< Levitiko 24 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
Zapovjedi sinovima Izrailjevim neka ti donesu ulja maslinova èista, cijeðena, za vidjelo, da žišci gore vazda.
3 Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
Pred zavjesom svjedoèanstva u šatoru od sastanka Aron æe ih namještati da gore od veèera do jutra pred Gospodom vazda zakonom vjeènim od koljena do koljena.
4 Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
Na svijetnjak èisti namještaæe žiške pred Gospodom vazda.
5 “Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
I uzmi bijeloga brašna, i ispeci dvanaest kolaèa, svaki kolaè da bude od dvije desetine efe.
6 Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
I postavi ih u dva reda, po šest u jedan red, na èistom stolu pred Gospodom.
7 Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
I na svaki red metni kada èistoga, da bude za svaki hljeb spomen, žrtva ognjena Gospodu.
8 Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
Svake subote neka ih postavlja sveštenik pred Gospodom vazda uzimajuæi od sinova Izrailjevih zakonom vjeènim.
9 Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
I biæe Aronovi i sinova njegovijeh, koji æe jesti na mjestu svetom, jer im je svetinja nad svetinjama od ognjenijeh žrtava Gospodnjih zakonom vjeènim.
10 Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
A izaðe sin jedne Izrailjke, kojemu je otac bio Misirac, meðu sinove Izrailjeve, i svadi se u okolu sin žene Izrailjke s nekim Izrailjcem.
11 Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
I psujuæi sin žene Izrailjke pohuli ime Božije, te ga dovedoše k Mojsiju; a mati mu bješe po imenu Salomita, kæi Davrijina, od plemena Danova.
12 Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
I metnuše ga u zatvor dokle im se kaže šta æe èiniti s njim po rijeèi Gospodnjoj.
13 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
A Gospod reèe Mojsiju govoreæi:
14 “Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
Izvedi toga psovaèa napolje iz okola, i neka svi koji su èuli metnu ruke svoje na glavu njegovu, i neka ga sav narod zaspe kamenjem.
15 Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
A sinovima Izrailjevim kaži i reci: ko bi god pohulio Boga svojega, nosiæe grijeh svoj.
16 Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
Ko bi ružio ime Gospodnje, da se pogubi, sav narod da ga zaspe kamenjem; i došljak i domorodac koji bi ružio ime Gospodnje, da se pogubi.
17 “‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
I ko ubije èovjeka, da se pogubi.
18 Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
A ko ubije živinèe, neka vrati drugo, živinèe za živinèe.
19 Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
I ko rani bližnjega svojega, kako uèini tako da mu bude:
20 kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
Ulom za ulom, oko za oko, zub za zub; kako ošteti tijelo èovjeku, onako da mu se uèini.
21 Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
Ko ubije živinèe, da vrati drugo; ali ko ubije èovjeka, da se pogubi.
22 Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Zakon da vam je jedan, došljaku da bude kao i roðenom u zemlji. Jer sam ja Gospod Bog vaš.
23 Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.
I Mojsije kaza sinovima Izrailjevim, a oni izvedoše psovaèa napolje iz okola, i zasuše ga kamenjem; i uèiniše sinovi Izrailjevi kako Gospod zapovjedi Mojsiju.

< Levitiko 24 >