< Oweruza 9 >

1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
Forsothe Abymelech, the sone of Gerobaal, yede in to Sichem to the britheren of his modir; and he spak to hem, and to al the kynrede of `the hows of his modir, and seide,
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
Speke ye to alle the men of Sichem, What is betere to you, that seuenti men, alle the sones of Gerobaal, be lordis of you, whether that o man be lord to you? and also biholde, for Y am youre boon, and youre fleisch.
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
And the britheren of his modir spaken of hym alle these wordis to alle the men of Sichem; and bowiden her hertis aftir Abymelech, and seiden, He is oure brother.
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
And thei yauen to hym seuenti weiytis of siluer of the temple of Baal Berith; and he hiride to hym therof men pore and hauynge no certeyn dwellynge, and thei sueden hym.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
And he cam in to `the hows of his fadir in Ephra, and killide hise britheren the sones of Gerobaal, `seuenti men, on o stoon. And Joathan, the leste sone of Gerobaal, lefte, and was hid.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
Forsothe alle the men of Sichem, and alle the meynees of the citee of Mello, weren gadirid to gydere, and thei yeden, and maden Abymelech kyng, bysidis the ook that stood in Sichem.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
And whanne this thing was teld to Joathan, he yede, and stood in the cop of the hil Garisym, and cried with `vois reisid, and seide, Ye men of Sichem, here me, so that God here you.
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
Trees yeden to anoynte a kyng on hem; and tho seiden to the olyue tre, Comaunde thou to vs.
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
Whiche answeride, Whether Y may forsake my fatnesse, which bothe Goddis and men vsen, and come, that Y be auaunsid among trees?
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
And the trees seiden to the fige tree, Come thou, and take the rewme on vs.
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
Which answeride to hem, Whether Y may forsake my swetnesse and swetteste fruytis, and go that Y be auaunsid among othere trees?
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
Also `the trees spaken to the vyne, Come thou, and comaunde to vs.
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
Which answeride, Whether Y may forsake my wyn, that gladith God and men, and be auaunsid among othere trees?
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
And alle trees seiden to the ramne, ether theue thorn, Come thou, and be lord on vs.
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
Whiche answeride to hem, If ye maken me verili kyng to you, come ye, and reste vndur my schadewe; sotheli, if ye nylen, fier go out of the ramne, and deuoure the cedris of the Liban.
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
Now therfor if riytfuli and without synne `ye han maad Abymelech kyng on you, and ye han do wel with Jerobaal, and with his hows, and ye han yolde while to the benefices of hym,
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
that fauyt for you, and yaf his lijf to perelis, that he schulde delyuere you fro the hond of Madian;
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
and ye han rise now ayens the hows of my fadir, and han slayn hyse sones, seuenti men, on o stoon, and `han maad Abymelech, sone of his handmayde, kyng on the dwelleris of Sichem, for he is youre brother;
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
therfor if ye han do riytfuli, and with out synne with Gerobaal and his hows, to dai be ye glad in Abymelech, and be he glad in you; but if ye han do weiwardli,
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
fier go out `of hym, and waste the dwelleris of Sichem, and the citee of Mello; and fier go out of the men of Sichem, and of the citee of Mello, and deuoure Abymelech.
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
And whanne he hadde seide these thingis, he fledde, and yede in to Berara, and dwellide there, for drede of Abymelech, his brother.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
And Abymelech regnede on Israel thre yeer.
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
And the Lord sente the worste spirit bitwixe Abymelech and the dwelleris of Sichem, whiche bigynnen to holde hym abomynable,
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
and to arette the felony of sleyng of seuenti sones of Gerobaal, and the schedyng out of her blood, in to Abymelech her brother, and to othere princes of Sichem, that hadden helpid hym.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
And thei settiden buyschementis ayens hym in the hiynesse of hillis; and the while thei abideden `the comyng of hym, thei hauntiden theftis, and token preies of men passynge forth; and it was teld to Abymelech.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
Forsothe Gaal, `the sone of Obed, cam with his britheren, and passide in to Siccima; at whos entryng the dwelleris of Sichem weren reisid, and yeden out `in to feeldis,
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
and wastiden vyneris, and `to-traden grapis; and with cumpeneys of syngeris maad thei entriden in to `the temple of her God, and among metis and drynkis thei cursiden Abymalech, while Gaal,
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
the sone of Obed, criede, Who is this Abymelech? And what is Sichem, that we serue hym? Whether he is not the sone of Jerobaal, and made Zebul his seruaunt prince on the men of Emor, fadir of Sichem? Whi therfor schulen we serue hym?
