; na mjestu gdje se prosipa pepeo neka se spali.
13 “‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu.
Ako li bi sav zbor sinova Izrailjevih zgriješio nehotice i ne bi zbor znao za to, i uèinili bi štogod što je Gospod zabranio da se ne èini, te bi skrivili,
14 Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
Kad se dozna za grijeh koji su uèinili, onda neka zbor prinese tele na žrtvu za grijeh, i neka ga dovedu pred šator od sastanka.
15 Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova.
I starješine od zbora neka metnu teletu na glavu ruke svoje pred Gospodom, i sveštenik neka zakolje tele pred Gospodom.
16 Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
I sveštenik pomazani neka unese krvi od teleta u šator od sastanka,
17 Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga.
I neka sveštenik zamoèi prst svoj u krv, i sedam puta pokropi pred Gospodom pred zavjesom.
18 Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
I tom krvlju neka pomaže rogove oltaru koji je pred Gospodom u šatoru od sastanka, a ostalu krv svu neka izlije na podnožje oltaru na kom se pali žrtva, na vratima šatora od sastanka.
19 Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa,
A sve salo izvadivši iz njega neka zapali na oltaru.
20 ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa.
I s tijem teletom neka èini onako kako èini s teletom za svoj grijeh, tako neka uèini s njim; tako æe ih sveštenik oèistiti od grijeha, i oprostiæe im se.
21 Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.
A tele neka iznese napolje iz okola, i spali ga kao i prvo tele; to je žrtva za grijeh svega zbora.
22 “‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula.
Ako li poglavar zgriješi, i uèini nehotice štogod što je Gospod Bog njegov zabranio da se ne èini, te skrivi,
23 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake.
Kad dozna za grijeh svoj, koji je uèinio, tada neka dovede na žrtvu jare muško, zdravo.
24 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo.
I neka metne ruku svoju jaretu na glavu, i sveštenik neka ga zakolje gdje se kolje žrtva paljenica pred Gospodom; to je žrtva za grijeh.
25 Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo.
I neka uzme sveštenik krvi od žrtve za grijeh na prst svoj, i pomaže rogove oltaru na kom se žrtva pali; a ostalu krv neka izlije na podnožje oltaru na kom se žrtva pali.
26 Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.
A sve salo neka zapali na oltaru kao salo od žrtve zahvalne; i tako æe ga oèistiti sveštenik od grijeha njegova, i oprostiæe mu se.
27 “‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula.
Ako li ko iz prostoga naroda zgriješi nehotice, i uèini štogod što je Gospod zabranio da se ne èini, te skrivi,
28 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo.
Kad dozna za grijeh svoj, koji je uèinio, tada neka dovede na žrtvu jare žensko zdravo za grijeh, koji je uèinio.
29 Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
I neka metne ruku svoju na glavu žrtvi za grijeh, i neka je sveštenik zakolje na mjestu gdje se kolje žrtva paljenica.
30 Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo.
I neka uzme sveštenik krvi od nje na prst svoj, i pomaže rogove oltaru na kom se pali žrtva; a ostalu krv svu neka izlije na podnožje oltaru.
31 Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.
I sve salo iz nje neka izvadi kao što se vadi salo iz žrtve zahvalne, i neka ga zapali sveštenik na oltaru za ugodni miris Gospodu; a tako æe ga oèistiti od grijeha sveštenik, i oprostiæe mu se.
32 “‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema.
Ako li bi doveo izmeðu ovaca na žrtvu za grijeh, neka dovede žensko zdravo.
33 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
I neka metne ruku svoju na glavu žrtvi za grijeh, i neka je sveštenik zakolje na mjestu gdje se kolje žrtva paljenica.
34 Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo.
I neka uzme sveštenik krvi od žrtve za grijeh na prst svoj, i neka pomaže rogove oltaru na kom se pali žrtva; a ostalu krv svu neka izlije na podnožje oltaru.
35 Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.
I sve salo neka izvadi kao što se vadi salo iz jagnjeta za žrtvu zahvalnu; i neka ga sveštenik zapali na oltaru za žrtvu ognjenu Gospodu; i tako æe ga oèistiti sveštenik od grijeha njegova, koji je uèinio, i oprostiæe mu se.

< Levitiko 4 >