< Levitiko 27 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Potem PAN powiedział do Mojżesza:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
Przemów do synów Izraela i powiedz im: Jeśli ktoś złoży PANU szczególny ślub, [da okup] według twojego oszacowania.
3 mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
A [takie] będzie twoje oszacowanie: Za mężczyznę w wieku od dwudziestu do sześćdziesięciu lat będzie wynosiło pięćdziesiąt syklów srebra według sykla świątynnego.
4 Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
A jeśli to jest kobieta, twoje oszacowanie będzie wynosiło trzydzieści syklów;
5 Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
A jeśli to będzie ktoś w wieku od pięciu do dwudziestu lat, wtedy twoje oszacowanie za osobę płci męskiej będzie wynosiło dwadzieścia syklów, a za osobę płci żeńskiej – dziesięć syklów.
6 Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
A jeśli to jest dziecko w wieku od [jednego] miesiąca do pięciu lat, wtedy twoje oszacowanie za chłopca będzie wynosiło pięć syklów srebra, a za dziewczynkę twoje oszacowanie będzie wynosiło trzy sykle srebra.
7 Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
A jeśli to jest ktoś w wieku od sześćdziesięciu lat wzwyż, jeśli to jest mężczyzna, wtedy twoje szacowanie będzie wynosiło piętnaście syklów, a za kobietę – dziesięć syklów.
8 Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
Lecz jeśli jest tak ubogi, że nie może zapłacić twego oszacowania, wtedy postawią go przed kapłanem i kapłan go oszacuje. Według możności tego, który ślubował, oszacuje go kapłan.
9 “‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
Jeśli to, co będzie PANU składane w ofierze, jest ze zwierząt, to wszystko z tego, które będzie oddane PANU, będzie święte;
10 Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
Nie zamieni go ani nie zastąpi go czym innym, ani lepszego gorszym, ani gorszego lepszym. Jeśli jednak nawet zastąpi zwierzę innym zwierzęciem, to ono i to, czym [zostało] zastąpione, będzie święte.
11 Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
A jeśli to będzie nieczyste zwierzę, którego nie składa się PANU w ofierze, wtedy stawi to zwierzę przed kapłanem;
12 ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
I kapłan je oszacuje, według tego, czy [jest] dobre, czy marne. Jak ty, kapłanie, je oszacujesz, tak będzie.
13 Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
A jeśli zechce je wykupić, to doda jedną piątą do twojego oszacowania.
14 “‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
Jeśli ktoś poświęci swój dom, żeby był święty dla PANA, wtedy kapłan oszacuje go według tego, czy jest dobry, czy marny. Jak kapłan go oszacuje, tak zostanie.
15 Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
A jeśli ten, który poświęcił, zechce wykupić swój dom, to doda jedną piątą wartości twego oszacowania i [dom] będzie jego.
16 “‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
Jeśli ktoś poświęci PANU część pola swojej posiadłości, wtedy twoje oszacowanie będzie według ilości wysianego ziarna; chomer jęczmienia odpowiada pięćdziesięciu syklom srebra.
17 Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
Jeśli poświęcił swoje pole do roku jubileuszowego, to zostanie według twego oszacowania.
18 Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
Ale jeśli poświęcił swoje pole po roku jubileuszowym, wtedy kapłan obliczy mu pieniądze według lat, które zostają do roku jubileuszowego, i zostanie to odjęte od twego szacowania.
19 Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
A jeśli ten, który poświęcił pole, zechce je wykupić, to doda jedną piątą wartości twego oszacowania i [pole] będzie jego.
20 Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
Ale jeśli nie wykupi pola, lecz będzie ono sprzedane komuś innemu, nie może być już wykupione.
21 Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
I to pole, gdy stanie się wolne w roku jubileuszowym, będzie święte dla PANA jako pole poświęcone; stanie się posiadłością kapłana.
22 “‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
A jeśli ktoś poświęca PANU kupione pole, które nie należy do pól jego posiadłości;
23 wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
Wówczas kapłan obliczy mu wysokość oszacowania aż do roku jubileuszowego i on tego samego dnia odda [sumę] twego szacowania jako rzecz świętą PANU.
24 Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
A w roku jubileuszowym pole wróci do tego, od którego zostało kupione, do którego posiadłość tej ziemi należy.
25 Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
A każde twoje oszacowanie będzie według sykla świątynnego. Jeden sykl będzie wynosił dwadzieścia ger.
26 “‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
Jednak pierworodnego ze zwierząt, które jako pierworodne należą do PANA, nikt nie poświęci, czy to wołu, czy owcy; należy do PANA.
27 Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
A jeśli będzie ze zwierząt nieczystych, to wykupi je według twego oszacowania i doda do tego jedną piątą; a jeśli nie zostanie wykupione, niech zostanie sprzedane według twego oszacowania.
28 “‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
Natomiast każda rzecz poświęcona, którą kto poświęca PANU ze wszystkiego, co ma – czy to z ludzi, czy ze zwierząt, czy z pola swojej posiadłości – nie będzie sprzedawana ani wykupiona, bo wszelka rzecz poświęcona jest najświętsza dla PANA.
29 “‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
To, co poświęcone, które będzie poświęcone przez człowieka, nie będzie odkupione, [ale] poniesie śmierć.
30 “‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
Wszelka dziesięcina ziemi – czy to z nasienia ziemi, czy z owocu drzewa – należy do PANA. Jest ona poświęcona PANU.
31 Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
Ale jeśli ktoś zechce wykupić [część] swoich dziesięcin, doda do nich jedną piątą.
32 Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
Także wszelka dziesięcina z bydła i z trzody, ze wszystkiego, co przechodzi pod laską [pasterską], każde dziesiąte będzie poświęcone PANU.
33 Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
[Nikt] nie będzie przebierał między dobrym a marnym ani nie będzie go zamieniać; a jeśli je nawet zamieni, to ono i to, na co [zostało] zamienione, będzie święte. Nie można tego wykupić.
34 Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.
To są przykazania, które PAN rozkazał Mojżeszowi dla synów Izraela na górze Synaj.

< Levitiko 27 >