< Levitiko 23 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
I PAN powiedział do Mojżesza:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
Przemów do synów Izraela i powiedz im: Uroczyste święta PANA, które będziecie ogłaszać jako święte zgromadzenia. One są moimi uroczystymi świętami.
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
Przez sześć dni będziecie wykonywać pracę, ale siódmy dzień będzie szabatem odpoczynku, świętym zgromadzeniem, nie będziecie wykonywać [wtedy] żadnej pracy. Jest to szabat PANA we wszystkich waszych domach.
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
Oto uroczyste święta PANA, święte zgromadzenia, które będziecie ogłaszać w ich oznaczonych porach:
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
W pierwszym miesiącu, czternastego dnia [tego miesiąca], o zmierzchu, jest Pascha PANA.
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
A piętnastego dnia tego miesiąca [będzie] Święto Przaśników dla PANA. Przez siedem dni będziecie jeść przaśne chleby.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
Pierwszego dnia będziecie mieć święte zgromadzenie. Nie będziecie wykonywać żadnej uciążliwej pracy.
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
Lecz będziecie składali PANU ofiarę spalaną przez siedem dni. Siódmego dnia będzie święte zgromadzenie. Nie będziecie wykonywać żadnej ciężkiej pracy.
9 Yehova anawuza Mose kuti,
I PAN powiedział do Mojżesza:
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
Przemów do synów Izraela i powiedz im: Gdy wejdziecie do ziemi, którą wam daję, i będziecie zbierać plony, wtedy przyniesiecie do kapłana snop z pierwocin waszego plonu.
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
I on będzie kołysał tym snopem przed PANEM, aby był przyjęty za was. Nazajutrz po sabacie kapłan będzie nim kołysał.
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
W dniu kołysania tym snopem złożycie w ofierze rocznego baranka bez skazy jako całopalenie dla PANA;
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
Wraz z nim na ofiarę pokarmową dwie dziesiąte efy mąki pszennej zmieszanej z oliwą jako ofiarę spalaną PANU na miłą woń, a do tego także ofiarę z płynów, jedną czwartą hinu wina.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Nie będziecie jeść chleba ani prażonego ziarna, ani świeżych kłosów aż do dnia, w którym przyniesiecie ofiarę waszemu Bogu. Będzie to wieczna ustawa przez wszystkie wasze pokolenia, we wszystkich waszych mieszkaniach.
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
I odliczycie sobie od pierwszego dnia po szabacie, od dnia, w którym przynieśliście snop kołysania, siedem pełnych tygodni.
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
Aż do pierwszego dnia po siódmym szabacie odliczycie pięćdziesiąt dni i wtedy złożycie PANU nową ofiarę pokarmową.
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
Przyniesiecie z waszych domów dwa chleby na [ofiarę] kołysania. Będą one z dwóch dziesiątych efy mąki pszennej, upieczone na zakwasie; [to] będą pierwociny dla PANA.
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
Razem z tym chlebem złożycie w ofierze siedem rocznych baranków bez skazy, jednego młodego cielca i dwa barany. Będą one na ofiarę całopalenia dla PANA wraz z ich ofiarą pokarmową i ofiarami z płynów. Będzie to ofiara spalana na miłą woń dla PANA.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
Złożycie też jednego kozła na ofiarę za grzech i dwa roczne baranki na ofiarę pojednawczą.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
I kapłan będzie je kołysał razem z chlebem pierwocin na ofiarę kołysania przed PANEM wraz z dwoma barankami. One będą poświęcone PANU, [przeznaczone] dla kapłana.
