< Yoswa 17 >

1 Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
And this lot fell to the tribe of Manasses (for he is the firstborn of Joseph) to Machir the firstborn of Manasses the father of Galaad, who was a warlike man, and had for possession Galaad and Basan.
2 Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
And to the rest of the children of Manasses according to their families: to the children of Abiezer, and to the children of Helec, and to the children of Esriel, and to the children of Sechem, and to the children of Hepher, and to the children of Semida: these are the male children of Manasses the son of Joseph, by their kindreds.
3 Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
But Salphaad the son of Hepher the son of Galaad the son of Machir the son of Manasses had no sons, but only daughters: whose names are these, Maala and Noa and Hegla and Melcha and Thersa.
4 Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
And they came in the presence of Eleazar the priest and of Josue the son of Nun, and of the princes, saying: The Lord commanded by the hand of Moses, that a possession should be given us in the midst of our brethren. And he gave them according to the commandment of the Lord a possession amongst the brethren of their father.
5 Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
And there fell ten portions to Manasses, beside the land of Galaad and Basan beyond the Jordan.
6 chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
For the daughters of Manasses possessed inheritance in the midst of his sons. And the land of Galaad fell to the lot of the rest of the children of Manasses.
7 Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
And the border of Manasses was from Aser, Machmethath which looketh towards Sichem: and it goeth out on the right hand by the inhabitants of the fountain of Taphua.
8 (Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
For the lot of Manasses took in the land of Taphua, which is on the borders of Manasses, and belongs to the children of Ephraim.
9 Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
And the border goeth down to the valley of the reeds, to the south of the torrent of the cities of Ephraim, which are in the midst of the cities of Manasses: the border of Manasses is on the north side of the torrent, and the outgoings of it are at the sea:
10 Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
So that the possession of Ephraim is on the south, and on the north that of Manasses, and the sea is the border of both, and they are joined together in the tribe of Aser on the north, and in the tribe of Issachar on the east.
11 Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
And the inheritance of Manasses in Issachar and in Aser, was Bethsan and its villages, and Jeblaam with its villages, and the inhabitants of Dor, with the towns thereof: the inhabitants also of Endor with the villages thereof: and in like manner the inhabitants of Thenac with the villages thereof: and the inhabitants of Mageddo with their villages, and the third part of the city of Nopheth.
12 Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
Neither could the children of Manasses overthrow these cities, but the Chanaanite began to dwell in his land.
13 Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
But after that the children of Israel were grown strong, they subdued the Chanaanites, and made them their tributaries, and they did not kill them.
14 Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
And the children of Joseph spoke to Josue, and said: Why hast thou given me but one lot and one portion to possess, whereas I am of so great a multitude, and the Lord hath blessed me?
15 Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
And Josue said to them: If thou be a great people, go up into the woodland, and cut down room for thyself in the land of the Pherezite and the Raphaims: because the possession of mount Ephraim is too narrow for thee.
16 Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
And the children of Joseph answered him: We cannot go up to the mountains, for the Chanaanites that dwell in the low lands, wherein are situate Bethsan with its towns, and Jezrael in the midst of the valley, have chariots of iron.
17 Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
And Josue said to the house of Joseph, to Ephraim and Manasses: Thou art a great people, and of great strength, thou shalt not have one lot only:
18 dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”
But thou shalt pass to the mountain, and shalt cut down the wood, and make thyself room to dwell in: and mayst proceed farther, when thou hast destroyed the Chanaanites, who as thou sayest have iron chariots, and are very strong.

< Yoswa 17 >