< Levitiko 2 >

1 “‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
A kad ko hoæe da prinese na žrtvu Gospodu dar, bijelo brašno neka bude žrtva njegova, i neka je polije uljem i metne na nju kad.
2 ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
I neka je donese sinovima Aronovijem sveštenicima, i neka sveštenik uzme toga brašna punu šaku i ulja i sav kad, i neka to zapali sveštenik na oltaru za spomen njezin; to je žrtva ognjena na ugodni miris Gospodu.
3 Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
A što ostane od toga dara, neka bude Aronu i sinovima njegovijem; to je svetinja nad svetinjama izmeðu žrtava koje se pale Gospodu.
4 “‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
Ako li hoæeš da prineseš dar peèen u peæi, neka budu pogaèe prijesne od bijeloga brašna, zamiješene s uljem, ili kolaèi prijesni, namazani uljem.
5 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
Ako li ti je dar peèeno što u tavi, neka je od bijeloga brašna bez kvasca zamiješeno s uljem.
6 Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
Razlomi ga na dijelove, i polij uljem; to je dar.
7 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Ako li ti je dar gotovljen u kotliæu, neka je od bijeloga brašna s uljem.
8 Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
I donesi dar koji naèiniš od toga Gospodu, i podaj ga svešteniku, i on æe ga odnijeti na oltar;
9 Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
I uzeæe sveštenik od dara spomen njegov, i zapaliæe ga na oltaru; to je žrtva ognjena na ugodni miris Gospodu.
10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
A što ostane od dara, neka bude Aronu i sinovima njegovijem; to je svetinja nad svetinjama izmeðu žrtava koje se pale Gospodu.
11 “‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
Nijedan dar koji prinosite Gospodu da ne bude s kvascem; jer ni kvasca ni meda ne treba da palite na žrtvu ognjenu Gospodu.
12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
Samo u žrtvi od prvina možete to prinijeti Gospodu; ali na oltar ne meæite za ugodni miris.
13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
A svaki dar koji prinosiš osoli solju, i nemoj ostaviti dara svojega bez soli zavjeta Boga svojega; sa svakim darom svojim prinesi soli.
14 “‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
A kad prinosiš dar od prvina Gospodu, klasove nove osuši na ognju, i što istreš iz klasova novih prinesi na dar od prvina svojih.
15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
I polij ga uljem i kad metni na nj; to je dar.
16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
I sveštenik uzevši istrvenoga žita i ulja sa svijem kadom neka zapali spomen. To je žrtva ognjena Gospodu.

< Levitiko 2 >