< Yoswa 3 >

1 Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
I usta Isus ujutru rano, i kretoše se od Sitima i doðoše do Jordana on i svi sinovi Izrailjevi, i noæiše ondje a ne prijeðoše.
2 Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
A poslije tri dana proðoše upravitelji kroz oko,
3 kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
I zapovjediše narodu govoreæi: kad vidite kovèeg zavjeta Gospoda Boga svojega i sveštenike Levite gdje ga nose, poðite i vi s mjesta svojega i idite za njim.
4 Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
Ali neka bude daljina izmeðu vas i njega do dvije tisuæe lakata; bliže do njega ne primièite se, da biste poznali put kojim æete iæi, jer još nikada nijeste išli tijem putem.
5 Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
I Isus reèe narodu: osveštajte se, jer æe sjutra uèiniti Gospod èudesa meðu vama.
6 Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
Potom reèe Isus sveštenicima govoreæi: uzmite kovèeg zavjetni, i idite pred narodom. I uzeše kovèeg zavjetni i poðoše pred narodom.
7 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
A Gospod reèe Isusu: danas te poèinjem uzvišavati pred svijem Izrailjem da poznadu da æu i s tobom biti kao što sam bio s Mojsijem.
8 Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
Zato ti zapovjedi sveštenicima koji nose kovèeg zavjetni, i reci: kad doðete na kraj vode Jordana, stanite u Jordanu.
9 Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
I reèe Isus sinovima Izrailjevim: pristupite ovamo, i èujte rijeèi Gospoda Boga svojega.
10 Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
Potom reèe Isus: po ovom æete poznati da je Bog živi posred vas, i da æe doista odagnati ispred vas Hananeje i Heteje i Jeveje i Ferezeje i Gergeseje i Amoreje i Jevuseje:
11 Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
Evo, kovèeg zavjeta Gospoda svoj zemlji poæi æe pred vama preko Jordana.
12 Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
Zato sada izberite dvanaest ljudi iz plemena Izrailjeva, po jednoga èovjeka iz svakoga plemena.
13 Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
I èim sveštenici noseæi kovèeg zavjeta Gospoda Gospoda svoj zemlji stanu nogama svojim u vodi Jordanskoj, voda æe se u Jordanu rastupiti, te æe voda koja teèe ozgo stati u gomilu.
14 Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
I kad se podiže narod iz šatora svojih da prijeðe preko Jordana, i sveštenici ponesoše kovèeg zavjetni pred narodom,
15 Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
I kad oni što nošahu kovèeg doðoše do Jordana, i sveštenici noseæi kovèeg okvasiše noge svoje na kraju vode jer je Jordan pun preko bregova svojih za cijelo vrijeme žetve
16 madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
Ustavi se voda što tecijaše ozgo, i stade u jednu gomilu vrlo nadaleko, od grada Adama, koji je kraj Zaretana; a što tecijaše dolje u more kraj polja, more slano, oteèe sasvijem; i narod prelažaše prema Jerihonu.
17 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.
A sveštenici koji nošahu kovèeg zavjeta Gospodnjega stajahu na suhu usred Jordana tvrdo, i sav Izrailj iðaše po suhu, dokle sav narod ne prijeðe preko Jordana.

< Yoswa 3 >