< Oweruza 12 >

1 Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
`Lo! forsothe discencioun roos in Effraym; for whi thei, that passiden ayens the north, seiden to Jepte, Whi yedist thou to batel ayens the sones of Amon, and noldist clepe vs, that we schulden go with thee? Therfor we schulen brenne thin hows.
2 Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
To whiche he answeride, Greet strijf was to me and to my puple ayens the sones of Amon, and Y clepide you, that ye schulden `yyue help to me, and ye nolden do.
3 Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
`Which thing Y siy, and puttide my lijf in myn hondis; and Y passide to the sones of Amon, and `the Lord bitook hem in to myn hondis; what haue Y disseruyd, that ye ryse togidere ayens me in to batel?
4 Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
Therfor whanne alle the men of Galaad weren clepid to hym, he fauyt ayens Effraym; and the men of Galaad smytiden Effraym; for he seide, Galaad is `fugitif ether exilid fro Effraym, and dwellith in the myddis of Effraym and of Manasses.
5 Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
And the men of Galaad ocupieden the forthis of Jordan, bi whiche Effraym schulden turne ayen. And whanne a man fleynge of the noumbre of Effraym hadde come to tho forthis, and hadde seid, Y biseche, that thou suffre me passe; men of Galaad seiden to hym, Whether thou art a man of Effraym? And whanne he seide, Y am not,
6 Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
thei axiden hym, Seie thou therfor Sebolech, `whiche is interpretid, `an eer of corn. Which answeride, Thebolech, and myyte not brynge forth an eer of corn bi the same lettre. And anoon thei strangeliden hym takun in thilke passyng of Jordan; and two and fourti thousynde of Effraym felden doun in that tyme.
7 Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
And so Jepte, `a man of Galaad, demyde Israel sixe yeer; and he `was deed, and biried in his citee Galaad.
8 Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
Abethsan of Bethleem, that hadde thretti sones, and so many douytris, demyde Israel aftir Jepte;
9 Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
whiche douytris he sente out, and yaf to hosebondis, and he took wyues to hise sones of the same noumbre, and brouyte in to hys hows; which demyde Israel seuene yeer;
10 Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
and he `was deed, and biried in Bethleem.
11 Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
Whos successour was Hailon of Zabulon; and he demyde Israel ten yeer;
12 Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
and he was deed, and biried in Zabulon.
13 Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
Aftir hym Abdon, the sone of Ellel, of Pharaton, demyde Israel;
14 Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
which Abdon hadde fourti sones, and of hem thretti sones, stiynge on seuenti coltis of femal assis, `that is, mulis, and he demyde Israel eiyte yeer;
15 Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.
and he `was deed, and biried in Pharaton, in the loond of Effraym, in the hil of Amalech.

< Oweruza 12 >