< Oweruza 15 >

1 Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
`Forsothe aftir sum del of tyme, whanne the daies of wheete heruest neiyiden, Sampson cam, and wolde visite his wijf, and he brouyte to hir a `kide of geet; and when he wolde entre in to hir bed bi custom, `the fadir of hir forbeed hym, and seide,
2 Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
Y gesside that thou haddist hatid hir, and therfor Y yaf hir to thi freend; but sche hath a sistir, which is yongere and fairere than sche, be sche `wijf to thee for hir.
3 Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
To whom Sampson answeride, Fro this day no blame schal be in me ayens Filistees, for Y schal do yuels to you.
4 Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
And he yede, and took thre hundrid foxis, and ioynede `the tailis of hem to tailis, and boond brondis in the myddis,
5 Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
whiche he kyndlid with fier, and leet hem, that thei schulden renne aboute hidur and thidur; `which yeden anoon in to the cornes of Filisteis, bi whiche kyndlid, bothe cornes `borun now to gidere, and yit stondynge in the stobil, weren brent, in so myche that the flawme wastide vyneris, and `places of olyue trees.
6 Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
And Filisteis seiden, Who dide this thing? To whiche it was seid, Sampson, hosebonde of the `douytir of Thannathei, for he took awey Sampsones wijf, and yaf to another man, `wrouyte this thing. And Filisteis stieden, and brenten bothe the womman and hir fadir.
7 Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
To whiche Sampson seide, Thouy ye han do this, netheles yit Y schal axe veniaunce of you, and than Y schal reste.
8 Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
And he smoot hem with greet wounde, so that thei wondriden, and `puttiden the hyndrere part of the hipe on the thiy; and he yede doun, and dwellide in the denne of the stoon of Ethan.
9 Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
Therfor Filisteis stieden in to the lond of Juda, and settiden tentis in the place, that was clepid aftirward Lethi, that is, a cheke, wher `the oost of hem was spred a brood.
10 Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
And men of the lynage of Juda seiden to hem, Whi `stieden ye ayens vs? Whiche answeriden, We comen that we bynde Sampson, and yelde to hym tho thingis whiche he wrouyte in vs.
11 Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
Therfor thre thousynde of men of Juda yeden doun to the denne of the flynt of Ethan; and thei seiden to Sampson, Woost thou not, that Filisteis comaunden to vs? Why woldist thou do this thing? To whiche he seide.
12 Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
As thei diden to me, Y dide to hem. Thei seien, We comen to bynde thee, and to bitake thee in to the `hondis of Filisteis. To whiche Sampson answeride, Swere ye, and `biheete ye to me, that ye sle not me.
13 Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
And thei seiden, We schulen not sle thee, but we schulen bitake thee boundun. And thei bounden him with twei newe cordis, and token fro the stoon of Ethan.
14 Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
And whanne thei hadden come to the place of cheke, and Filisteis criynge hadden runne to hym, the spirit of the Lord felde in to hym, and as stikis ben wont to be wastid at the odour of fier, so and the bondis, with whiche he was boundun, weren scaterid and vnboundun.
15 Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
And he took a cheke foundun, that is, the lowere cheke boon of an asse, that lay, `and he killyde `with it a thousinde men; and seide,
16 Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
With the cheke of an asse, that is, with the lowere cheke of a colt of femal assis, Y dide hem awey, and Y killide a thousynde men.
17 Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
And whanne he songe these wordis, and `hadde fillid, he castide forth fro the hond the lowere cheke; and he clepide the name of that place Ramath Lethi, `which is interpretid, the reisyng of a cheke.
18 Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
And he thristide greetly, and criede to the Lord, and seide, Thou hast youe in the hond of thi seruaunt this grettest helthe and victory; and lo! Y die for thyrst, and Y schal falle in to the hondis of vncircumcidid men.
19 Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
Therfor the Lord openyde a wang tooth in the cheke boon of the asse, and watris yeden out therof, `bi whiche drunkun he refreischide the spirit, and resseuede strengthis; therfor the name of that place was clepid the Welle of the clepere of the cheke `til to present dai.
20 Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.
And he demyde Israel in the daies of Filistiym twenti yeer.

< Oweruza 15 >