< Yoswa 22 >

1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
Tada sazove Jošua sinove Rubenove i Gadove i polovinu plemena Manašeova
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
i reče im: “Izvršili ste sve što vam je Mojsije, sluga Jahvin, zapovjedio i poslušali ste me u svemu što sam vam zapovjedio.
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
Niste ostavili svoje braće unatoč dugom vojevanju do današnjega dana i vršili ste vjerno zapovijedi Jahve, Boga svojega.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
Sada je Jahve, Bog vaš, dao mir braći vašoj, kako im bijaše obećao. Vratite se sada u svoje šatore, u zemlju koju vam je dao Mojsije, sluga Jahvin, u baštinu s onu stranu Jordana.
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Samo pazite da vršite zapovijedi i Zakon što vam ga dade Mojsije, sluga Jahvin: da ljubite Jahvu, Boga svojega, da uvijek idete putovima njegovim, da čuvate zapovijedi njegove, da se držite uz njega i da mu služite svim srcem i svom dušom.”
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
I blagoslovi ih Jošua i otpusti, a oni se zatim vrate u svoje šatore.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
Mojsije bijaše jednoj polovini plemena Manašeova dao baštinu u Bašanu; a drugoj polovini dade je Jošua usred njihove braće zapadno od Jordana. Otpuštajući ih u njihove šatore, Jošua ih blagoslovi.
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
I reče im: “Vratite se u svoje šatore s velikim blagom i s mnogom stokom, sa srebrom, zlatom, tučem, željezom i haljinama u izobilju i podijelite plijen od neprijatelja svojih s braćom svojom.”
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
Vratiše se sinovi Rubenovi i sinovi Gadovi i polovina plemena Manašeova; odoše od sinova Izraelovih iz Šila u zemlji kanaanskoj da krenu u zemlju gileadsku, na svoju baštinu koju su zaposjeli, kako im je zapovjedio Jahve preko Mojsija.
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
Kad su stigli do jordanskog područja u zemlji kanaanskoj, podigoše sinovi Rubenovi, sinovi Gadovi i polovina plemena Manašeova žrtvenik na Jordanu, žrtvenik velik, izdaleka se vidio.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
Čuli Izraelci gdje se govori: “Evo, sinovi Rubenovi, sinovi Gadovi i polovina plemena Manašeova podigoše žrtvenik prema zemlji kanaanskoj, kod Jordana, na izraelskoj strani.”
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
Na to se skupi sva zajednica sinova Izraelovih u Šilu da pođu u boj na njih.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
Izraelci sinovima Rubenovim, sinovima Gadovim i polovini plemena Manašeova u gileadsku zemlju poslaše Pinhasa, sina svećenika Eleazara,
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
i s njime deset knezova, po jednoga rodovskog glavara od svakoga plemena Izraelova, a svaki je od njih bio glavar obitelji među tisućama porodica Izraelovih.
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
I kad oni dođoše k sinovima Rubenovim, sinovima Gadovim i polovini plemena Manašeova u zemlju gileadsku, rekoše im:
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
“Evo što veli sva zajednica Jahvina: 'Što znači nevjera koju činite protiv Jahve, Boga Izraelova? Zašto se odvrgoste danas od Jahve i, podigavši žrtvenik, zašto se bunite protiv Jahve?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
Zar vam nije dosta zločina iz Peora, od kojega se nismo očistili do dana današnjega i zbog kojega je došao pomor na zajednicu Jahvinu?
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
Ako se danas odvraćate od Jahve i bunite se danas protiv njega, neće li se sutra izliti njegov gnjev na svu zajednicu Izraelovu?
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Ili vam je možda zemlja vaše baštine nečista? Onda prijeđite u zemlju baštine Jahvine, u kojoj je Jahvino Prebivalište, i prebivajte među nama. Ali se ne bunite protiv Jahve i ne bunite se protiv nas dižući sebi žrtvenik mimo žrtvenik Jahve, Boga našega.
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Nije li se Akan, Zerahov sin, sam ogriješio o 'herem' te se oborila srdžba na svu zajednicu Izraelovu? Zar nije umro zbog krivice svoje?'”
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
Tada odgovoriše sinovi Rubenovi, sinovi Gadovi i polovina plemena Manašeova govoreći plemenskim glavarima Izraelovim:
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
“Bog, Bog Jahve, Bog nad bogovima, Jahve zna i neka zna Izrael: ako je to bila pobuna ili nevjernost prema Jahvi, neka nam uskrati svoju pomoć danas;
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
ako smo podigli žrtvenik da se odvrgnemo od Jahve i da prinosimo žrtve paljenice, prinosnice i žrtve pričesnice, neka nam onda sudi Jahve!
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
Učinismo to od brige i skrbi i rekosmo: 'Jednoga će dana sinovi vaši reći našima: Što vam je zajedničko s Jahvom, Bogom Izraelovim?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
Zar nije, sinovi Rubenovi i sinovi Gadovi, postavio Jahve između vas i nas među našu - Jordan? Vi nemate dijela s Jahvom.' I tako bi sinovi vaši mogli učiniti da se sinovi naši odvrate te ne štuju Jahvu.
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
Zato smo rekli: 'Podignimo žrtvenik, ali ne za žrtve paljenice niti za klanice,
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
nego da bude svjedočanstvo između nas i vas, među potomcima našim, da želimo služiti Jahvi paljenicama, klanicama i pričesnicama. Tako da ne mognu jednom vaši sinovi reći našima: Nemate dijela s Jahvom.'
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
Ako bi kada tako rekli nama i potomcima našim, mogli bismo odgovoriti: 'Pogledajte slog žrtvenika Jahvina što su ga podigli oci naši ne za žrtve paljenice ni klanice, nego za svjedočanstvo između nas i vas.'
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
Nije nam ni na kraj pameti pomisao da se bunimo protiv Jahve i da se odvraćamo od njega dižući žrtvenik za žrtve paljenice, prinosnice i klanice, mimo žrtvenik Jahve, Boga našega, koji je pred njegovim Prebivalištem!”
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
Kad svećenik Pinhas, knezovi zbora i glavari izraelskih plemena koji su bili s njim čuše riječi koje im rekoše sinovi Gadovi, sinovi Rubenovi i sinovi Manašeovi, umiriše se.
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
Tada svećenik Pinhas, sin Eleazarov, odgovori sinovima Rubenovim, sinovima Gadovim i sinovima Manašeovim: “Spoznali smo sada da je Jahve među nama, jer mu se niste iznevjerili: tako ste sačuvali sinove Izraelove od kazne Jahvine.”
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
Svećenik Pinhas, sin Eleazarov, i knezovi odoše od sinova Rubenovih i sinova Gadovih i vratiše se iz zemlje gileadske u kanaansku k sinovima Izraelovim i kazaše im odgovor.
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
Izraelovim sinovima bijaše drag taj odgovor: hvalili su Boga i odustali su od nauma da udare na njih i da opustoše zemlju u kojoj su živjeli sinovi Rubenovi i sinovi Gadovi.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
Sinovi Rubenovi i sinovi Gadovi nazvali su žrtvenik “Ed” - “Svjedočanstvo”, jer rekoše: “To je svjedočanstvo među nama: Jahve je Bog.”

< Yoswa 22 >