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
I ogłosicie w tym dniu święto; będzie to dla was święte zgromadzenie. Nie będziecie wykonywać żadnej uciążliwej pracy. [To będzie] wieczysta ustawa we wszystkich waszych domach, przez wszystkie wasze pokolenia.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
A gdy będziecie zbierać plony waszej ziemi, nie będziesz wycinać doszczętnie skraju twego pola i nie będziesz zbierać pokłosia twoich plonów. Zostawisz je dla ubogiego i przybysza. Ja jestem PAN, wasz Bóg.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
PAN dalej mówił do Mojżesza:
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
Przemów do synów Izraela i powiedz im: W siódmym miesiącu, pierwszego [dnia] tego miesiąca, będziecie mieli szabat, upamiętnienie przez trąbienie, święte zgromadzenie.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
Nie będziecie wykonywać żadnej uciążliwej pracy, lecz złożycie PANU ofiarę spalaną.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
PAN powiedział jeszcze do Mojżesza:
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
Lecz dziesiątego dnia tego siódmego miesiąca będzie Dzień Przebłagania. Będzie to dla was święte zgromadzenie; będziecie trapić swoje dusze i składać PANU ofiarę spalaną.
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
W tym dniu nie będziecie wykonywać żadnej pracy, gdyż jest to Dzień Przebłagania, żeby dokonano dla was przebłagania przed PANEM, waszym Bogiem.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
Każdy bowiem człowiek, który nie będzie trapił swojej duszy tego dnia, zostanie wykluczony ze swego ludu.
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
Także każdego, kto będzie wykonywał jakąkolwiek pracę w tym dniu, zgładzę spośród jego ludu.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Nie będziecie wykonywać żadnej pracy; będzie to wieczysta ustawa przez wszystkie wasze pokolenia, we wszystkich waszych domach.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
Będzie to dla was szabat odpoczynku i będziecie trapić swoje dusze. Dziewiątego dnia tego miesiąca, wieczorem, od wieczora aż do wieczora, będziecie obchodzić wasz szabat.
33 Yehova anawuza Mose kuti,
PAN dalej mówił do Mojżesza:
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
Przemów do synów Izraela i powiedz im: Piętnastego dnia tego siódmego miesiąca będzie Święto Namiotów przez siedem dni dla PANA.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
Pierwszego dnia będzie święte zgromadzenie. Nie będziecie wykonywać żadnej uciążliwej pracy.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
Przez siedem dni będziecie składać PANU ofiarę spalaną. Ósmego dnia będziecie mieć święte zgromadzenie i będziecie składać PANU ofiarę spalaną. Jest to święto, żadnej uciążliwej pracy nie będziecie wykonywać.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
To są święta PANA, które ogłosicie jako święte zgromadzenia, abyście składali PANU ofiarę spalaną, całopalenie, ofiarę pokarmową, ofiarę [pojednawczą] i ofiary z płynów, każdą w swój dzień;
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
Oprócz szabatów PANA, oprócz waszych darów, oprócz wszystkich waszych ślubów i wszystkich waszych dobrowolnych ofiar, które będziecie składać PANU.
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
Piętnastego dnia siódmego miesiąca, gdy zbierzecie plony ziemi, będziecie obchodzili święto dla PANA przez siedem dni; w pierwszym dniu będzie odpoczynek, także w ósmym dniu będzie odpoczynek.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
Pierwszego dnia weźmiecie sobie owoce z najlepszych drzew, gałązki palmowe, gałązki gęstych drzew i wierzbiny znad potoku i będziecie się weselić przed PANEM, waszym Bogiem, przez siedem dni.
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Będziecie obchodzić to święto dla PANA przez siedem dni, co rok. Będzie to wieczysta ustawa przez wszystkie wasze pokolenia. W siódmym miesiącu będziecie je obchodzić.
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
Przez siedem dni będziecie mieszkać w szałasach. Wszyscy urodzeni Izraelici będą mieszkać w szałasach;
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Aby wasze pokolenia wiedziały, że kazałem synom Izraela mieszkać w szałasach, gdy wyprowadziłem ich z ziemi Egiptu. Ja jestem PAN, wasz Bóg.
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
I ogłosił Mojżesz synom Izraela te święta PANA.

< Levitiko 23 >