< Oweruza 1 >

1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
Po śmierci Jozuego synowie Izraela pytali PANA: Któż z nas wyruszy pierwszy przeciwko Kananejczykom, aby walczyć z nimi?
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
I PAN powiedział: Wyruszy Juda. Oto dałem ziemię w jego ręce.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
Juda powiedział do swego brata Symeona: Chodź ze mną do mego losu, a będziemy walczyć z Kananejczykami. Potem ja pójdę z tobą do twego losu. I Symeon poszedł z nim.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
Wyruszył więc Juda, a PAN wydał Kananejczyków i Peryzzytów w ich ręce i zabili w Bezek dziesięć tysięcy mężczyzn.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
W Bezek znaleźli Adoni-Bezeka i walczyli z nim, i zabili Kananejczyków i Peryzzytów.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
I Adoni-Bezek uciekł, oni zaś ścigali go; a gdy go pojmali, ucięli mu kciuki u rąk i [paluchy] u nóg.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
Wtedy Adoni-Bezek powiedział: Siedemdziesięciu królów z obciętymi kciukami u rąk i [paluchami] u nóg zbierało [okruchy] pod moim stołem. Jak ja uczyniłem, tak mi Bóg odpłacił. I przyprowadzili go do Jerozolimy, i tam umarł.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
Przedtem bowiem synowie Judy walczyli przeciwko Jerozolimie, zdobyli ją i pobili ostrzem miecza, a miasto spalili ogniem.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
Potem synowie Judy wyruszyli, aby walczyć z Kananejczykami mieszkającymi w górach, na południu i na nizinie.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
Następnie Juda wyruszył przeciwko Kananejczykom, którzy mieszkali w Hebronie (a Hebron przedtem nazywał się Kiriat-Arba), i pobił Szeszaja, Achimana i Talmaja.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
Stamtąd wyruszył przeciwko mieszkańcom Debiru, a Debir przedtem nazywał się Kiriat-Sefer.
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
I Kaleb powiedział: Temu, kto pobije Kiriat-Sefer i zdobędzie je, dam swoją córkę Aksę za żonę.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
Zdobył je Otniel, syn Kenaza, młodszego brata Kaleba. I dał mu swoją córkę Aksę za żonę.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
A gdy ona przyszła do niego, namawiała go, aby prosił jej ojca o pole; i zsiadła z osła, a Kaleb zapytał ją: Czego sobie życzysz?
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
A ona odpowiedziała: Daj mi błogosławieństwo. Skoro dałeś mi ziemię południową, daj mi też źródła wód. I Kaleb dał jej źródła górne i źródła dolne.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
Synowie Kenity, teścia Mojżesza, wyruszyli z miasta palm razem z synami Judy na pustynię Judy leżącą na południu od Arad. Gdy tam przybyli, zamieszkali z ludem.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Potem Juda wyruszył ze swym bratem Symeonem i zabili Kananejczyków mieszkających w Sefat, i zburzyli je, i nazwali to miasto Chorma.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
Juda zdobył też Gazę wraz z jej granicami, Aszkelon wraz z jego granicami i Ekron wraz z jego granicami.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
I PAN był z Judą, który posiadł górę, lecz nie mógł wypędzić mieszkańców doliny, bo ci mieli żelazne rydwany.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
Kalebowi zaś dano Hebron, jak powiedział Mojżesz. Stamtąd wygnał [on] trzech synów Anaka.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
Ale synowie Beniamina nie wygnali Jebusytów mieszkających w Jerozolimie; dlatego Jebusyci mieszkają z synami Beniamina w Jerozolimie aż do dziś.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
Wyruszył też dom Józefa przeciwko Betel, a PAN był z nim.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
I dom Józefa wyszpiegował Betel – a miasto [to] przedtem nazywało się Luz.
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
A gdy szpiedzy zobaczyli człowieka wychodzącego z miasta, powiedzieli do niego: Prosimy, pokaż nam wejście do miasta, a okażemy ci miłosierdzie.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
I pokazał im wejście do miasta, a oni pobili miasto ostrzem miecza, lecz tego człowieka wraz z całą jego rodziną puścili wolno.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
I tak człowiek ten udał się do ziemi Chetytów, zbudował miasto i nadał mu nazwę Luz. To jest jego nazwa aż do dziś.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
Manasses nie wypędził też [mieszkańców] Bet-Szean i jego miasteczek ani [mieszkańców] Tanaku i jego miasteczek, ani mieszkańców Dor i jego miasteczek, ani mieszkańców Jibleam i jego miasteczek, ani mieszkańców Megiddo i jego miasteczek. Kananejczycy nadal mieszkali więc w tej ziemi.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
A gdy Izrael się wzmocnił, kazał Kananejczykom płacić daninę i nie wygnał ich.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Także i Efraim nie wypędził Kananejczyków mieszkających w Gezer, dlatego Kananejczycy mieszkali wśród nich w Gezer.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Zebulon [również] nie wypędził mieszkańców Kitron ani mieszkańców Nahalol, dlatego Kananejczycy mieszkali wśród nich i płacili [im] daninę.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Aszer także nie wypędził mieszkańców Akko ani mieszkańców Sydonu, Achlab, Akzibu, Chelba, Afik i Rechob.
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
I Aszer mieszkał pośród Kananejczyków mieszkających w tej ziemi, gdyż ich nie wypędził.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Neftali [też] nie wypędził mieszkańców Bet-Szemesz ani mieszkańców Bet-Anat i mieszkał wśród Kananejczyków mieszkających w tej ziemi. Jednakże mieszkańcy Bet-Szemesz i Bet-Anat płacili [mu] daninę.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
Amoryci zaś wyparli synów Dana w góry, tak że nie pozwalali im schodzić do doliny.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
Amoryci utrzymali się i mieszkali na górze Cheres, w Ajjalonie i w Szaalbin, lecz wzmocniła się ręka domu Józefa i zaczęli mu płacić daninę.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
A granica Amorytów [biegła] od wzniesienia do Akrabbim, od skały i wyżej.

< Oweruza 1 >