< Oweruza 4 >

1 Ehudi atamwalira, Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova.
A po smrti Aodovoj opet sinovi Izrailjevi èiniše što je zlo pred Gospodom.
2 Choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Yabini, mfumu ya ku Kanaani, imene inkalamulira ku Hazori. Mkulu wa ankhondo ake anali Sisera, amene ankakhala ku Haroseti-Hagoyimu.
I Gospod ih dade u ruke Javinu caru Hananskom, koji vladaše u Asoru, a vojsci njegovoj bješe vojvoda Sisara, koji življaše u Arosetu neznabožaèkom.
3 Aisraeli analira kwa Yehova kuti awathandize, chifukwa Sisera anali ndi magaleta achitsulo 900 ndipo anazunza Aisraeli mwankhanza kwa zaka makumi awiri.
I sinovi Izrailjevi vapiše ka Gospodu; jer on imaše devet stotina gvozdenijeh kola, i veoma pritješnjavaše sinove Izrailjeve dvadeset godina.
4 Debora, mneneri wamkazi, mkazi wake wa Rapidoti ndiye ankatsogolera Israeli nthawi imeneyo.
U to vrijeme Devora proroèica, žena Lafidotova, suðaše Izrailju.
5 Iye ankakhala pansi pa mtengo wa mgwalangwa wa Debora, pakati pa Rama ndi Beteli mʼdziko la ku mapiri la Efereimu, ndipo Aisraeli ankapita kwa iye kuti akaweruze milandu yawo.
I Devora stanovaše pod palmom izmeðu Rame i Vetilja u gori Jefremovoj, i dolažahu k njoj sinovi Izrailjevi na sud.
6 Debora uja anatuma munthu kuti akayitane Baraki mwana wa Abinoamu wa ku Kedesi mʼdziko la Nafutali ndipo anati kwa iye, “Yehova Mulungu wa Israeli akukulamula iwe kuti, ‘Pita kasonkhanitse anthu ku phiri la Tabori. Ubwere nawo anthu 10,000 a fuko la Nafutali ndi a fuko la Zebuloni.
A ona poslavši dozva Varaka sina Avinejemova iz Kedesa Neftalimova, i reèe mu: nije li zapovjedio Gospod Bog Izrailjev: idi, skupi narod na goru Tavor, i uzmi sa sobom deset tisuæa ljudi izmeðu sinova Neftalimovijeh i sinova Zavulonovijeh?
7 Ine ndidzakokera Sisera mkulu wa ankhondo a Yabini pamodzi ndi magaleta ake ndi asilikali ake kwa inu ku mtsinje wa Kisoni ndipo ndidzamupereka mʼmanja mwanu.’”
Jer æu dovesti k tebi na potok Kison Sisaru vojvodu Javinova i kola njegova i ljudstvo njegovo, i predaæu ga tebi u ruke.
8 Baraki anamuyankha kuti, “Mukapita nane limodzi ine ndipita. Koma ngati sitipitira limodzi, inenso sindipita.”
A Varak joj reèe: ako æeš ti iæi sa mnom, iæi æu; ako li neæeš iæi sa mnom, neæu iæi.
9 Debora anati, “Chabwino, ine ndipita nawe limodzi. Koma mudziwe kuti inu simudzalandirapo ulemu pa zimene mwachitazi popeza Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwa munthu wamkazi.” Choncho Debora ananyamuka kupita ku Kedesi pamodzi ndi Baraki.
A ona reèe: ja æu iæi s tobom, ali neæeš imati slave na putu kojim æeš iæi; jer æe ženi u ruku dati Gospod Sisaru. I ustavši Devora otide s Varakom u Kedes.
10 Baraki anayitana mafuko a Zebuloni ndi Nafutali kuti abwere ku Kedesi. Anthu 10,000 anamutsatira, ndipo Debora anapita naye pamodzi.
I Varak sazvavši sinove Zavulonove i Neftalimove u Kedes, povede za sobom deset tisuæa ljudi; i Devora iðaše s njim.
11 Nthawi imeneyo nʼkuti Mkeni wina dzina lake Heberi atalekana ndi Akeni anzake, zidzukulu za Hobabu, mlamu wa Mose, nakamanga tenti yake pafupi ndi mtengo wa thundu ku Zananimu pafupi ndi Kedesi.
A Ever Kenejin bješe se odvojio od Keneja, od sinova Ovava tasta Mojsijeva, i bješe razapeo svoj šator kod hrastova Zanajimskih, a to je kod Kedesa.
12 Pamene Sisera anamva kuti Baraki mwana wa Abinoamu wapita ku phiri la Tabori,
I javiše Sisari da je izašao Varak sin Avinejemov na goru Tavor.
13 anasonkhanitsa magaleta ake achitsulo 900 ndi anthu onse amene anali naye ndipo anachoka ku Haroseti-Hagoyimu kupita ku mtsinje wa Kisoni.
