< Yoswa 13 >

1 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
Josue was eld and of greet age; and the Lord seide to him, Thou hast woxe eld, and art of long tyme; and largeste lond is left, which is not yit departid bi lot;
2 “Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
that is, al Galile, Filistiym, and al Gessuri,
3 kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
fro the troblid flood that moistith Egipt, `til to the termes of Acaron ayenus the north; the lond of Chanaan, which is departid `in to fyue litle kyngis of Filistym, of Gaza, and of Azotus, of Ascolon, of Geth, and of Accaron.
4 Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
Forsothe at the south ben Eueis, al the lond of Canaan, and Maara of Sidonyes, `til to Affetha, and to the termes of Amorrei, and the coostis of hym;
5 Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
and the cuntrei of Liban ayens the eest, fro Baalgath, vndur the hil of Hermon, til thou entrist into Emath,
6 “Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
of alle men that dwelliden in the hil, fro the Liban `til to the watris of Masserephoth, and alle men of Sidon; Y am, that schal do awei hem fro the face of the sones of Israel; therfor come it in to the part of eritage of Israel, as Y comaundide to thee.
7 Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
And thou now departe the lond in to possessioun to the nyne lynagis, and to the half lynage of Manasses,
8 Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
with which lynage Ruben and Gad weldiden the lond, which lond Moises, the `seruaunt of the Lord, yaf to hem biyende the flowyngis of Jordan, at the eest coost;
9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
fro Aroer, which is set in the brynke of the stronde of Arnon, in the middis of the valei, and alle the feeldi places of Medaba,
10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
`til to Dibon, and alle the citees of Seon, kyng of Amorreis, that regnyde in Esebon, `til to the termes of the sones of Amon,
11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
and of Galaad, and to the termes of Gessuri, and of Machati, and al the hil of Hermon, and al Basan, `til to Salecha;
12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
al the rewme of Og in Basan, that regnede in Astoroth, and in Edraym; `he was of the relikis of Rafaym, `that is, of giauntis; and Moises smoot hem and dide awey hem.
13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
And the sones of Israel nolden destrye Gessurri and Machati; and thei dwelliden in the myddis of Israel, `til in to present dai.
14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
Sotheli he yaf not possessioun to the lynage of Leuy, but sacrifices, and slayn sacrifices of the Lord God of Israel; that is `his eritage, as God spak to hym.
15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
Therfor Moises yaf possessioun to the lynage of the sones of Ruben, bi her kynredis;
16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
and `the term of hem was fro Aroer, which is set in the brenke of the stronde of Arnon, and in the myddil valei of the same stronde, al the pleyn that ledith to Medaba,
17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
and Esebon, and alle the townes of tho, that ben in the feeldi places; and Dibon, and Baal Bamoth, and the citee of Baal Meon,
18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
and Gesa, and Sedymoth, and Mephe,
19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
and Cariathaym, and Sabana, and Sarathaphar, in the hil of the valey of Betheroeth,
20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
and of Asedoch, Phasca, and Bethaissymoth;
21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
alle the feeldi citees, and alle the rewmes of Seon, kyng of Amorrey, that regnede in Esebon, whom Moyses smoot, with hise princes, Madian, Euey and Recten, and Sur, and Hur, and Rebee, duykis of Seon, enhabiters of the lond.
22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
And the sones of Israel killiden bi swerd Balaam, the fals diuynour, the sone of Beor, with othere men slayn.
23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
And the terme of the sones of Ruben was maad the flood of Jordan; this is the possessioun of Rubenytis bi her kynredis of citees and of townes.
24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
And Moises yaf to the lynage of Gad, and to the sones therof, bi her kynredis, possessioun, of which this is departyng;
25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
he yaf the termes of Jazer, and alle the citees of Galaad, and the half part of the lond of the sones of Amon, `til to Aroer which is ayens Tabba;
26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
and fro Esebon `til to Ramoth of Masphe, and Bethamyn, and Manayn, `til to the termes of Dabir;
27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
and in the valei he yaf Betharan, and Bethneuar, and Socoth, and Saphan, the tother part of the rewme of Seon, kyng of Esebon; and the ende of this is Jordan, `til to the laste part of the see of Cenereth ouer Jordan, at the eest coost.
28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
This is the possessioun of the sones of Gad, bi her meynees, the citees and townes of tho.
29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
He yaf also possessioun to the half lynage of Manasses, and to hise sones, bi her kynredis,
30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
of which possessioun this is the bigynnyng; he yaf Ammaym, and al Basan, and alle the rewmes of Og, kyng of Basan, and alle the townes of Jair, that ben in Basan, sixti citees;
31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
and half the part of Galaad, and Astoroth, and Edray, the citees of the rewme of Og, kyng of Basan; to the sones of Machir, sones of Manasses, and to half the part of the sones of Machir, bi her kynredis.
32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
Moises departide this possessioun in the feeldi placis of Moab ouer Jordan, ayens Jericho, at the eest coost.
33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.
Forsothe he yaf not possessioun to the lynage of Leuy; for the Lord God himself of Israel is the possessioun of Leuy, as the Lord spak to hym.

< Yoswa 13 >