< Levitiko 13 >

1 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
Jošte reèe Gospod Mojsiju i Aronu govoreæi:
2 “Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
Èovjek u koga bi na koži tijela njegova bio otok ili krasta ili bubuljica, i bilo bi na koži tijela njegova nalik na gubu, neka se dovede k Aronu svešteniku ili ka kojemu sinu njegovu svešteniku.
3 Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
I neka sveštenik vidi boljeticu na koži tijela njegova; ako dlaka na boljetici bude pobijeljela i boljetica bude na oèi niža od ostale kože tijela njegova, onda je guba; pa kad je vidi sveštenik proglasiæe ga da je neèist.
4 Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
Ako li bude bijela bubuljica na koži tijela njegova i ne bude na oèi niža od ostale kože niti dlaka na njoj pobijeljela, onda neka zatvori sveštenik za sedam dana èovjeka sa takom boljeticom.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
A sedmoga dana neka vidi sveštenik; ako opazi da je boljetica ostala kako je bila i nije se dalje razišla po koži, neka ga zatvori sveštenik opet za sedam dana.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
I neka ga sveštenik opet vidi sedmoga dana, pa ako opazi da se boljetica smanjala i nije se dalje razišla po koži, proglasiæe ga sveštenik da je èist; krasta je; i on neka opere haljine svoje i biæe èist.
7 Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
Ako li se dalje raširi krasta po koži njegovoj, pošto ga sveštenik vidi i proglasi da je èist, nanovo neka se pokaže svešteniku;
8 Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
Ako vidi sveštenik da se krasta raširila po koži njegovoj, proglasiæe sveštenik da je neèist; guba je.
9 “Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
Kad je guba na èovjeku, neka ga dovedu k svešteniku.
10 Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
I sveštenik neka ga vidi; ako bude bijel otok na koži i dlaka bude pobijeljela, ako bi i zdravo meso bilo na otoku,
11 limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
Guba je zastarjela na koži tijela njegova; zato æe ga sveštenik proglasiti da je neèist, i neæe ga zatvoriti, jer je neèist.
12 “Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
Ako li se guba izaspe po koži i pokriju svu kožu èovjeku od glave do pete, gdje bi god sveštenik oèima pogledao,
13 wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
Kad sveštenik vidi da je guba pokrila svu kožu na njemu, proglasiæe da je èovjek èist, jer je sve pobijeljelo, pa je èist.
14 Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
Ali ako se pokaže na njemu divlje meso, biæe neèist.
15 Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
Pa kad sveštenik vidi divlje meso, proglasiæe ga da je neèist; ono je divlje meso neèisto, guba je.
16 Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
A kad bi se divlje meso promijenilo i pobijeljelo, neka doðe k svešteniku.
17 Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
I kad vidi sveštenik da je boljetica pobijeljela, sveštenik æe proglasiti da je èist; èist je.
18 “Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
Kad u koga na koži bude èir, pa proðe,
19 ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
A poslije na mjestu gdje je bio èir izaðe otok bijel ili bubuljica bijela i crvenkasta, neka se pokaže svešteniku.
20 Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
Ako sveštenik vidi da je na oèi niža od ostale kože i dlaka na njoj pobijeljela, proglasiæe ga sveštenik da je neèist, guba je, izašla je iz èira.
21 Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Ako li sveštenik gledajuæi vidi da nije dlaka na njoj pobijeljela niti je niža od kože, nego se smanjala, onda æe ga zatvoriti sveštenik za sedam dana.
22 Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
Ako se raširi po koži, onda æe ga sveštenik proglasiti da je neèist; bolest je.
23 Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
Ako li ostane na svom mjestu bubuljica i ne raširi se, požiljak je od èira; zato æe ga sveštenik proglasiti da je èist.
24 “Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
Ako se ko po koži ožeže ognjem, pa pošto se zalijeèi ostane bubuljica bijela i crvenkasta ili samo bijela,
25 wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
Neka ga vidi sveštenik; ako dlaka na bubuljici bude pobijeljela i ako na oèi bude niža nego koža, guba je, izašla je iz ožegline; zato æe ga sveštenik proglasiti da je neèist; guba je.
26 Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Ako li sveštenik vidi da na bubuljici nema bijele dlake niti je niža od kože, nego se smanjala, zatvoriæe ga za sedam dana.
27 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
Pa æe je sedmoga dana pogledati sveštenik; ako se bude raširila po koži, tada æe ga sveštenik proglasiti da je neèist; guba je.
28 Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
Ako li bubuljica bude ostala na svom mjestu, i ne bude se raširila po koži, nego se smanjala, onda je rana od toga što se ožegao; zato æe ga sveštenik proglasiti da je èist, jer je požiljak od ožegline.
