< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
Alef: Yo soy un hombre que ve aflicción en la vara de su enojo.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
Alef: Me guió y me llevó en tinieblas, mas no en luz.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Alef: Ciertamente contra mí volvió y revolvió su mano todo el día.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
Bet: Hizo envejecer mi carne y mi piel; quebrantó mis huesos.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
Bet: Edificó contra mí, y me cercó de tósigo y de trabajo.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
Bet: Me asentó en oscuridades, como los muertos para siempre.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
Guímel: Me cercó de seto, y no saldré; agravó mis grillos.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Guímel: Aun cuando clamé y di voces, cerró mi oración.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
Guímel: Cercó de seto mis caminos a piedra tajada, torció mis senderos.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
Dálet: Oso que acecha fue para mí, como león en escondrijos.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
Dálet: Torció mis caminos, y me despedazó; me tornó asolado.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
Dálet: Su arco entesó, y me puso como blanco a la saeta.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
He: Hizo entrar en mis riñones las saetas de su aljaba.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
He: Fui escarnio a todo mi pueblo, canción de ellos todos los días.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
He: Me llenó de amarguras, me embriagó de ajenjos.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
Vau: Me quebró los dientes con cascajo, me cubrió de ceniza.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
Vau: Y mi alma se alejó de la paz, me olvidé del bien.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
Vau: Y dije: Pereció mi fortaleza, y mi esperanza del SEÑOR.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
Zain: Acuérdate de mi aflicción y de mi lloro, del ajenjo y de la hiel.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
Zain: Lo tendrá aún en memoria mi alma, porque en mí está humillada.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
Zain: Esto reduciré a mi corazón, por tanto esperaré.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
Chet: Es por las misericordias del SEÑOR que no somos consumidos, porque nunca decayeron sus misericordias.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
Chet: Nuevas son cada mañana; grande es tu fe.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
Chet: Mi parte es el SEÑOR, dijo mi alma; por tanto a él esperaré.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
Tet: Bueno es el SEÑOR a los que en él esperan, al alma que le buscare.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
Tet: Bueno es esperar callando en la salud del SEÑOR.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
Tet: Bueno es al varón, si llevare el yugo desde su juventud.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
Yod: Se sentará solo, y callará, porque lo llevó sobre sí.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
Yod: Pondrá su boca en el polvo, si por ventura habrá esperanza.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Yod: Dará la mejilla al que le hiriere; se llenará de afrenta.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
Cof: Porque el Señor no desechará para siempre;
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
Cof: Antes si afligiere, también se compadecerá según la multitud de sus misericordias.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
Cof: Porque no aflige ni acongoja de su corazón a los hijos de los hombres.
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
Lámed: Para desmenuzar debajo de sus pies todos los encarcelados de la tierra,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
Lámed: Para hacer apartar el derecho del hombre ante la presencia del Altísimo,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
Lámed: Para trastornar al hombre en su causa, el Señor no lo sabe.
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Mem: ¿Quién será aquel que diga, que vino algo que el Señor no mandó?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Mem: ¿De la boca del Altísimo no saldrá malo ni bueno?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Mem: ¿Por qué tiene dolor el hombre viviente, el hombre en su pecado?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Nun: Escudriñemos nuestros caminos, y busquemos, y volvámonos al SEÑOR.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Nun: Levantemos nuestros corazones con las manos a Dios en los cielos.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
Nun: Nosotros nos hemos rebelado, y fuimos desleales; por tanto tú no perdonaste.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
Sámec: Desplegaste la ira, y nos perseguiste; mataste, no perdonaste.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Sámec: Te cubriste de nube, para que no pasase la oración nuestra.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
Sámec: Raedura y abominación nos tornaste en medio de los pueblos.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
Pe: Todos nuestros enemigos abrieron sobre nosotros su boca.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Pe: Temor y lazo fue para nosotros, asolamiento y quebrantamiento.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Pe: Ríos de aguas echan mis ojos, por el quebrantamiento de la hija de mi pueblo.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
Ayin Mis ojos destilan, y no cesan, porque no hay alivio,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
Ayin Hasta que el SEÑOR mire y vea desde los cielos.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Ayin Mis ojos contristaron mi alma, por todas las hijas de mi ciudad.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
Tsade: Mis enemigos me dieron caza como a ave, sin razón.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
Tsade: Ataron mi vida en mazmorra, pusieron piedra sobre mí.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Tsade Aguas de avenida vinieron sobre mi cabeza; yo dije: muerto soy.
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
Cof: Invoqué tu nombre, oh SEÑOR, desde la cárcel profunda.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
Cof: Oíste mi voz; no escondas tu oído a mi clamor, para mi respiro.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Cof: Te acercaste el día que te invoqué; dijiste: No temas.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
Resh: Abogaste, Señor, la causa de mi alma; redimiste mi vida.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
Resh: Tú has visto, oh SEÑOR, mi sinrazón; pleitea mi causa.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Resh: Tú has visto toda su venganza; todos sus pensamientos contra mí.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
Sin: Tú has oído la afrenta de ellos, oh SEÑOR, todas sus maquinaciones contra mí;
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
Sin: Los dichos de los que se levantaron contra mí, y su designio contra mí todo el día.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Sin: Su sentarse, y su levantarse mira; yo soy su canción.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Tau: Dales el pago, oh SEÑOR, según la obra de sus manos.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
Tau: Dales ansia de corazón, tu maldición a ellos.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Tau: Persíguelos en tu furor, y quebrántalos de debajo de los cielos, oh SEÑOR.

< Maliro 3 >