< Oweruza 9 >

1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
Wtedy Abimelek, syn Jerubbaala, poszedł do Sychem, do braci swej matki, i mówił do nich oraz do całej rodziny domu ojca swej matki:
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
Powiedzcie do uszu wszystkich przełożonych Sychem: Co jest dla was lepsze: aby panowało nad wami siedemdziesięciu ludzi, wszyscy synowie Jerubbaala, czy żeby panował nad wami jeden człowiek? Pamiętajcie, że jestem z waszej kości i waszego ciała.
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
Wtedy bracia jego matki opowiadali o nim wszystkie te słowa do uszu wszystkich przełożonych Sychem, a ich serce skłoniło się ku Abimelekowi, bo powiedzieli: To jest nasz brat.
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
I dali mu siedemdziesiąt srebrników z domu Baal-Berita, a Abimelek najął za nie ludzi, lekkomyślnych próżniaków, którzy poszli za nim.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
Potem przyszedł do domu swojego ojca w Ofra i na jednym kamieniu zabił swoich braci, synów Jerubbaala, siedemdziesięciu ludzi. Został tylko Jotam, najmłodszy syn Jerubbaala, ponieważ się ukrył.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
Wtedy zebrali się wszyscy mężczyźni Sychem i cały dom Millo, poszli i obwołali Abimeleka królem na równinie, gdzie stał słup w Sychem.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
Gdy doniesiono o tym Jotamowi, poszedł, stanął na szczycie góry Gerizim, podniósł głos i zawołał do nich: Posłuchajcie mnie, panowie Sychem, a was [też] Bóg usłyszy.
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
Zebrały się drzewa, aby namaścić nad sobą króla. I powiedziały do oliwki: Króluj nad nami.
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
Lecz oliwka odpowiedziała: Czy mam porzucić swój tłuszcz, przez który czci się Boga i ludzi, i pójść, aby być postawiona nad drzewami?
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
Potem drzewa powiedziały do drzewa figowego: Chodź ty i króluj nad nami.
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
Lecz drzewo figowe odpowiedziało im: Czy mam porzucić swoją słodycz i wyborny owoc i pójść, aby być postawione nad drzewami?
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
Następnie drzewa powiedziały do winorośli: Chodź ty i króluj nad nami.
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
Lecz winorośl odpowiedziała im: Czy mam porzucić swój moszcz, który cieszy Boga i ludzi, i pójść, aby być postawiona nad drzewami?
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
I wszystkie drzewa powiedziały do ostu: Chodź ty i króluj nad nami.
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
A oset odpowiedział drzewom: Jeśli naprawdę chcecie namaścić mnie na króla nad sobą, chodźcie i chrońcie się w moim cieniu. A jeśli nie, niech ogień wyjdzie z ostu i spali cedry libańskie.
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
Teraz więc, jeśli postąpiliście uczciwie i szczerze, ustanawiając sobie Abimeleka królem, i jeśli dobrze obeszliście się z Jerubbaalem i jego domem i odpłaciliście mu za dobrodziejstwa jego ręki;
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
Mój ojciec walczył bowiem za was i narażał swe życie na niebezpieczeństwo, aby was wyrwać z ręki Midianitów;
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
Wy zaś powstaliście dziś przeciw domowi mego ojca i zabiliście na jednym kamieniu jego synów, siedemdziesięciu ludzi, a syna jego służącej, Abimeleka, ustanowiliście królem nad ludźmi Sychem, dlatego że jest waszym bratem.
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
Jeśli więc uczciwie i szczerze obeszliście się dziś z Jerubbaalem i z jego domem, cieszcie się z Abimeleka, a on niech się też cieszy z was.
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
Lecz jeśli nie, niech wyjdzie ogień z Abimeleka i pożre mężczyzn Sychem i dom Millo; niech też wyjdzie ogień od mężczyzn Sychem i z domu Millo i pożre Abimeleka.
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
Wtedy Jotam umknął, uciekł i przybył do Beer, gdzie mieszkał z obawy przed swym bratem Abimelekiem.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
A gdy Abimelek panował nad Izraelem przez trzy lata;
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
Bóg posłał złego ducha między Abimeleka a mężczyzn Sychem; i mężczyźni Sychem zbuntowali się przeciw Abimelekowi;
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
Aby została pomszczona krzywda dokonana na siedemdziesięciu synach Jerubbaala, aby ich krew spadła na ich brata Abimeleka, który ich zabił, i na mężczyzn Sychem, którzy pomogli mu zabić swoich braci.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
I mężczyźni Sychem zasadzili się na niego na szczycie gór i napadali na każdego, kto przechodził tamtą drogą. I doniesiono o tym Abimelekowi.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
Przyszedł też Gaal, syn Obeda, wraz ze swoimi braćmi, i przybył do Sychem, a mężczyźni Sychem zaufali mu.
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
Potem wyszli na pola, zbierali [plony] swoich winnic, tłoczyli [winogrona] i urządzili zabawę. Następnie weszli do domu swoich bogów, jedli, pili i złorzeczyli Abimelekowi.
