< Yoswa 19 >

1 Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
Und das zweite Los kam heraus für Schimeon, für den Stamm der Söhne Schimeons nach ihren Familien; und ihr Erbe war inmitten des Erbes der Söhne Judahs.
2 Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
Und für sie waren in ihrem Erbe: Beer-Schaba und Scheba und Moladah;
3 Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
Und Chazar-Schual und Balah und Ezem;
4 Elitoladi, Betuli, Horima,
Und Eltholad und Bethul und Chormah;
5 Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
Und Ziklag und Beth Marchaboth und Chazar Susah;
6 Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
Und Beth-Lebaoth und Scharuchen, dreizehn Städte und ihre Dörfer;
7 Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
Ain, Rimmon und Ether und Aschan, vier Städte und ihre Dörfer;
8 Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
Und alle Dörfer, die rings um diese Städte waren bis Baalath-Beer, Ramath-Negeb. Dies das Erbe des Stammes der Söhne Schimeons nach ihren Familien.
9 Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
Von dem Erbteil der Söhne Judahs ward das Erbe der Söhne Schimeons; denn der Teil der Söhne Judahs war zu viel für sie und die Söhne Schimeons erbten in der Mitte ihres Erbes.
10 Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
Und das dritte Los stieg auf für die Söhne Sebuluns nach ihren Familien und die Grenze ihres Erbes war bis Sarid;
11 Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
Und ihre Grenze ging hinauf gegen das Meer und Maralah und stieß an den Bach vor Jokneam.
12 Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
Und von Sarid wendete es sich herum nach Osten, nach dem Aufgang der Sonne nach der Grenze von Chisloth-Thabor und ging hinaus nach Dabrath und ging hinauf nach Japhia.
13 Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
Und von da ging sie hinüber nach Osten nach dem Aufgang gen Gath-Chepher, gen Itha-Kazin und ging aus nach Rimmon- Methoar, Neah;
14 Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
Und die Grenze wandte sich um dieses nördlich nach Channathon, und ihre Ausläufe waren in der Schlucht Jiphtach-El.
15 Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
Und Kattath und Nahalal und Schimron und Jidalah und Bethlechem, zwölf Städte und ihre Dörfer.
16 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
Dies ist das Erbe der Söhne Sebuluns nach ihren Familien: Diese Städte und ihre Dörfer.
17 Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
Für Issaschar kam das vierte Los heraus, für die Söhne Issaschars nach ihren Familien.
18 Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
Und ihre Grenze war: Jisreel, Chessulloth und Schunem.
19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
Und Chapharajim und Schion und Anacharath;
20 Rabiti, Kisoni, Ebezi,
Und Rabbith und Kischjon und Ebez;
21 Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
Und Remeth und En-Gannim und En-Chaddah und Beth-Pazzez;
22 Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
Und stieß die Grenze an Thabor und Schachazimah und Beth-Schemesch, und waren die Ausläufe ihrer Grenze am Jordan. Sechzehn Städte und ihre Dörfer.
23 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
Das ist das Erbe des Stammes der Söhne Issaschars nach ihren Familien, die Städte und ihr Dörfer.
24 Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
Und das fünfte Los kam heraus für den Stamm der Söhne Aschers nach ihren Familien.
25 Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
Und ihre Grenze war: Chelkath und Chali und Beten und Achschaph.
26 Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
Und Allammelech und Amad und Mischal; und dem Meere zu stieß sie an den Karmel und an Schichor-Libnath;
27 Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
Und wandte sich zurück nach dem Aufgang der Sonne gen Beth-Dagon und stieß an Sebulun und an die Schlucht Jiphthach-El, nördlich von Beth-Emek und Negiel und ging hinaus nach Kabul zur Linken;
28 Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
Und Ebron und Rechob und Chammon und Kanah bis Zidon, der großen;
29 Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
Und die Grenze wandte sich zurück nach Ramah und bis zur Stadt Mizbar-Zor; und die Grenze wandte sich zurück nach Chosah, und ihre Ausläufe waren nach dem Meere hin vom Landstrich nach Achsib;
30 Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
Und Ummah und Aphek und Rechob, zweiundzwanzig Städte und ihre Dörfer.
31 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
Dies ist das Erbe des Stammes der Söhne Aschers nach ihren Familien, diese Städte und ihre Dörfer.
32 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
Für die Söhne Naphthalis kam das sechste Los heraus, für die Söhne Naphthalis nach ihren Familien.
33 Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
Und ihre Grenze war von Cheleph, von Elon in Zaanannim und Adami Nekeb und Jabneel bis Lakkum, und ihre Ausläufe waren an den Jordan.
34 Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
Und die Grenze wandte sich zurück dem Meere zu nach Asnoth Thabor und ging von da aus nach Chukkok und stieß an Sebulun auf der Mittagseite und an Ascher stieß sie gegen das Meer, und am Jordan gegen Aufgang der Sonne an Judah.
35 Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
Und feste Städte hatten sie: Ziddim, Zer und Chammath, Rakkath und Chinnereth.
36 Adama, Rama, Hazori,
Und Adamah und Ramah und Chazor.
37 Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
Und Kedesch und Edrei und En-Chazor;
38 Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
Und Jiron und Migdal-El, Chorem und Beth-Anath und Beth-Schemesch, neunzehn Städte und ihre Dörfer.
39 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
Dies ist das Erbe des Stammes der Söhne Naphthalis nach ihren Familien: die Städte und ihre Dörfer.
40 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
Für den Stamm der Söhne Dans nach ihren Familien kam heraus das siebente Los.
41 Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
Und die Grenze ihres Erbes war: Zorah und Eschthaol und Ir-Schemesch;
42 Saalabini, Ayaloni, Itira,
Und Schaalabbin und Ajalon und Jithlah;
43 Eloni, Timna, Ekroni,
Und Elon und Timnatha und Ekron
44 Eliteke, Gibetoni, Baalati,
Und Elthekeh und Gibbethon und Baa- lath.
45 Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
Und Jehud und Bene-Barak, und Gath-Rimmon;
46 Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
Und Me-Jarkon und Rakkon mit der Grenze gegen Japho.
47 Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
Und die Grenze der Söhne Dans ging über sie hinaus, und die Söhne Dans zogen hinauf und stritten mit Leschem und eroberten sie und schlugen sie mit der Schärfe des Schwertes und nahmen sie ein und wohnten darin, und nannten Leschem Dan nach dem Namen ihres Vaters Dan.
48 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
Das ist das Erbe des Stammes der Söhne Dans nach ihren Familien, diese Städte und ihre Dörfer.
49 Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
Und als sie die Erbverteilung des Landes nach seinen Grenzen vollendet hatten, da gaben die Söhne Israels Joschua, dem Sohne Nuns, ein Erbe in ihrer Mitte.
50 Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
Nach dem Munde Jehovahs gaben sie ihm die Stadt, die er sich erbeten, Timnath-Serach, auf dem Gebirge Ephraim, und er baute die Stadt und wohnte darin.
51 Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.
Dies sind die Erbe, die Eleasar, der Priester, und Joschua, der Sohn Nuns, und die Häupter der Väter der Stämme der Söhne Israels in Schiloh vor Jehovah am Eingang des Versammlungszeltes durch das Los zum Erbe verteilten, und sie vollendeten die Verteilung des Landes.

< Yoswa 19 >