< Yoswa 13 >

1 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
And Joshua [was] old and very advanced in years; and the Lord said to Joshua, You are advanced in years, and there is much land left to inherit.
2 “Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
And this [is] the land that is left: the borders of the Phylistines, the Gesirite, and the Chananite,
3 kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
from the wilderness before Egypt, as far as the borders of Accaron on the left of the Chananites [the land] is reckoned to the five principalities of the Phylistines, to the inhabitant of Gaza, and of Azotus, and of Ascalon, and of Geth, and of Accaron, and to the Evite;
4 Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
from Thaeman even to all the land of Chanaan before Gaza, and the Sidonians as far as Aphec, as far as the borders of the Amorites.
5 Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
And all the land of Galiath of the Phylistines, and all Libanus eastward from Galgal, under the mountain Aermon as far as the entering in of Emath;
6 “Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
every one that inhabits the hill country from Libanus as far as Masereth Memphomaim. All the Sidonians, I will destroy them from before Israel; but do you give them by inheritance to Israel, as I charged you.
7 Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
And now divide this land by lot to the nine tribes, and to the half tribe of Manasse.
8 Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
From Jordan to the great sea westward you shall give it [them]: the great sea shall be the boundary. [But] to the two tribes and to the half tribe of Manasse, to Ruben and to Gad Moses gave [an inheritance] beyond Jordan: Moses the servant of the Lord gave [it] to them eastward,
9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
from Aroer, which is on the bank of the brook of Arnon, and the city in the midst of the valley, and all Misor from Maedaban.
10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
All the cities of Seon king of the Amorites, who reigned from Esebon to the coasts of the children of Ammon;
11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
and the region of Galaad, and the borders of the Gesirites and the Machatites, the whole mount of Aermon, and all the land of Basan to Acha.
12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
All the kingdom of Og in the region of Basan, who reigned in Astaroth and in Edrain: he was left of the giants; and Moses struck him, and destroyed him.
13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
But the children of Israel destroyed not the Gesirite and the Machatite and the Chananite; and the king of the Gesiri and the Machatite lived among the children of Israel until this day.
14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
Only no inheritance was given to the tribe of Levi: the Lord God of Israel, he [is] their inheritance, as the Lord said to them; and this [is] the division which Moses made to the children of Israel in Araboth Moab, on the other side of Jordan, by Jericho.
15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
And Moses gave the land to the tribe of Ruben according to their families.
16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
And their borders were from Aroer, which is opposite the brook of Arnon, and [theirs is] the city that is in the valley of Arnon; and all Misor,
17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
to Esebon, and all the cities in Misor, and Daebon, and Baemon-Baal, and the house of Meelboth;
18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
and Basan, and Bakedmoth, and Maephaad,
19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
and Kariathaim, and Sebama, and Serada, and Sion in mount Enab;
20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
and Baethphogor, and Asedoth Phasga, and Baetthasinoth,
21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
and all the cities of Misor, and all the kingdom of Seon king of the Amorites, whom Moses struck, even him and the princes of Madian, and Evi, and Roboc, and Sur, and Ur, and Robe prince of the spoils of Sion, and the inhabitants of Sion.
22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
And Balaam the son of Baeor the prophet they killed in the battle.
23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
And the borders of Ruben were—[even] Jordan [was the] boundary; this [is] the inheritance of the children of Ruben according to their families, [these were] their cities and their villages.
24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
And Moses gave inheritance to the sons of Gad according to their families.
25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
And their borders were Jazer, all the cities of Galaad, and half the land of the children of Ammon to Araba, which is before Arad.
26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
And from Esebon to Araboth by Massepha, and Botanim, and Maan to the borders of Daebon,
27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
and Enadom, and Othargai, and Baenthanabra, and Soccotha, and Saphan, and the rest of the kingdom of Sean king of Esebon: and Jordan shall be the boundary as far as part of the sea of Chenereth beyond Jordan eastward.
28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
This [is] the inheritance of the children of Gad according to their families and according to their cities: according to their families they will turn their backs before their enemies, because their cities and their villages were according to their families.
29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
And Moses gave to half the tribe of Manasse according to their families.
30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
And their borders were from Maan, and all the kingdom of Basan, and all the kingdom of Og king of Basan, and all the villages of Jair, which are in the region of Basan, sixty cities:
31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
and the half of Galaad, and in Astaroth, and in Edrain, royal cities of Og in the land of Basan, [Moses gave] to the sons of Machir the sons of Manasse, even to the half-tribe sons of Machir the sons of Manasse, according to their families.
32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
These [are] they whom Moses caused to inherit beyond Jordan in Araboth Moab, beyond Jordan by Jericho eastward.
33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Yoswa 13 >