< Yoswa 5 >

1 Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
A kad èuše svi carevi Amorejski, koji bijahu s ovu stranu Jordana k zapadu, i svi carevi Hananski, koji bijahu pokraj mora, da je Gospod osušio Jordan pred sinovima Izrailjevijem dokle prijeðoše, rastopi se srce u njima i nesta u njima junaštva od straha sinova Izrailjevijeh.
2 Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
U to vrijeme reèe Gospod Isusu: naèini oštre nože, i obreži opet sinove Izrailjeve.
3 Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
I naèini Isus oštre nože, i obreza sinove Izrailjeve na brdašcu Aralotu.
4 Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
A ovo je uzrok zašto ih Isus obreza: sav narod što izide iz Misira, sve muškinje, svi ljudi vojnici pomriješe u pustinji na putu, pošto izidoše iz Misira;
5 Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
Jer bješe obrezan sav narod koji izide, ali ne obrezaše nikoga u narodu koji se rodi u pustinji na putu, pošto izidoše iz Misira.
6 Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
Jer èetrdeset godina iðahu sinovi Izrailjevi po pustinji dokle ne pomrije sav narod, ljudi vojnici, što izidoše iz Misira, jer ne slušaše glasa Gospodnjega, te im se zakle Gospod da im neæe dati da vide zemlju, za koju se zakleo Gospod ocima njihovijem da æe nam je dati, zemlju, gdje teèe mlijeko i med;
7 Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
I na mjesto njihovo podiže sinove njihove; njih obreza Isus, jer bijahu neobrezani, jer ih ne obrezaše na putu.
8 Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
A kad se sav narod obreza, ostaše na svojem mjestu u okolu dokle ne ozdraviše.
9 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
Tada reèe Gospod Isusu: danas skidoh s vas sramotu Misirsku. I prozva se ono mjesto Galgal do današnjega dana.
10 Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
I sinovi Izrailjevi stojeæi u okolu u Galgalu, slaviše pashu èetrnaestog dana onoga mjeseca uveèe u polju Jerihonskom.
11 Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
I sjutradan poslije pashe jedoše od žita one zemlje hljebove prijesne i zrna pržena, isti dan.
12 Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
I presta mana sjutradan pošto jedoše žita one zemlje, i veæ više ne imaše mane sinovi Izrailjevi, nego jedoše od roda zemlje Hananske one godine.
13 Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
I kad Isus bijaše kod Jerihona, podiže oèi svoje i pogleda, a to èovjek stoji prema njemu s golijem maèem u ruci. I pristupi k njemu Isus i reèe mu: jesi li naš ili naših neprijatelja?
14 Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
A on reèe: nijesam; nego sam vojvoda vojske Gospodnje, sada doðoh. I Isus pade nièice na zemlju, i pokloni se, i reèe mu: šta zapovijeda gospodar moj sluzi svojemu?
15 Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.
A vojvoda vojske Gospodnje reèe Isusu: izuj obuæu s nogu svojih, jer je mjesto gdje stojiš sveto. I uèini Isus tako.

< Yoswa 5 >