< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
I zamoli se Jona Gospodu Bogu svojemu iz trbuha ribljega,
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
I reèe: zavapih u nevolji svojoj ka Gospodu, i usliši me; iz utrobe grobne povikah, i ti èu glas moj. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Jer si me bacio u dubine, u srce moru, i voda me opteèe; sve poplave tvoje i vali tvoji prelaziše preko mene.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
I rekoh: odbaèen sam ispred oèiju tvojih; ali æu još gledati svetu crkvu tvoju.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Optekoše me vode do duše, bezdana me opkoli, sita omota mi se oko glave.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
Sidoh do krajeva gorskih, prijevornice zemaljske nada mnom su dovijeka; ali ti izvadi život moj iz jame, Gospode Bože moj.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Kad nestajaše duše moje u meni, pomenuh Gospoda, i molitva moja doðe k tebi, u svetu crkvu tvoju.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Koji drže lažne taštine, ostavljaju svoju milost.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
A ja æu ti glasom zahvalnijem prinijeti žrtvu, ispuniti što sam zavjetovao; spasenje je u Gospoda.
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
I Gospod zapovjedi ribi, te izbljuva Jonu na zemlju.

< Yona 2 >