< Levitiko 23 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
Kaži sinovima Izrailjevim, i reci im: praznici Gospodnji, koje æete zvati sveti sabori, ovo su praznici moji:
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
Šest dana radi, a sedmi dan, koji je subota za poèivanje, neka bude sveti sabor, ne radite nijednoga posla; subota je Gospodnja po svijem stanovima vašim.
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
Ovo su praznici Gospodnji, sabori sveti, na koje æete se sabirati u vrijeme njihovo:
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
Èetrnaestoga dana prvoga mjeseca uveèe pasha je Gospodnja.
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
A petnaestoga dana istoga mjeseca praznik je prijesnijeh hljebova Gospodu; sedam dana jedite hljebove prijesne.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
Prvi dan neka vam bude sabor sveti, nikakvoga posla ropskoga ne radite.
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
Nego za sedam dana prinosite Gospodu žrtve ognjene; a sedmi dan neka je sabor sveti; ne radite nijednoga posla ropskoga.
9 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
Kaži sinovima Izrailjevim, i reci im: kad doðete u zemlju koju æu vam dati, i stanete žeti u njoj, tada donesite snop prvina od žetve svoje k svešteniku;
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
A on neka obræe snop pred Gospodom, da bi vam se primio; sjutradan po suboti neka ga obræe sveštenik.
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
A isti dan kad budete obrtali snop, prinesite jagnje od godine dana zdravo na žrtvu paljenicu Gospodu;
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
I dar uza nj, dvije desetine efe bijeloga brašna zamiješena s uljem, da bude žrtva ognjena Gospodu na ugodni miris; i naljev uza nj, vina èetvrt ina.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
A hljeba, ni zrna pržena ni zrna u klasu nemojte jesti do onoga dana kad prinesete žrtvu Bogu svojemu; to da vam je vjeèna uredba od koljena do koljena po svijem stanovima vašim.
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
Potom od prvoga dana po suboti, od dana kad prinesete snop za žrtvu obrtanu, brojte sedam nedjelja punijeh;
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
Do prvoga dana po sedmoj nedjelji nabrojte pedeset dana; onda prinesite nov dar Gospodu.
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
Iz stanova svojih donesite dva hljeba za žrtvu obrtanu; od dvije desetine efe bijeloga brašna da budu, s kvascem neka budu peèeni; to su prvine Gospodu.
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
A s tijem hljebom prinesite sedam jaganjaca od godine zdravijeh, i jedno tele i dva ovna, da bude žrtva paljenica Gospodu s darovima svojim i naljevima svojim, da bude žrtva ognjena na ugodni miris Gospodu.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
Zakoljite i jarca jednoga za grijeh i dva jagnjeta od godine za žrtvu zahvalnu.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
I sveštenik neka to obrne tamo i amo s hljebom od prvina i sa dva jagnjeta na žrtvu obrtanu pred Gospodom; i biæe svete stvari Gospodu za sveštenika.
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
I saberite se u taj dan, sabor sveti da vam je; nijednoga posla ropskoga ne radite zakonom vjeènim po svijem stanovima svojim od koljena do koljena.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
A kad stanete žeti u zemlji svojoj, nemoj sasvijem požeti njive svoje, ni pabirèi po žetvi; ostavi siromahu i došljaku; ja sam Gospod Bog vaš.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
Kaži sinovima Izrailjevim, i reci: prvi dan sedmoga mjeseca neka vam je odmor, spomen trubni, sabor sveti.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
Nijednoga posla ropskoga nemojte raditi, nego prinesite žrtvu ognjenu Gospodu.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
A deseti je dan toga mjeseca sedmoga dan oèišæenja; sabor sveti neka vam je, i muèite duše svoje, i prinesite Gospodu žrtvu ognjenu.
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
U taj dan nemojte raditi nijednoga posla, jer je dan oèišæenja, da se oèistite pred Gospodom Bogom svojim.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
A svaka duša koja se ne bi muèila u taj dan, da se istrijebi iz naroda svojega.
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
I svaku dušu koja bi radila kakav posao u taj dan, ja æu zatrti dušu onu u narodu njezinu.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Nijednoga posla nemojte raditi; to da je vjeèna uredba od koljena do koljena u svijem stanovima vašim.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
Subota poèivanja neka vam bude, i muèite duše svoje; devetoga dana istoga mjeseca kad bude veèe, od veèera do veèera praznujte poèinak svoj.
33 Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
Kaži sinovima Izrailjevim, i reci: petnaestoga dana sedmoga mjeseca praznik je sjenica za sedam dana Gospodu.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
Prvi dan neka bude sabor sveti, nijednoga posla ropskoga nemojte raditi.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
Za sedam dana prinosite žrtve ognjene Gospodu; osmi dan neka vam bude sabor sveti, i prinesite žrtve ognjene Gospodu; praznik je, nijednoga posla ropskoga nemojte raditi.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
To su praznici Gospodnji, koje æete praznovati na saborima svetim da prinesete žrtve ognjene Gospodu: žrtvu paljenicu i dar i žrtvu zahvalnu i naljev, sve kad je èemu dan,
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
Osim subota Gospodnjih i osim darova vaših i osim svijeh zavjeta vaših i osim svijeh dobrovoljnijeh prinosa vaših, koje æete davati Gospodu.
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
Ali petnaesti dan toga mjeseca sedmoga, kad saberete rod zemaljski, praznujte praznik Gospodu sedam dana; u prvi je dan odmor i u osmi je dan odmor.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
U prvi dan uzmite voæa s lijepijeh drveta, i grana palmovijeh i grana s gustijeh drveta i vrbe s potoka, i veselite se pred Gospodom Bogom svojim sedam dana.
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
I praznujte taj praznik Gospodu sedam dana svake godine zakonom vjeènim od koljena do koljena, sedmoga mjeseca praznujte ga.
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
I pod sjenicama budite sedam dana, ko je god roðen u Izrailju neka bude pod sjenicama,
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Da bi znalo natražje vaše da sam ja uèinio da žive pod sjenicama sinovi Izrailjevi kad sam ih izveo iz zemlje Misirske. Ja sam Gospod Bog vaš.
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
I Mojsije kaza praznike Gospodnje sinovima Izrailjevijem.

< Levitiko 23 >