< Yoswa 13 >

1 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
I gdy Jozue zestarzał się i był w podeszłym wieku, PAN powiedział do niego: Zestarzałeś się i posunąłeś się w latach, a pozostało jeszcze dużo ziemi do zdobycia.
2 “Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
Oto ziemia, która pozostała: wszystkie okręgi Filistynów i Geszurytów;
3 kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
Od Szichoru, który jest naprzeciw Egiptu, aż do granicy Akaronu na północy – [jest to ziemia] przynależąca do Kananejczyków, pięciu książąt filistyńskich: z Gazy, Aszdodu, Aszkelonu, Gat i Ekronu, oraz Awwici;
4 Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
Od południa: cała ziemia Kananejczyków oraz Meara, która należy do Sydończyków, aż do Afek [i] aż do granicy Amorytów;
5 Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
I ziemia Gibilitów i cały Liban na wschodzie, od Baal-Gad pod górę Hermon, aż do wejścia do Chamat.
6 “Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
Wszystkich mieszkańców gór od Libanu aż do Misrefot-Maim [i] wszystkich Sydończyków wypędzę przed synami Izraela. Tylko podziel ją losem między Izraelitów jako dziedzictwo, tak jak ci rozkazałem.
7 Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
Rozdziel więc teraz tę ziemię jako dziedzictwo dziewięciu pokoleniom i połowie pokolenia Manassesa;
8 Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
Gdyż z drugą [połową] Rubenici i Gadyci otrzymali już swoje dziedzictwo, które dał im Mojżesz za Jordanem na wschodzie, jak przydzielał im Mojżesz, sługa PANA;
9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
Od Aroeru, leżącego nad brzegiem rzeki Arnon, i od miasta, które jest w środku rzeki, wraz z całą równiną Medeby aż do Dibonu;
10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
I wszystkie miasta Sichona, króla Amorytów, który królował w Cheszbonie, aż do granicy synów Ammona;
11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
Także Gilead i obszar Geszurytów i Maakatytów, całą górę Hermon i cały Baszan aż do Salka;
12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
Całe królestwo Oga w Baszanie, który królował w Asztarot i w Edrei; był on ostatnim z Refaitów, których Mojżesz pobił i wypędził.
13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
Lecz synowie Izraela nie wypędzili Geszurytów i Maakatytów, dlatego Geszuryci i Maakatyci mieszkają pośród Izraelitów do dziś.
14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
Tylko pokoleniu Lewiego nie dał dziedzictwa; ofiary spalane dla PANA, Boga Izraela, są jego dziedzictwem, jak mu [Bóg] powiedział.
15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
Mojżesz dał więc pokoleniu synów Rubena [dziedzictwo] według ich rodzin.
16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
Ich granica była od Aroeru, leżącego nad brzegiem rzeki Arnon, i od miasta, które jest w środku rzeki, wraz z całą równiną ku Medebie;
17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
Cheszbon i wszystkie przyległe do niego miasta, które były na równinie: Dibon, Bamot-Baal i Bet-Baal-Meon;
18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
Jahaza, Kedemot i Mefaat;
19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
Kiriataim, Sibma i Seret-Haszszachar na górze w dolinie;
20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
Bet-Peor, Aszdod-Pisga i Bet-Jeszimot.
21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
I wszystkie miasta na równinie oraz całe królestwo Sichona, króla Amorytów, który królował w Cheszbonie, a którego Mojżesz zabił tak jak książąt Midianu: Ewi, Rekem, Sur, Chur, Reba, książęta Sichona zamieszkali w [tej] ziemi.
22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
I wróżbitę Balaama, syna Beora, wraz z innymi zabitymi synowie Izraela zabili mieczem.
23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
Granicą synów Rubena był Jordan ze [swymi] granicami. Oto dziedzictwo synów Rubena według ich rodzin, miast i przyległych do nich wsi.
24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
Mojżesz dał też [dziedzictwo] pokoleniu Gada, synom Gada według ich rodzin.
25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
A ich granice obejmowały Jazer i wszystkie miasta Gileadu oraz połowę ziemi synów Ammona aż do Aroeru [leżącego] naprzeciw Rabby;
26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
I od Cheszbonu aż do Ramat-Mispa i Betonim oraz od Machanaim aż do granicy Debiru.
27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
W dolinie zaś: Bet-Haram, Bet-Nimra, Sukkot i Safon, resztę królestwa Sichona, króla Cheszbonu, Jordan i [jego] pogranicze aż do końca morza Kinneret po wschodniej stronie Jordanu.
28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
Oto dziedzictwo synów Gada według ich rodzin, miast i przyległych do nich wsi.
29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
Mojżesz dał też [posiadłość] połowie pokolenia Manassesa; przypadła ona połowie pokolenia synów Manassesa według ich rodzin.
30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
Ich granica była od Machanaim, obejmowała cały Baszan [i] całe królestwo Oga, króla Baszanu oraz wszystkie wsie Jaira, które są w Baszanie, sześćdziesiąt miast.
31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
Połowę Gileadu, Asztarot i Erdei, miasta królestwa Oga w Baszanie, [dał] synom Makira, syna Manassesa, a ściśle – połowie synów Makira według ich rodzin.
32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
Oto [posiadłości], które Mojżesz podzielił na polach Moabu za Jordanem, [naprzeciw] Jerycha na wschodzie.
33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.
Lecz pokoleniu Lewiego Mojżesz nie dał dziedzictwa, gdyż PAN, Bóg Izraela, sam [jest] ich dziedzictwem, jak im to powiedział.

< Yoswa 13 >