< Levitiko 16 >

1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
I reèe Gospod Mojsiju pošto pogiboše dva sina Aronova, a pogiboše kad pristupiše pred Gospoda,
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
I kaza Gospod Mojsiju: reci Aronu bratu svojemu da ne ulazi u svako doba u svetinju za zavjes pred zaklopac koji je na kovèegu, da ne pogine, jer æu se u oblaku nad zaklopcem javljati.
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
S ovijem neka ulazi Aron u svetinju: s juncem za žrtvu radi grijeha i s ovnom za žrtvu paljenicu.
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
Svetu košulju lanenu neka obuèe, i gaæe lanene neka su na tijelu njegovu, i neka se opaše pojasom lanenijem i kapu lanenu neka metne na glavu; to su haljine svete, i neka opere tijelo svoje vodom, pa onda neka ih obuèe.
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
A od zbora sinova Izrailjevijeh neka uzme dva jarca za žrtvu radi grijeha, i jednoga ovna za žrtvu paljenicu.
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
I neka prinese Aron junca svojega na žrtvu za grijeh i oèisti sebe i dom svoj.
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
Potom neka uzme dva jarca, i neka ih metne pred Gospoda na vrata šatora od sastanka.
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
I neka Aron baci ždrijeb za ta dva jarca, jedan ždrijeb Gospodu a drugi ždrijeb Azazelu.
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
I neka Aron prinese na žrtvu jarca na kojega padne ždrijeb Gospodnji, neka ga prinese na žrtvu za grijeh.
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
A jarca na kojega padne ždrijeb Azazelov neka metne živa pred Gospoda, da uèini oèišæenje na njemu, pa neka ga pusti u pustinju Azazelu.
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
I neka Aron prinese junca svojega na žrtvu za grijeh i oèisti sebe i dom svoj, i neka zakolje junca svojega na žrtvu za grijeh.
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
I neka uzme kadionicu punu žeravice s oltara, koji je pred Gospodom, i pune pregršti kada mirisnoga istucanoga, i neka unese za zavjes.
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
I neka metne kad na oganj pred Gospodom, da dim od kada zakloni zaklopac koji je na svjedoèanstvu; tako neæe poginuti.
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
Poslije neka uzme krvi od junca i pokropi s prsta svojega po zaklopcu prema istoku, a pred zaklopcem neka sedam puta pokropi tom krvlju s prsta svojega.
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
I neka zakolje jarca na žrtvu za grijeh narodni, i neka unese krv njegovu za zavjes; i neka uèini s krvlju njegovom kao što je uèinio s krvlju junèijom, i pokropi njom po zaklopcu i pred zaklopcem.
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
I tako æe oèistiti svetinju od neèistota sinova Izrailjevih i od prijestupa njihovijeh u svijem grijesima njihovijem; tako æe uèiniti i u šatoru od sastanka, koji je meðu njima usred neèistota njihovijeh.
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
A niko da ne bude u šatoru od sastanka kad on uðe da èini oèišæenje u svetinji, dokle ne izaðe i svrši oèišæenje za se i za dom svoj i za sav zbor Izrailjski.
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
A neka izaðe k oltaru koji je pred Gospodom, i oèisti ga; i uzevši krvi od junca i krvi od jarca neka pomaže rogove oltaru unaokolo;
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
I neka ga pokropi ozgo istom krvlju s prsta svojega sedam puta; tako æe ga oèistiti i posvetiti ga od neèistota sinova Izrailjevih.
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
A kad oèisti svetinju i šator od sastanka i oltar, tada neka dovede jarca živoga.
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
I metnuvši Aron obje ruke svoje na glavu jarcu živomu, neka ispovjedi nad njim sva bezakonja sinova Izrailjevih i sve prijestupe njihove u svijem grijesima njihovijem, i metnuvši ih na glavu jarcu neka ga da èovjeku spremnom da ga istjera u pustinju.
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
I jarac æe odnijeti na sebi sva bezakonja njihova u pustinju; i pustiæe onoga jarca u pustinju.
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
Potom neka opet uðe Aron u šator od sastanka i svuèe haljine lanene koje je obukao kad je išao u svetinju, i ondje neka ih ostavi.
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
Pa neka opere tijelo svoje na svetom mjestu i obuèe svoje haljine; i izašav neka prinese svoju žrtvu paljenicu i narodnu žrtvu paljenicu, i oèisti sebe i narod.
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
A salo od žrtve za grijeh neka zapali na oltaru.
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
A ko odvede jarca za Azazela, neka opere haljine svoje i okupa tijelo svoje u vodi, pa onda neka uðe u oko.
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
A junca za grijeh i jarca za grijeh, od kojih je krv unesena da se uèini oèišæenje u svetinji, neka iznesu napolje iz okola, i neka spale ognjem kože njihove i meso njihovo i balegu njihovu.
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
A ko ih spali, neka opere haljine svoje i okupa tijelo svoje u vodi, pa onda neka doðe u oko.
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
I ovo neka vam bude vjeèna uredba: deseti dan sedmoga mjeseca muèite duše svoje, i ne radite nikakoga posla, ni domorodac ni došljak koji se bavi meðu vama.
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
Jer u taj dan biva oèišæenje za vas, da se oèistite; biæete oèišæeni od svijeh grijeha svojih pred Gospodom.
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
To neka vam je poèivanje subotno, i muèite duše svoje po uredbi vjeènoj.
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
A sveštenik koji bude pomazan i koji bude osveæen da vrši službu sveštenièku na mjesto oca svojega, on neka oèišæa obukavši se u haljine lanene, haljine svete.
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
I neka oèisti svetinju svetu i šator od sastanka; i oltar neka oèisti; i sveštenike i sav narod sabrani neka oèisti.
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
I ovo neka vam je vjeèna uredba da oèišæate sinove Izrailjeve od svijeh grijeha njihovijeh jedanput u godini. I uèini Mojsije kako mu zapovjedi Gospod.

< Levitiko 16 >