I Sisara skupi sva kola svoja, devet stotina kola gvozdenijeh, i sav narod koji bijaše s njim od Aroseta neznabožaèkoga do potoka Kisona.
14 Debora anawuza Baraki kuti, “Dzukani! Paja ndi lero limene Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwako. Kodi Yehova sanakhale akukutsogolerani?” Choncho Baraki anatsika phiri la Tabori, anthu 10,000 akumutsata.
Tada reèe Devora Varaku: ustani, jer je ovo dan, u koji ti dade Gospod Sisaru u ruke. Ne ide li Gospod pred tobom? I Varak siðe s gore Tavora, i deset tisuæa ljudi za njim.
15 Yehova anasokoneza Sisera ndi magaleta ake pamodzi ndi ankhondo ake onse. Baraki ndi anthu ake anawapirikitsa ndipo Sisera anatsika pa galeta yake nayamba kuthawa pansi.
I Gospod smete Sisaru i sva kola njegova i svu vojsku oštrim maèem pred Varakom; i Sisara siðe s kola svojih i pobježe pješice.
16 Baraki analondola magaletawo pamodzi ndi ankhondo onse mpaka ku Haroseti-Hagoyimu, ndipo ankhondo onse a Sisera anaphedwa ndi lupanga. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe anatsala.
A Varak potjera kola i vojsku do Aroseta neznabožaèkoga; i pade sva vojska Sisarina od oštroga maèa, ne osta nijedan.
17 Komabe Sisera anathawa pansi mpaka anakafika ku tenti ya Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni uja, chifukwa panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori ndi banja la Heberi, Mkeni uja.
A Sisara uteèe pješice do šatora Jailje žene Evera Kenejina; jer bijaše mir meðu Javinom carem Asorskim i domom Evera Kenejina.
18 Yaeli anatuluka kukachingamira Sisera ndipo anati, “Bwerani mbuye wanga, lowani momwemo musaope.” Choncho analowa mʼtenti muja, ndipo anamufunditsa chofunda.
I izide Jailja na susret Sisari, i reèe mu: skloni se, gospodaru, skloni se kod mene; ne boj se. I on se skloni kod nje u šator, i ona ga pokri pokrivaèem.
19 Anati, “Ndili ndi ludzu, chonde patseniko madzi pangʼono akumwa, ndili ndi ludzu.” Mkaziyo anatsekula thumba la chikopa mmene munali mkaka, namupatsa kuti amwe, ndipo anamufunditsanso.
A on joj reèe: daj mi malo vode da se napijem, jer sam žedan. A ona otvori mijeh mlijeka i napoji ga, pa ga pokri.
20 Kenaka anawuza mkaziyo kuti, “Muyime pa khomo la tentili, ndipo munthu wina akabwera kudzakufunsani kuti, ‘Kodi kwafika munthu wina kuno?’ Inu muyankha kuti, ‘Ayi.’”
A on joj reèe: stoj na vratima od šatora, i ako ko doðe i zapita te i reèe: ima li tu ko? reci: nema.
21 Koma Yaeli mkazi wa Heberi, anatenga chikhomo cha tenti ndi hamara ndi kupita mwakachetechete kwa Sisera uja. Tsono Sisera ali mtulo chifukwa chotopa, mkazi uja anamukhomera chikhomo chija mʼmutu mwake. Chinatulukira kwinaku mpaka kulowa mʼnthaka, ndipo anafa pomwepo.
Tada Jailja žena Everova uze kolac od šatora, i uze malj u ruku, i pristupi k njemu polako, i satjera mu kolac kroz slijepe oèi, te proðe u zemlju, kad spavaše tvrdo umoran, i umrije.
22 Baraki atafika akulondola Sisera, Yaeli anatuluka kukamuchingamira namuwuza kuti, “Lowani mudzaone munthu amene mukumufunafuna.” Tsono atalowa anangoona Sisera ali thapsa pansi wakufa ndi chikhomo chili mʼmutu mwake.
I gle, Varak tjeraše Sisaru, i Jailja mu izide na susret, i reèe mu: hodi da ti pokažem èovjeka kojega tražiš. I uðe k njoj, i gle, Sisara ležaše mrtav, i kolac mu u slijepijem oèima.
23 “Choncho pa tsiku limenelo Mulungu anagonjetsa Yabini mfumu ya Akanaani, pamaso pa Aisraeli.
Tako pokori Bog u onaj dan Javina cara Hananskoga pred sinovima Izrailjevijem.
24 Ndipo Aisraeli anapanikizabe Yabini, mfumu ya Akanaani, mpaka kumuwonongeratu.
I ruka sinova Izrailjevijeh bivaše sve teža Javinu caru Hananskom, dokle ne istrijebiše Javina cara Hananskoga.

< Oweruza 4 >