29 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
Ako u èovjeka ili u žene bude boljetica na glavi ili na bradi,
30 wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
Sveštenik neka vidi boljeticu; ako na oèi bude niža od ostale kože i na njojzi dlaka žuækasta i tanka, sveštenik æe proglasiti da je neèist; ospa je, guba na glavi ili na bradi;
31 Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
A kad sveštenik vidi boljeticu, i opazi da na oèi nije niža od ostale kože i da nema na njoj crne dlake, tada æe zatvoriti sveštenik za sedam dana onoga na kom je ospa.
32 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
Pa kad sveštenik sedmi dan vidi a ospa se nije dalje razišla niti dlaka na njoj požutjela, niti je na oèi ospa niža od kože,
33 wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
Tada neka se obrije, ali ospu da ne obrije, i sveštenik neka zatvori još za sedam dana onoga na kom je ospa.
34 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
I sedmoga dana neka sveštenik opet vidi ospu; ako opazi da se ospa nije dalje razišla po koži niti je na oèi niža od ostale kože, tada æe ga proglasiti sveštenik da je èist, pa neka opere haljine svoje, i biæe èist.
35 Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
Ako li se raširi ospa po koži, pošto bude proglašen da je èist,
36 wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
Tada neka ga vidi sveštenik; ako se bude raširila ospa po koži, neka više ne gleda sveštenik ima li žutijeh dlaka; neèist je.
37 Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
Ako li opazi da je ospa ostala gdje je bila i da je crna dlaka izrasla po njoj, zalijeèila se ospa, èist je, i sveštenik æe proglasiti da je èist.
38 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
Kad u èovjeka ili u žene budu bubuljice po koži tijela njihova, bubuljice bijele,
39 wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
Sveštenik neka vidi; ako na koži tijela njihova budu bijele bubuljice male, bijela je ospa izašla po koži, èist je.
40 “Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
Kome opadne kosa s glave, æelav je, èist je.
41 Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
Ako mu sprijeda opadne kosa s glave, pola je æelav, i èist je.
42 Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
Kad na glavi sasvijem æelavoj ili pola æelavoj bude bijela i crvenkasta boljetica, guba je, izašla na glavi svoj æelavoj ili pola æelavoj.
43 Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
I neka ga vidi sveštenik; ako opazi da je bijel i crvenkast otok na glavi svoj æelavoj ili pola æelavoj nalik na gubu po koži ostaloga tijela,
44 ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
Èovjek je gubav, neèist je, i sveštenik æe ga proglasiti da je neèist; guba mu je na glavi.
45 “Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
A gubavac na kom je ta bolest, neka ide u haljinama razdrtijem i gologlav, i usta neka zastre, i neka vièe: neèist, neèist.
46 Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
Dokle je god bolest na njemu, neka bude neèist; neèist je, neka živi sam, iza okola neka mu bude stan.
47 “Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
I ako na haljini bude guba, na haljini vunenoj ili lanenoj,
48 kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
Ili na osnovi ili na pouèici od lana ili od vune, ili na koži, ili na èem god od kože,
49 ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
I ako boljetica bude zelenkasta ili crvenkasta na haljini ili na koži ili na osnovi ili na pouèici ili na èem god od kože, guba je, i neka se pokaže svešteniku.
50 Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
I kad vidi sveštenik bolest, neka zatvori za sedam dana stvar na kojoj je guba.
51 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
I sedmoga dana ako vidi da se dalje razišla bolest po haljini ili po osnovi ili po pouèici ili po koži ili po èemu god od kože, ljuta je guba bolest ona, stvar je neèista.
52 Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
Zato neka spali onu haljinu ili osnovu ili pouèicu od vune ili od lana, ili što god bude od kože, na èem bude bolest; jer je ljuta guba, ognjem neka se spali.
53 “Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
Ako li opazi sveštenik da se bolest nije razišla po haljini ili po osnovi ili pouèici, ili po èemu god od kože,
54 iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
Tada neka zapovjedi sveštenik da se opere ono na èem je bolest, pa onda neka zatvori opet za sedam dana.
55 Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
Pa neka vidi sveštenik pošto se opere stvar na kojoj je bolest, i ako opazi da bolest nije promijenila boje svoje, ako se i ne bude dalje razišla, stvar je neèista, spali je ognjem; jer je ljuta guba na gornjoj ili na donjoj strani.
56 Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
Ako li vidi sveštenik da se mjesto smanjalo pošto je oprano, onda neka ga otkine od haljine ili od kože ili od osnove ili od pouèice.
57 Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
Ako li se opet pokaže na haljini ili na osnovi ili na pouèici ili na èem god od kože, guba je koja se širi, ognjem spali ono na èem bude.
58 Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
A haljinu ili osnovu ili pouèicu ili što mu drago od kože, kad opereš, pa otide s njega ta bolest, operi još jednom, i biæe èisto.
59 Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.
Ovo je zakon za gubu na haljini vunenoj ili lanenoj, ili na osnovi ili na pouèici, ili na èem god od kože, kako se može znati je li što èisto ili neèisto.

< Levitiko 13 >