< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
Dis à Aaron et à ses fils, qu'afin de ne pas profaner mon saint nom, il y aura des cas où ils s'abstiendront des choses saintes que me consacrent les enfants d'Israël. Je suis l'Éternel.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Dis-leur: Si dans vos générations futures l'un quelconque de vos descendants s'approche, étant en état d'impureté, des choses saintes que les enfants d'Israël consacrent à l'Éternel, cette personne-là sera éliminée de ma présence. Je suis l'Éternel.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
Tout descendant d'Aaron ayant la lèpre ou un flux ne mangera des choses consacrées qu'après être redevenu pur; de même si quelqu'un a touché ce qui a été souillé par un cadavre, ou a eu un écoulement séminal,
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
ou si quelqu'un a touché un reptile qui le rende impur
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
ou un homme entaché d'une souillure quelconque, celui qui aura touché ces objets, sera jusqu'au soir en état d'impureté, et ne mangera pas des choses consacrées, mais il baignera son corps dans l'eau;
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
et après le coucher du soleil il sera en état de pureté et pourra ensuite manger des choses saintes; car c'est sa nourriture.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
Il ne mangera pas d'une bête morte ou déchirée afin de ne pas en être souillé. Je suis l'Éternel.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
Qu'ils observent ainsi ce qu'ils ont à observer envers moi, afin de ne pas se mettre sous le poids d'un péché et de ne pas mourir pour s'être profanés par là. Je suis l'Éternel qui les consacre.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
Nul étranger ne mangera des choses saintes; celui qui n'est qu'attaché au service d'un prêtre et le mercenaire ne mangeront point des choses saintes.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
Mais si un Prêtre a acheté un esclave à prix d'argent, celui-ci en mangera, ainsi que l'esclave né dans la maison; ceux-là pourront manger de son pain.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
Et si la fille d'un Prêtre se marie à un homme d'une autre tribu, elle ne pourra pas manger des choses saintes offertes par élévation.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
Mais si la fille d'un Prêtre devient veuve ou est répudiée, et qu'elle n'ait point d'enfants, et qu'elle revienne habiter la maison de son père comme dans sa jeunesse, elle pourra manger du pain de son père; mais nul étranger n'en mangera.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
Et si quelqu'un par mégarde mange des choses saintes, il restituera au Prêtre la chose consacrée en y ajoutant un cinquième.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
Et ils ne profaneront point les choses saintes des enfants d'Israël, ce qu'ils offrent par élévation à l'Éternel;
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
par là ils les mettraient sous le poids du délit dont ils se rendraient coupables en mangeant ce qu'ils ont consacré; car je suis l'Éternel qui les consacre.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
Parle à Aaron et ses fils et à tous les enfants d'Israël et leur dis: Tout individu de la maison d'Israël ou des étrangers domiciliés en Israël, qui présentera en oblation quelqu'une de leurs victimes votives ou volontaires qu'ils offrent à l'Éternel en holocauste,
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
devra prendre pour la faire agréer une victime sans défaut, un mâle parmi vos bœufs, vos moutons ou vos chèvres;
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
vous n'en offrirez aucune qui ait un défaut, vous ne la feriez pas agréer.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
Et si quelqu'un offre à l'Éternel en sacrifice pacifique pour l'acquit d'un vœu, ou comme don volontaire, une pièce de gros ou de menu bétail, elle doit être sans défaut pour être agréée; il ne doit s'y trouver aucun défaut.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
Celle qui serait aveugle, ou fracturée, ou blessée, ou ulcérée, ou atteinte de la gale ou de la teigne, vous ne la présenterez point à l'Éternel, et n'en ferez point sur l'Autel de sacrifice igné à l'Éternel.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
Le bœuf ou le mouton ayant une excroissance, ou arrêté dans sa croissance, vous pourrez l'offrir comme sacrifice volontaire, mais comme sacrifice votif il ne serait point agréé.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
Tout animal châtré par compression, par contusion, par extraction ou par amputation, vous ne le présenterez point à l'Éternel, et ne le sacrifierez point dans votre pays.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
Et vous ne recevrez de l'enfant de l'étranger aucune victime pareille pour l'offrir comme pain de votre Dieu, car il y a là corruption et il y a là défaut; vous ne pourriez la faire agréer.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
Le bœuf, le mouton ou la chèvre qui naîtra, restera sept jours sous sa mère, et dès le huitième jour et au delà, il sera agréé comme oblation ignée pour l'Éternel.
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Mais bœuf ou mouton vous n'égorgerez pas le petit et sa mère le même jour.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
Et quand vous offrirez un sacrifice de louange à l'Éternel, offrez-le de manière à être agréé.
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Il se mangera le jour même, et vous n'en garderez rien jusqu'au matin. Je suis l'Éternel.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
Observez ainsi mes commandements et pratiquez-les. Je suis l'Éternel.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
Et ne profanez pas mon saint nom, afin que ma sainteté se montre au milieu des enfants d'Israël.
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
Je suis l'Éternel qui vous ai consacrés, qui vous ai tirés du pays d'Egypte pour être votre Dieu. Je suis l'Éternel.

< Levitiko 22 >