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
`Y wolde, that sum man yaf this puple vndur myn hond, that Y schulde take awei Abimelech fro the myddis. And it was seid to Abymelech, Gadere thou the multitude of oost, and come thou.
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
For whanne the wordis of Gaal, sone of Obed, weren herd, Zebul, the prynce of the citee, was ful wrooth;
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
and he sente priueli messangeris to Abymelech, and seide, Lo! Gaal, sone of Obed, cam in to Siccymam, with hise britheren, and he excitith the citee to fiyte ayens thee;
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
therfor rise thou bi niyt with the puple, which is with thee, and be thou hid in the feeld;
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
and first in the morewtid, whanne the sunne rysith, falle on the citee; forsothe whanne he goth out with his puple ayens thee, do thou to hym that that thou maist.
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
Therfor Abymelech roos with al his oost bi nyyt, and settide buyschementis bisidis Siccimam, in foure placis.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
And Gaal, the sone of Obed, yede out, and stood in the entryng of `the yate of the citee. Forsothe Abymelech and al the oost with hym roos fro the place of buyschementis.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
And whanne Gaal hadde seyn the puple, he seide to Zebul, Lo! a multitude cometh doun fro the hillis. To whom he answeride, Thou seest the schadewis of hillis as the `heedis of men, and thou art disseyued bi this errour.
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
And eft Gaal seide, Lo! a puple cometh doun fro the myddis of erthe, `that is, fro the hiynesse of hillis, and o cumpeny cometh bi the weie that biholdith the ook.
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
To whom Zebul seide, Where is now thi mouth, bi which thou spekist, Who is Abymelech, that we serue hym? Whether this is not the puple, whom thou dispisidist? Go thou out, and fiyte ayens hym.
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
Therfor Gaal yede, while the puple of Sichen abood; and he fauyt ayens Abymelech.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
Which pursuede Gaal fleynge, and constreynede to go in to the citee; and ful many of his part felde doun `til to the yate of the citee.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
And Abymelech sat in Ranna; sotheli Zebul puttide Gaal and hise felowis out of the citee, and suffride not to dwelle ther ynne.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
Therfor in the dai suynge the puple yede out in to the feeld; and whanne this thing was teld to Abymelech,
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
he took his oost, and departide `in to thre cumpenyes, and settide buyschementis in the feeldis; and he siy that the puple yede out of the citee, and he roos,
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
and felde on hem with his cumpeny, and enpugnyde and bisegide the citee. Sothely twei cumpenyes yeden aboute opynli bi the feeld, and pursueden aduersaries.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
Certis Abymelech fauyt ayens the citee in al that dai, which he took, whanne the dwelleris weren slayn, and that citee was destried, so that he spreynte abrood salt ther ynne.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
And whanne thei, that dwelliden in the tour of Sichem, hadde herd this, thei entriden in to the temple of her god Berith, where thei hadden maad boond of pees with hym; and of that the place took name, which place was ful strong.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
And Abymelech herde the men of the tour of Sichem gaderid to gidere,
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
and he stiede in to the hil Selmon with al his puple; and with an axe takun he kittide doun a boow of a tre, and he bar it, put on the schuldur, and seide to felowis, Do ye this thing, which ye seen me do.
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
Therfor with strijf thei kittiden doun bowis of the trees, and sueden the duyk; whiche cumpassiden and brenten `the tour; and so it was doon, that with smooke and fier a thousynde of men weren slayn, men togidere and wymmen, of the dwelleris of the tour of Sichem.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
Forsothe Abymelech wente forth fro thennus, and cam to the citee of Thebes, which he cumpasside, and bisegide with an oost.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
Forsothe the tour was hiy in the myddis of the citee, to which men togidere and wymmen fledden, and alle the princes of the citee, while the yate was closid stronglieste; and thei stoden on the roof of the tour bi toretis.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
And Abymelech cam bisidis the tour, and fauyt strongli, and he neiyede to the dore, and enforside to putte fier vndur; and lo!
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
o womman castide fro aboue a gobet of a mylnestoon, and hurtlide to `the heed of Abymelech, and brak his brayn.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
And he clepide soone his squyer, and seide to hym, Drawe out thi swerd, and sle me, lest perauenture it be seid, that Y am slan of a womman. Which performede `the comaundementis, and `killide Abymelech;
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
and whanne he was deed, alle men of Israel that weren with hym turneden ayen to her seetis.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
And God yeldide to Abymelech the yuel that he dide ayens his fadir, for he killide hise seuenti britheren.
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
Also that thing was yoldun to men of Sichem, which thei wrouyten, and the curs of Joathan, sone of Jerobaal, cam on hem.

< Oweruza 9 >