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
Wtedy Gaal, syn Obeda, powiedział: Kim jest Abimelek i czym jest Sychem, żebyśmy mu służyli? Czy to nie jest syn Jerubbaala, a Zebul nie jest jego urzędnikiem? Służcie [raczej] mężczyznom Chamora, ojca Sychema. Dlaczego mielibyśmy służyć jemu?
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
Oby kto dał ten lud w moje ręce, abym usunął Abimeleka! I powiedział Abimelekowi: Zbierz sobie wojsko i wyjdź.
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
A gdy Zebul, przełożony tego miasta, usłyszał słowa Gaala, syna Obeda, zapłonął gniewem.
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
I potajemnie wyprawił posłańców do Abimeleka, mówiąc: Oto Gaal, syn Obeda, wraz ze swoimi braćmi przyszedł do Sychem i oto podburzają miasto przeciwko tobie.
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
Wstańcie więc nocą, ty i lud, który jest z tobą, i uczyńcie zasadzkę w polu.
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
A rano, gdy słońce wzejdzie, wstaniesz i uderzysz na miasto. A gdy on i lud, który [jest] z nim, wyjdą przeciwko tobie, uczynisz z nim według swego uznania.
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
Wstał więc w nocy Abimelek wraz z całym ludem, który z nim był, i zasadzili się na Sychem w czterech oddziałach.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
A Gaal, syn Obeda, wyszedł i stanął w samej bramie miasta; wtedy Abimelek wraz z ludem, który z nim był, wyszedł z zasadzki.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
A gdy Gaal zobaczył lud, powiedział do Zebula: Oto lud schodzi ze szczytu gór. Zebul odpowiedział mu: Widzisz cień gór i bierzesz go za ludzi.
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
I Gaal powiedział powtórnie: Oto lud schodzi z góry, a jeden oddział idzie drogą przez równinę Meonenim.
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
Wtedy Zebul powiedział do niego: Gdzież teraz są twoje usta, które mówiły: Kim jest Abimelek, abyśmy mu mieli służyć? Czyż to nie ten lud, którym wzgardziłeś? Wyjdź teraz i walcz z nim.
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
Wyszedł więc Gaal na czele mężczyzn Sychem i walczył z Abimelekiem.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
I Abimelek ścigał go, gdy przed nim uciekał, a poległo wielu rannych aż do samej bramy.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
Potem Abimelek został w Arum. A Zebul wygnał Gaala z jego braćmi tak, że nie mogli mieszkać w Sychem.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
Nazajutrz lud wyszedł w pole i doniesiono o tym Abimelekowi.
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
Wziął więc lud, podzielił go na trzy oddziały i zasadził się w polu; a gdy zobaczył, że lud wychodzi z miasta, uderzył na niego i pobił [go].
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
Abimelek i oddziały, które z nim były, wyruszyli i stanęli u samej bramy miasta, inne dwa oddziały zaś uderzyły na wszystkich, którzy [byli] na polu, i pobiły ich.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
I Abimelek nacierał na miasto przez cały ten dzień, i zdobył je; a lud, który w nim [był], zabił, miasto zaś zburzył i rozsiał na nim sól.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
A kiedy usłyszeli o tym wszyscy mężczyźni, którzy byli w wieży Sychem, weszli do twierdzy domu boga Berit.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
I doniesiono Abimelekowi, że zgromadzili się tam wszyscy mężczyźni z wieży Sychem.
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
Wtedy Abimelek wszedł na górę Salmon, on i cały lud, który z nim był; zabrał ze sobą siekierę, uciął gałąź z drzewa, wziął ją, włożył na swoje ramiona i powiedział do ludu, który z nim był: Co widzicie, że uczyniłem, szybko czyńcie to samo.
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
Każdy więc z całego ludu uciął swoją gałąź i poszedł za Abimelekiem; potem kładli je dokoła twierdzy i spalili nimi twierdzę ogniem. I zginęli tam wszyscy ludzie z wieży Sychem, około tysiąca mężczyzn i kobiet.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
Potem Abimelek poszedł do Tebes, rozbił obóz naprzeciwko Tebes i zdobył je.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
Lecz w środku miasta była potężna wieża, do której uciekli wszyscy mężczyźni, kobiety i wszyscy naczelnicy miasta. Zamknęli ją za sobą i weszli na dach wieży.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
Wtedy Abimelek podszedł aż do samej wieży i nacierał na nią. Kiedy stanął u samych drzwi wieży, chciał ją spalić ogniem.
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
A pewna kobieta zrzuciła kawałek kamienia młyńskiego na głowę Abimeleka i rozbiła mu czaszkę.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
On natychmiast zawołał młodzieńca, który nosił jego broń, i powiedział mu: Dobądź swój miecz i zabij mnie, by nie mówiono o mnie: Kobieta go zabiła. Przebił go więc jego giermek, tak że umarł.
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
A gdy mężczyźni Izraela zobaczyli, że Abimelek umarł, rozeszli się, każdy do swego miejsca.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
Tak Bóg odpłacił Abimelekowi za zło, które wyrządził swemu ojcu, zabijając siedemdziesięciu swych braci.
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
I całe zło mężczyzn Sychem Bóg obrócił na ich głowy. Tak przyszło na nich przekleństwo Jotama, syna Jerubbaala.

< Oweruza 9 >