< Levitiko 21 >

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
The Lord also said to Moses: Speak to the priests, the sons of Aaron, and you shall say to them: Do not allow a priest to be contaminated by the death of his citizens,
2 Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
except only by his blood-relatives and near-relatives, that is, by a father or mother, or by a son or daughter, or also a brother,
3 kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
or a virgin sister, who is not married to a husband.
4 Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
But not even by the leader of his people shall he be contaminated.
5 “‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
Neither shall they shave their head or their beard, and they shall not make incisions in their flesh.
6 Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
They shall be holy to their God, and they shall not pollute his name. For they offer the incense of the Lord and the bread of their God, and because of this they shall be holy.
7 “‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
They shall not take as a wife a promiscuous woman, or a prostitute, or her who has been repudiated by her husband. For they are consecrated to their God,
8 Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
and they offer the bread of the presence. Therefore, let them be holy, for I also am holy: the Lord, who sanctifies them.
9 “‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
If the daughter of a priest will have been taken into prostitution, and will have violated the name of her father, she shall be consumed by fire.
10 “‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
The high priest, that is, the priest who is the greatest among his brothers, upon whose head the oil of anointing has been poured, and whose hands have been consecrated for the priesthood, and who has been vested with the holy vestments: he shall not expose his head; he shall not rend his vestments.
11 Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
And he shall not enter to any dead body whatsoever; likewise, not even by his father or mother shall he be contaminated.
12 Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
Neither shall he exit from the holy places, lest he pollute the Sanctuary of the Lord. For the oil of the holy anointing of his God is upon him. I am the Lord.
13 “‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
He shall take a virgin as his wife.
14 Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
But a widow, or one who has been repudiated or defiled, or also a mistress, he shall not accept, but only a maiden from among his own people.
15 kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
He shall not mingle the stock of his family with the common people of his nation. For I am the Lord, who sanctifies him.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
17 “Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
Say to Aaron: A man from your offspring, throughout their families, who has a blemish, shall not offer the bread to his God.
18 Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
Neither shall he approach to minister to him: if he is blind, if he is lame, if he is small, or large, or has a crooked nose,
19 munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
if his foot or hand is broken,
20 kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
if he has a bulging back or bleary eyes, or if he has a white spot in his eye, or a chronic scab, or a skin disease on his body, or a hernia.
21 Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
Anyone from the offspring of Aaron, the priest, who has a blemish, shall not approach to offer sacrifices to the Lord, nor the bread to his God.
22 Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
Nevertheless, he shall eat from the loaves which are offered in the Sanctuary.
23 Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
But even so, he may not enter within the veil, nor approach to the altar. For he has a blemish, and he must not contaminate my Sanctuary. I am the Lord, who sanctifies them.
24 Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.
Therefore, Moses spoke to Aaron, and to his sons, and to all of Israel, everything that had been commanded to him.

< Levitiko 21 >