< Yoswa 14 >

1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
Ce sont ici [les terres] que les enfants d'Israël eurent pour héritage au pays de Canaan, qu'Eléazar le Sacrificateur, et Josué, fils de Nun, et les chefs des pères des Tribus des enfants d'Israël leur partagèrent en héritage.
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
Selon le sort de leur héritage, comme l'Eternel l'avait commandé par le moyen de Moïse, [savoir] à neuf Tribus, et à la moitié d'une Tribu.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
Car Moïse avait donné un héritage à deux Tribus, et à la moitié d'une Tribu au delà du Jourdain, mais il n'avait point donné d'héritage parmi eux aux Lévites.
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
Parce que les enfants de Joseph, [savoir], Manassé et Ephraïm, faisaient deux Tribus; et on ne donna point de part aux Lévites dans le pays, excepté les villes pour y habiter avec leurs fauxbourgs pour leurs troupeaux, et pour [le reste de] leur bien.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Les enfants d'Israël firent comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse, et ils partagèrent la terre.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
Or les enfants de Juda vinrent à Josué en Guilgal; et Caleb fils de Jéphunné Kénizien, lui dit: Tu sais la parole que l'Eternel a dite de moi, et de toi, à Moïse homme de Dieu, en Kadès-barné.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
J'étais âgé de quarante ans quand Moïse serviteur de l'Eternel m'envoya de Kadès-barné pour reconnaître le pays, et je lui rapportai la chose comme elle était en mon cœur.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
Et mes frères qui étaient montés avec moi, faisaient fondre le cœur du peuple; mais je persévérai à suivre l'Eternel mon Dieu.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
Et Moïse jura en ce jour-là disant: Si la terre sur laquelle ton pied a marché n'est à toi en héritage, et à tes enfants pour jamais; parce que tu as persévéré à suivre l'Eternel mon Dieu.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
Or maintenant voici, l'Eternel m'a fait vivre selon qu'il en avait parlé; il y a déjà quarante-cinq ans que l'Eternel prononça cette parole à Moïse, lorsque Israël marchait par le désert, et maintenant voici, je suis aujourd'hui âgé de quatre-vingt et cinq ans.
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
Et [je] suis encore aujourd'hui aussi fort que j'étais le jour que Moïse m'envoya, et j'ai maintenant la même force que j'avais alors pour le combat, et pour aller et venir.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
Maintenant donc donne-moi cette montagne, de laquelle l'Eternel parla en ce jour-là; car tu entendis en ce jour-là que les Hanakins y habitent, et qu'il y a de grandes villes fortes; peut-être que l'Eternel sera avec moi, et je les déposséderai, comme l'Eternel en a parlé.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
Josué donc le bénit, et donna Hébron en héritage à Caleb, fils de Jéphunné.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
C'est pourquoi Hébron fut à Caleb, fils de Jéphunné Kénizien, en héritage jusqu'à ce jour, parce qu'il avait persévéré à suivre l'Eternel, le Dieu d'Israël.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
Or le nom d'Hébron était auparavant Kirjath-Arbah, et [Arbah] avait été un fort grand homme entre les Hanakins. Et le pays fut tranquille sans avoir guerre.

< Yoswa 14 >