< Yoswa 8 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
Potem PAN powiedział do Jozuego: Nie bój się ani się nie lękaj. Weź ze sobą wszystkich wojowników, powstań i wyrusz do Aj. Patrz, daję w twoje ręce króla Aj, jego lud i jego ziemię.
2 Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
I postąpisz z Aj i jego królem tak, jak postąpiłeś z Jerychem i jego królem. Tym razem weźmiecie sobie jego łupy i bydło. Zastaw zasadzkę na miasto od jego tyłu.
3 Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
Powstali więc Jozue i wszyscy wojownicy, by wyruszyć przeciwko Aj. Jozue wybrał trzydzieści tysięcy bardzo dzielnych mężczyzn i wysłał ich nocą.
4 nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
I rozkazał im: Uważajcie, przygotujcie zasadzkę za miastem. Nie oddalajcie się od miasta zbyt daleko i bądźcie wszyscy w pogotowiu.
5 Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
Ja zaś i cały lud, który [jest] ze mną, podejdziemy pod miasto; a gdy oni wyjdą nam naprzeciw, jak za pierwszym razem, uciekniemy przed nimi.
6 Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
A oni pójdą za nami, aż ich odciągniemy od miasta, bo powiedzą: Uciekają przed nami, tak jak za pierwszym razem, gdyż będziemy uciekać przed nimi.
7 inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
Wtedy wyjdziecie z zasadzki i opanujecie miasto. PAN bowiem, wasz Bóg, odda je w wasze ręce.
8 Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
A gdy zdobędziecie miasto, podpalicie je. Postąpicie zgodnie ze słowem PANA. Patrzcie, ja to wam rozkazuję.
9 Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
Jozue więc ich wysłał, a oni poszli przygotować zasadzkę; i zostali między Betel a Aj, na zachód od Aj. Jozue zaś spędził tę noc wśród ludu.
10 Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
Następnego dnia Jozue wstał wcześnie rano, obliczył lud i poszedł przed nim wraz ze starszymi Izraela przeciwko Aj.
11 Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
Wszyscy wojownicy, którzy z nim byli, wyruszyli, przybyli pod miasto i rozbili obóz po północnej stronie Aj, tak że między nimi a Aj była dolina.
12 Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
Następnie wziął około pięciu tysięcy mężczyzn, których umieścił w zasadzce między Betel a Aj, po zachodniej stronie miasta.
13 Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
I ustawiono lud, całe wojsko po północnej stronie miasta, a tych, którzy przygotowali zasadzkę – po zachodniej stronie. Jozue zaś wyruszył tej nocy na środek doliny.
14 Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
Gdy spostrzegł to król Aj, ludzie z miasta pośpieszyli się, wstali wcześnie rano i wyruszyli do walki z Izraelem – on i cały jego lud – w wyznaczonym czasie przed równiną. Nie wiedział jednak, że za miastem została przygotowana na nich zasadzka.
15 Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
Wtedy Jozue i cały Izrael udawali pokonanych przez nich i uciekali drogą [wiodącą] ku pustyni.
16 Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
I zwołano cały lud, który był w mieście, aby ich ścigać. Ścigali więc Jozuego i zostali odciągnięci od miasta.
17 Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
W Aj i Betel nie pozostał nikt, kto by nie wyruszył za Izraelem; i pozostawili miasto otwarte, i ścigali Izraelitów.
18 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
Wtedy PAN powiedział do Jozuego: Podnieś oszczep, który masz w ręce, w kierunku Aj, gdyż dam je w twoje ręce. I Jozue podniósł oszczep, który [miał] w ręce, w kierunku miasta.
19 Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
A gdy tylko podniósł rękę, ludzie, którzy byli w zasadzce, powstali szybko ze swego miejsca, pobiegli i weszli do miasta, zajęli je i szybko podpalili.
20 Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
A gdy ludzie z Aj obejrzeli się, zobaczyli, że dym wznosi się z miasta ku niebu, a nie mieli siły uciekać ani w jedną, ani w drugą stronę. Tymczasem lud, który uciekał na pustynię, zwrócił się przeciw ścigającym.
21 Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
Jozue bowiem i cały [lud] Izraela zobaczyli, że ludzie z zasadzki zajęli miasto i że z miasta unosi się dym, zawrócili [więc] i [zaczęli] zabijać ludzi z Aj.
22 Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
A [drudzy] wyszli im naprzeciw z miasta i zostali oni otoczeni przez Izraelitów, jedni z jednej, a drudzy z drugiej strony. I zabili ich tak, że nikt z nich nie pozostał przy życiu ani nie uciekł.
23 kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
Króla Aj jednak pojmali żywcem i przyprowadzili do Jozuego.
24 Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
Gdy więc Izraelici wybili wszystkich mieszkańców Aj na polu, na pustyni, gdzie ich ścigali, i gdy wszyscy oni polegli od miecza, aż zostali zgładzeni, wszyscy Izraelici zawrócili do Aj i pobili je ostrzem miecza.
25 Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
Wszystkich poległych tego dnia, mężczyzn i kobiet, było dwanaście tysięcy, [byli to] wszyscy mieszkańcy Aj.
26 Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
A Jozue nie opuścił ręki, którą wyciągnął z oszczepem, aż zgładził wszystkich mieszkańców Aj.
27 Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
Tylko bydło i łupy tego miasta Izraelici podzielili między siebie według słowa PANA, które przekazał on Jozuemu.
28 Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
Wtedy Jozue spalił Aj i uczynił je wieczną mogiłą i pustynią aż do dziś.
29 Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
A króla Aj powiesił na drzewie aż do wieczora. A gdy słońce zaszło, Jozue kazał zdjąć jego zwłoki z drzewa i porzucić je [przy samej] bramie miasta, i wznieść nad nim wielki stos kamieni, [który trwa] aż do dziś.
30 Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
Wtedy Jozue zbudował ołtarz dla PANA, Boga Izraela, na górze Ebal;
31 Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
Jak nakazał synom Izraela Mojżesz, sługa PANA, [i] jak jest napisane w księdze Prawa Mojżesza: ołtarz z całych kamieni, których nie tknęło [żadne] żelazo. I na nim złożyli PANU całopalenia i ofiary pojednawcze.
32 Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
Tam też napisał na kamieniach odpis Prawa Mojżesza, który napisał w obecności synów Izraela.
33 Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
A cały Izrael oraz jego starsi, przełożeni i sędziowie stali po obu stronach arki przed kapłanami lewitami, którzy nosili arkę przymierza PANA, zarówno przybysz, jak i rodowity, połowa ich naprzeciw góry Gerizim, a połowa naprzeciw góry Ebal jak przedtem nakazał Mojżesz, sługa PANA, aby błogosławić lud Izraela.
34 Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
Potem czytał wszystkie słowa prawa, błogosławieństwa i przekleństwa według wszystkiego, co zostało napisane w księdze Prawa.
35 Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.
Nie było ani jednego słowa ze wszystkiego, co Mojżesz nakazał, którego Jozue nie odczytał przed całym zgromadzeniem Izraela, przed kobietami, dziećmi i przybyszami, którzy mieszkali wśród nich.

< Yoswa 8 >